< Proverbs 15 >
1 A soft answer turns back fury, And a grievous word raises up anger.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 The tongue of the wise makes knowledge good, And the mouth of fools utters folly.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 The eyes of YHWH are in every place, Watching the evil and the good.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 A healed tongue [is] a tree of life, And perverseness in it—a breach in the spirit.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 A fool despises the instruction of his father, And whoever is regarding reproof is prudent.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 Abundant strength [is in] the house of the righteous, And in the increase of the wicked—trouble.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 The lips of the wise scatter knowledge, And the heart of fools [is] not right.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 The sacrifice of the wicked [is] an abomination to YHWH, And the prayer of the upright [is] His delight.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 The way of the wicked [is] an abomination to YHWH, And He loves whoever is pursuing righteousness.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 Discipline [is] grievous to him who is forsaking the path, Whoever is hating reproof dies.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Sheol and destruction [are] before YHWH, Surely also the hearts of the sons of men. (Sheol )
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
12 A scorner does not love his reprover, He does not go to the wise.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 A joyful heart makes the face glad, And the spirit is struck by grief of heart.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 The heart of the intelligent seeks knowledge, And the mouth of fools enjoys folly.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 All the days of the afflicted [are] evil, And gladness of heart [is] a perpetual banquet.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Better [is] a little with the fear of YHWH, Than much treasure, and tumult with it.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Better [is] an allowance of green herbs and love there, Than a fatted ox, and hatred with it.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 A man of fury stirs up contention, And the slow to anger appeases strife.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 The way of the slothful [is] as a hedge of briers, And the path of the upright is raised up.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 A wise son makes a father glad. And a foolish man is despising his mother.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 Folly is joy to one lacking heart, And a man of intelligence directs [his] going.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 The making void of purposes [is] without counsel, And in a multitude of counselors it is established.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 Joy [is] to a man in the answer of his mouth, And a word in its season—how good!
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 A path of life [is] on high for the wise, To turn aside from Sheol beneath. (Sheol )
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
25 YHWH pulls down the house of the proud, And He sets up the border of the widow.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 Thoughts of wickedness [are] an abomination to YHWH, And sayings of pleasantness [are] pure.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 A dishonest gainer is troubling his house, And whoever is hating gifts lives.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 The heart of the righteous meditates to answer, And the mouth of the wicked utters evil things.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 YHWH [is] far from the wicked, And He hears the prayer of the righteous.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 The light of the eyes makes the heart glad, A good report makes the bone fat.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 An ear that is hearing the reproof of life Lodges among the wise.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 Whoever is refusing instruction is despising his soul, And whoever is hearing reproof Is getting understanding.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 The fear of YHWH [is] the instruction of wisdom, And humility [is] before honor!
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.