< Mark 6 >

1 And He went forth from there, and came to His own country, and His disciples follow Him,
Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
2 and Sabbath having come, He began to teach in the synagogue, and many hearing were astonished, saying, “From where [did] this One [hear] these things? And what [is] the wisdom that was given to Him, that also such mighty works are done through His hands?
Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
3 Is this not the carpenter, the Son of Mary, and brother of James, and Joses, and Judas, and Simon? And are His sisters not here with us?” And they were being stumbled at Him.
Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
4 And Jesus said to them, “A prophet is not without honor, except in his own country, and among his relatives, and in his own house”;
Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
5 and He was not able to do any mighty work there, except having put hands on a few sick, He healed [them];
Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
6 and He wondered because of their unbelief. And He was going around the villages, in a circle, teaching,
Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
7 and He calls near the Twelve, and He began to send them forth two by two, and He was giving them power over the unclean spirits,
Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
8 and He commanded them that they may take nothing for the way, except a staff only—no leather pouch, no bread, no brass in the girdle,
Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
9 but having been shod with sandals, and you may not put on two coats.
Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
10 And He said to them, “Whenever you may enter into a house, remain there until you may depart from there,
Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
11 and as many as may not receive you nor hear you, going out from there, shake off the dust that is under your feet for a testimony to them; [[truly I say to you, it will be more tolerable for Sodom or Gomorrah in [the] day of judgment than for that city.”]]
Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
12 And having gone forth they were preaching that [men] might convert,
Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
13 and they were casting out many demons, and they were anointing many sick with oil, and they were healing [them].
Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
14 And King Herod heard (for His Name became public), and he said, “John the Immerser was raised out of the dead, and because of this the mighty powers are working in him.”
Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
15 Others said, “It is Elijah,” and others said, “It is a prophet, or as one of the prophets.”
Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
16 And Herod having heard, said, “He whom I beheaded—John—this is he; he was raised out of the dead.”
Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
17 For Herod himself, having sent forth, laid hold on John, and bound him in the prison, because of Herodias, the wife of his brother Philip, because he married her,
Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
18 for John said to Herod, “It is not lawful for you to have the wife of your brother”;
Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
19 and Herodias was having a quarrel with him, and was willing to kill him, and was not able,
Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
20 for Herod was fearing John, knowing him [to be] a righteous and holy man, and was keeping watch over him, and having heard him, was doing many things, and hearing him gladly.
chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
21 And a seasonable day having come when Herod on his birthday was making a banquet to his great men, and to the chiefs of thousands, and to the first men of Galilee,
Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
22 and the daughter of that Herodias having come in, and having danced, and having pleased Herod and those dining with him, the king said to the girl, “Ask of me whatever you will, and I will give to you,”
Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
23 and he swore to her, “Whatever you may ask me, I will give to you—to the half of my kingdom.”
Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
24 And she, having gone forth, said to her mother, “What will I ask for myself?” And she said, “The head of John the Immerser”;
Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
25 and having come in immediately with haste to the king, she asked, saying, “I will that you may immediately give me the head of John the Immerser on a plate.”
Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
26 And the king, made very sorrowful because of the oaths and of those reclining with him, would not put her away,
Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
27 and immediately the king having sent a guardsman, commanded his head to be brought,
Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
28 and he having gone, beheaded him in the prison, and brought his head on a plate, and gave it to the girl, and the girl gave it to her mother;
nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
29 and having heard, his disciples came and took up his corpse, and laid it in the tomb.
Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
30 And the apostles are gathered together to Jesus, and they told Him all, and how many things they did, and how many things they taught,
Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
31 and He said to them, “Come yourselves apart to a desolate place, and rest a little,” for those coming and those going were many, and not even to eat had they opportunity,
Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
32 and they went away to a desolate place, in the boat, by themselves.
Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
33 And the multitudes saw them going away, and many recognized Him, and they ran there by land from all the cities, and went before them, and came together to Him,
Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
34 and having come forth, Jesus saw a great multitude, and was moved with compassion on them, that they were as sheep not having a shepherd, and He began to teach many things.
Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
35 And now the hour being advanced, His disciples having come near to Him, say, “The place is desolate, and the hour is now advanced,
Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
36 let them away, that having gone away into the surrounding fields and villages, they may buy loaves for themselves, for they do not have what they may eat.”
Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
37 And He answering said to them, “You give them to eat,” and they say to Him, “Having gone away, may we buy two hundred denarii worth of loaves, and give to them to eat?”
Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
38 And He says to them, “How many loaves do you have? Go and see”; and having known, they say, “Five, and two fishes.”
Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
39 And He commanded them to make all recline in companies on the green grass,
Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
40 and they sat down in squares, by hundreds, and by fifties.
Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
41 And having taken the five loaves and the two fishes, having looked up to the sky, He blessed, and broke the loaves, and was giving [them] to His disciples, that they may set [them] before them, and the two fishes He divided to all,
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
42 and they all ate, and were filled,
Onse anadya ndipo anakhuta,
43 and they took up of broken pieces twelve hand-baskets full, and of the fishes,
ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
44 and those eating of the loaves were about five thousand men.
Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
45 And immediately He constrained His disciples to go into the boat, and to go before [Him] to the other side, to Bethsaida, until He may let the multitude away,
Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
46 and having taken leave of them, He went away to the mountain to pray.
Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
47 And evening having come, the boat was in the midst of the sea, and He alone on the land;
Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
48 and He saw them harassed in the rowing, for the wind was against them, and about the fourth watch of the night He comes to them walking on the sea, and wished to pass by them.
Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
49 And they having seen Him walking on the sea, thought [it] to be an apparition, and cried out,
koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
50 for they all saw Him, and were troubled, and immediately He spoke with them, and says to them, “Take courage! I AM; do not be afraid.”
pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
51 And He went up to them into the boat, and the wind stilled, and greatly out of measure they were amazed in themselves, and were wondering,
Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
52 for they did not understand concerning the loaves, for their heart has been hard.
popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
53 And having passed over, they came on the land of Gennesaret, and drew to the shore,
Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
54 and they having come forth out of the boat, immediately having recognized Him,
Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
55 they ran around through all that surrounding region, and they began to carry around on the pallets those being ill, where they were hearing that He is,
Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
56 and wherever He was going, to villages, or cities, or fields, in the marketplaces they were laying the ailing, and were calling on Him, that they may touch if it were but the fringe of His garment, and as many as were touching Him were saved.
Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.

< Mark 6 >