< Numbers 18 >

1 And YHWH says to Aaron, “You, and your sons, and the house of your father with you, bear the iniquity of the sanctuary; and you and your sons with you bear the iniquity of your priesthood;
Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu.
2 and also your brothers, the tribe of Levi, the tribe of your father, bring near with you, and they are joined to you, and serve you, even you and your sons with you, before the Tent of the Testimony.
Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.
3 And they have kept your charge, and the charge of all the tent; only, they do not come near to the vessels of the holy place and to the altar, and they do not die, either they or you;
Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe.
4 and they have been joined to you and have kept the charge of the Tent of Meeting for all the service of the tent; and a stranger does not come near to you;
Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.
5 and you have kept the charge of the holy place and the charge of the altar, and there is no more wrath against the sons of Israel.
“Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.
6 And I, behold, have taken your brothers the Levites from the midst of the sons of Israel; they are a gift given to you by YHWH to do the service of the Tent of Meeting;
Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
7 and you and your sons with you keep your priesthood for everything of the altar and within the veil, and you have served; I make your priesthood a gift [for] service; and the stranger who is coming near is put to death.”
Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.
8 And YHWH speaks to Aaron: “And I, behold, have given to you the charge of My raised-offerings, of all the hallowed things of the sons of Israel—I have given them to you and to your sons for the anointing, by a continuous statute.
“Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse.
9 This is yours from the most holy things, from the fire: all their offering, of all their present, and of all their sin-offering, and of all their guilt-offering, which they give back to Me, is most holy to you and to your sons;
Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna.
10 you eat it among the most holy things; every male eats it; it is holy to you.
Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.
11 And this [is] yours: the raised-offering of their gift, with all the wave-offerings of the sons of Israel; I have given them to you, and to your sons, and to your daughters with you, by a continuous statute; every clean one in your house eats it;
“Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.
12 all the best of the oil, and all the best of the new wine, and wheat—their first-[fruits] which they give to YHWH—I have given them to you.
“Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo.
13 The first-fruits of all that [is] in their land, which they bring to YHWH, are yours; every clean one in your house eats it;
Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.
14 every devoted thing in Israel is yours;
“Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako.
15 everyone opening a womb of all flesh which they bring near to YHWH, among man and among beast, is yours; only, you certainly ransom the firstborn of man, and you ransom the firstling of the unclean beast.
Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa.
16 And their ransomed ones from a son of a month, you ransom with your valuation [for] five shekels of silver, by the shekel of the holy place; it [is] twenty gerahs.
Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.
17 Only, the firstling of a cow, or the firstling of a sheep, or the firstling of a goat, you do not ransom, they [are] holy: you sprinkle their blood on the altar, and you make incense of their fat [as] a fire-offering of refreshing fragrance to YHWH;
“Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
18 and their flesh is yours, as the breast of the wave-offering and as the right leg are yours.
Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako.
19 All the raised-offerings of the holy things, which the sons of Israel lift up to YHWH, I have given to you, and to your sons, and to your daughters with you, by a continuous statute—a covenant of salt; it [is] continuous before YHWH to you and to your seed with you.”
Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”
20 And YHWH says to Aaron, “You do not inherit in their land, and you do not have a portion in their midst: I [am] your portion and your inheritance in the midst of the sons of Israel;
Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.
21 and to the sons of Levi, behold, have given all the tenth in Israel for inheritance in exchange for their service which they are serving—the service of the Tent of Meeting.
“Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano.
22 And the sons of Israel no longer come near to the Tent of Meeting, to bear sin, to die,
Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa.
23 and the Levites have done the service of the Tent of Meeting, and they bear their iniquity; [it is] a continuous statute throughout your generations that they have no inheritance in the midst of the sons of Israel;
Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli.
24 but the tithe of the sons of Israel which they lift up to YHWH, a raised-offering, I have given to the Levites for inheritance; therefore I have said of them, They have no inheritance in the midst of the sons of Israel.”
Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’”
25 And YHWH speaks to Moses, saying,
Yehova anati kwa Mose,
26 “And you speak to the Levites, and you have said to them: When you take the tithe from the sons of Israel which I have given to you from them for your inheritance, then you have lifted up the raised-offering of YHWH from it, a tithe of the tithe;
“Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova.
27 and your raised-offering has been reckoned to you as grain from the threshing-floor and as the fullness from the wine-vat;
Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa.
28 so you lift up—you also—the raised-offering of YHWH from all your tithes which you receive from the sons of Israel; and you have given the raised-offering of YHWH from it to Aaron the priest;
Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe.
29 out of all your gifts you lift up every raised-offering of YHWH, out of all its fat—its hallowed part—out of it.
Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’
30 And you have said to them: In your lifting up its fat out of it, then it has been reckoned to the Levites as increase of a threshing-floor and as increase of a wine-vat;
“Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa.
31 and you have eaten it in every place, you and your households, for it [is] your hire in exchange for your service in the Tent of Meeting;
Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano.
32 and you bear no sin for it in your lifting up its fat out of it, but you do not defile the holy things of the sons of Israel, and you do not die.”
Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’”

< Numbers 18 >