< Proverbs 12 >

1 Whoever is loving instruction, is loving knowledge, And whoever is hating reproof [is] brutish.
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
2 The good brings forth favor from YHWH, And the man of wicked schemes He condemns.
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
3 A man is not established by wickedness, And the root of the righteous is not moved.
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
4 A virtuous woman [is] a crown to her husband, And as rottenness in his bones [is] one causing shame.
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
5 The thoughts of the righteous [are] justice, The counsels of the wicked—deceit.
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
6 The words of the wicked [are]: “Lay [in] wait for blood,” And the mouth of the upright delivers them.
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
7 Overthrow the wicked, and they are not, And the house of the righteous stands.
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
8 A man is praised according to his wisdom, And the perverted of heart becomes despised.
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
9 Better [is] the lightly esteemed who has a servant, Than the self-honored who lacks bread.
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
10 The righteous knows the life of his beast, And the mercies of the wicked [are] cruel.
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
11 Whoever is tilling the ground is satisfied [with] bread, And whoever is pursuing vanities is lacking heart,
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
12 The wicked has desired the net of evildoers, And the root of the righteous gives.
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
13 The snare of the wicked [is] in transgression of the lips, And the righteous goes out from distress.
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
14 One [is] satisfied [with] good from the fruit of the mouth, And the deed of man’s hands returns to him.
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
15 The way of a fool [is] right in his own eyes, And whoever is listening to counsel [is] wise.
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
16 The fool—his anger is known in a day, And the prudent is covering shame.
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
17 Whoever utters faithfulness declares righteousness, And a false witness—deceit.
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
18 A rash speaker is like piercings of a sword, And the tongue of the wise is healing.
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
19 The lip of truth is established forever, And a tongue of falsehood for a moment.
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
20 Deceit [is] in the heart of those devising evil, But for counselors of peace—joy.
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
21 No iniquity is desired by the righteous, And the wicked have been full of evil.
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
22 Lying lips [are] an abomination to YHWH, And steadfast doers [are] his delight.
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
23 A prudent man is concealing knowledge, And the heart of fools proclaims folly.
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
24 The hand of the diligent rules, And slothfulness becomes tributary.
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
25 Sorrow in the heart of a man bows down, And a good word makes him glad.
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
26 The righteous searches his companion, And the way of the wicked causes them to err.
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
27 The slothful does not roast his game, And the wealth of a diligent man is precious.
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
28 In the path of righteousness [is] life, And in the way of [that] path [is] no death!
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< Proverbs 12 >