< Numbers 16 >

1 And Korah, son of Izhar, son of Kohath, son of Levi, takes both Dathan and Abiram sons of Eliab, and On son of Peleth, sons of Reuben,
Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
2 and they rise up before Moses with men of the sons of Israel, two hundred and fifty princes of the congregation, called of the convention, men of renown,
ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
3 and they are assembled against Moses and against Aaron, and say to them, “Enough of you! For all the congregation—all of them [are] holy, and YHWH [is] in their midst; and why do you lift yourselves up above the assembly of YHWH?”
Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
4 And Moses hears, and falls on his face,
Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
5 and he speaks to Korah and to all his congregation, saying, “Indeed, [in the] morning YHWH may cause [you] to know those who are His and him who is holy, and has brought [him] near to Him; even him whom He fixes on He brings near to Him.
Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
6 Do this: take censers for yourselves—Korah and all his company—
Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
7 and put fire in them and put incense on them before YHWH tomorrow, and it has been, the man whom YHWH chooses, he [is] the holy one—enough of you, sons of Levi!”
ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
8 And Moses says to Korah, “Now hear, sons of Levi;
Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
9 is it little to you that the God of Israel has separated you from the congregation of Israel to bring you near to Himself, to do the service of the Dwelling Place of YHWH, and to stand before the congregation to serve them?
Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
10 Indeed, He brings you near, and all your brothers, the sons of Levi, with you—and you have also sought the priesthood!
Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
11 Therefore, you and all your congregation are meeting against YHWH; and Aaron, what [is] he, that you murmur against him?”
Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
12 And Moses sends to call for Dathan and for Abiram, sons of Eliab, and they say, “We do not come up!
Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
13 Is it little that you have brought us up out of a land flowing with milk and honey, to put us to death in a wilderness, that you also certainly make yourself prince over us?
Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
14 Indeed, you have not brought us into a land flowing with milk and honey, nor do you give an inheritance of field and vineyard to us; do you pick out the eyes of these men? We do not come up!”
Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
15 And it is very displeasing to Moses, and he says to YHWH, “Do not turn to their present; I have not taken one donkey from them, nor have I afflicted one of them.”
Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
16 And Moses says to Korah, “You and all your congregation, be [present] before YHWH—you, and they, and Aaron—tomorrow;
Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
17 and let each take his censer and you have put incense on them, and each has brought his censer near before YHWH—two hundred and fifty censers; indeed, you and Aaron, each [with] his censer.”
Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
18 And they each take his censer, and put fire on them, and lay incense on them, and they stand at the opening of the Tent of Meeting with Moses and Aaron.
Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
19 And Korah assembles all the congregation against them at the opening of the Tent of Meeting, and the glory of YHWH is seen by all the congregation.
Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
20 And YHWH speaks to Moses and to Aaron, saying,
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
21 “Be separated from the midst of this congregation, and I consume them in a moment”;
“Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
22 and they fall on their faces, and say, “God, God of the spirits of all flesh—one man sins, and are You angry against all the congregation?”
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
23 And YHWH speaks to Moses, saying,
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
24 “Speak to the congregation, saying, Go up from around the dwelling place of Korah, Dathan, and Abiram.”
“Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
25 And Moses rises, and goes to Dathan and Abiram, and [the] elderly of Israel go after him,
Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
26 and he speaks to the congregation, saying, “Now turn aside from the tents of these wicked men, and do not come against anything that they have, lest you are consumed in all their sins.”
Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
27 And they go up from the dwelling place of Korah, Dathan, and Abiram, from all around, and Dathan and Abiram have come out, standing at the opening of their tents, with their wives, and their sons, and their infants.
Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
28 And Moses says, “By this you know that YHWH has sent me to do all these works, that [they are] not from my own heart;
Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
29 if these die according to the death of all men, or the charge of all men is charged on them, YHWH has not sent me;
Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
30 but if YHWH does a strange thing, and the ground has opened her mouth and swallowed them and all that they have, and they have gone down alive to Sheol, then you have known that these men have despised YHWH.” (Sheol h7585)
Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
31 And it comes to pass at his finishing speaking all these words, that the ground which [is] under them cleaves,
Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
32 and the earth opens her mouth and swallows them, and their houses, and all the men who [are] for Korah, and all the goods,
ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
33 and they go down—they and all that they have—alive to Sheol, and the earth closes over them, and they perish from the midst of the assembly; (Sheol h7585)
Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
34 and all Israel who [are] around them have fled at their voice, for they said, “Lest the earth swallow us”;
Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
35 and fire has come out from YHWH and consumes the two hundred and fifty men bringing the incense near.
Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
36 And YHWH speaks to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
37 “Say to Eleazar son of Aaron the priest to lift up the censers from the midst of the burning and scatter the fire away, for they have been hallowed.
“Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
38 [As for] the censers of these sinners against their own souls, indeed, they have made them [into] spread-out plates [for] a covering for the altar, for they have brought them near before YHWH, and they are hallowed; and they become a sign to the sons of Israel.”
Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
39 And Eleazar the priest takes the bronze censers which they who are burned had brought near, and they spread them out [for] a covering for the altar—
Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
40 a memorial to the sons of Israel, so that a stranger who is not of the seed of Aaron does not draw near to make incense before YHWH, and is not as Korah and as his congregation, as YHWH has spoken by the hand of Moses to him.
monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
41 And on the next day all the congregation of the sons of Israel murmurs against Moses and against Aaron, saying, “You have put the people of YHWH to death.”
Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
42 And it comes to pass, in the congregation being assembled against Moses and against Aaron, that they turn toward the Tent of Meeting, and behold, the cloud has covered it and the glory of YHWH is seen;
Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
43 and Moses comes—Aaron also—to the front of the Tent of Meeting.
Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
44 And YHWH speaks to Moses, saying,
ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
45 “Get up from the midst of this congregation, and I consume them in a moment”; and they fall on their faces,
“Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
46 and Moses says to Aaron, “Take the censer and put fire on it from off the altar, and place incense, and go quickly to the congregation and make atonement for them, for the wrath has gone out from the presence of YHWH—the plague has begun.”
Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
47 And Aaron takes [it] as Moses has spoken, and runs to the midst of the assembly, and behold, the plague has begun among the people; and he gives the incense, and makes atonement for the people,
Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
48 and stands between the dead and the living, and the plague is restrained;
Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
49 and those who die by the plague are fourteen thousand and seven hundred, apart from those who die for the matter of Korah;
Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
50 and Aaron turns back to Moses, to the opening of the Tent of Meeting, and the plague has been restrained.
Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.

< Numbers 16 >