< Nehemiah 10 >
1 And over those sealed [are] Nehemiah the Tirshatha, son of Hachaliah, and Zidkijah,
Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
2 Seraiah, Azariah, Jeremiah,
Seraya, Azariya, Yeremiya
3 Pashhur, Amariah, Malchijah,
Pasuri, Amariya, Malikiya,
4 Huttush, Shebaniah, Malluch,
Hatusi, Sebaniya, Maluki,
5 Harim, Meremoth, Obadiah,
Harimu, Meremoti, Obadiya,
6 Daniel, Ginnethon, Baruch,
Danieli, Ginetoni, Baruki,
7 Meshullam, Abijah, Mijamin,
Mesulamu, Abiya, Miyamini
8 Maaziah, Bilgai, Shemaiah; these [are] the priests.
Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
9 And the Levites: both Jeshua son of Azaniah, Binnui of the sons of Henadad, Kadmiel;
Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
10 and their brothers: Shebaniah, Hodijah, Kelita, Pelaiah, Hanan,
ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
11 Micha, Rehob, Hashabiah,
Mika, Rehobu, Hasabiya,
12 Zaccur, Sherebiah, Shebaniah,
Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
13 Hodijah, Bani, Beninu.
Hodiya, Bani ndi Beninu.
14 Heads of the people: Parosh, Pahath-Moab, Elam, Zatthu, Bani,
Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
16 Adonijah, Bigvai, Adin,
Adoniya, Bigivai, Adini,
17 Ater, Hizkijah, Azzur,
Ateri, Hezekiya, Azuri,
18 Hodijah, Hashum, Bezai,
Hodiya, Hasumu, Bezayi
19 Hariph, Anathoth, Nebai,
Harifu, Anatoti, Nebayi,
20 Magpiash, Meshullam, Hezir,
Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
21 Meshezabeel, Zadok, Jaddua,
Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
22 Pelatiah, Hanan, Anaiah,
Pelatiya, Hanani, Ananiya,
23 Hoshea, Hananiah, Hashub,
Hoseya, Hananiya, Hasubu
24 Hallohesh, Pilha, Shobek,
Halohesi, Piliha, Sobeki,
25 Rehum, Hashabnah, Maaseiah,
Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
26 and Ahijah, Hanan, Anan,
Ahiya, Hanani, Anani,
27 Malluch, Harim, Baanah.
Maluki, Harimu ndi Baana.
28 And the rest of the people, the priests, the Levites, the gatekeepers, the singers, the Nethinim, and everyone who has been separated from the peoples of the lands to the Law of God, their wives, their sons, and their daughters, every knowing intelligent one,
Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
29 are laying hold on their brothers, their majestic ones, and coming into an execration and an oath, to walk in the Law of God, that was given by the hand of Moses, servant of God, and to observe and to do all the commands of YHWH our Lord, and His judgments, and His statutes;
tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
30 and that we do not give our daughters to the peoples of the land, and we do not take their daughters to our sons;
“Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
31 and the peoples of the land who are bringing in the wares and any grain on the Sabbath day to sell, we do not receive of them on the Sabbath, and on a holy day, and we leave the seventh year, and usury on every hand.
“Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
32 And we have appointed for ourselves commands, to put on ourselves the third of a shekel in a year, for the service of the house of our God,
“Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
33 for bread of the arrangement, and the continual present, and the continual burnt-offering of the Sabbaths, of the new moons, for appointed times, and for holy things, and for sin-offerings, to make atonement for Israel, even all the work of the house of our God.
Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
34 And we have caused the lots to fall for the offering of wood, [among] the priests, the Levites, and the people, to bring into the house of our God, by the house of our fathers, at times appointed, year by year, to burn on the altar of our God YHWH, as it is written in the Law,
“Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
35 and to bring in the first-fruits of our ground, and the first-fruits of all fruit of every tree, year by year, to the house of YHWH,
“Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
36 and the firstlings of our sons, and of our livestock, as it is written in the Law, and the firstlings of our herds and our flocks, to bring into the house of our God, to the priests who are ministering in the house of our God.
“Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
37 And the beginning of our dough, and our raised-offerings, and the fruit of every tree, of new wine, and of oil, we bring to the priests, into the chambers of the house of our God, and the tithe of our ground to the Levites; and they—the Levites—have the tithes in all the cities of our tillage;
“Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
38 and the priest, son of Aaron, has been with the Levites in the tithing of the Levites, and the Levites bring up the tithe of the tithe to the house of our God to the chambers, to the treasure-house;
Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
39 for they bring to the chambers—the sons of Israel and the sons of Levi—the raised-offering of the grain, the new wine, and the oil, and there [are] vessels of the sanctuary, and the priests, those ministering, and the gatekeepers, and the singers, and we do not forsake the house of our God.
Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”