< Mark 11 >
1 And when they come near to Jerusalem, to Bethphage, and Bethany, to the Mount of Olives, He sends forth two of His disciples,
Atayandikira ku Yerusalemu, anafika ku Betifage ndi Betaniya ku phiri la Olivi. Yesu anatuma awiri a ophunzira ake
2 and says to them, “Go away into the village that is in front of you, and immediately, entering into it, you will find a colt tied, on which no one of men has sat, having loosed it, bring [it]:
nati kwa iwo, “Pitani ku mudzi uli patsogolo panu, ndipo mukamakalowa, mukapeza mwana wabulu atamangiriridwa pamenepo, amene wina aliyense sanakwerepo. Kamumasuleni ndi kubwera naye kuno.
3 and if anyone may say to you, Why do you do this? Say that the LORD has need of it, and immediately He will send it here.”
Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Mukuchita zimenezi chifukwa chiyani?’ Kamuwuzeni kuti, ‘Ambuye akumufuna ndipo akamutumiza kuno msanga.’”
4 And they went away, and found the colt tied at the door outside, by the two ways, and they loose it,
Anapita ndipo anakapeza mwana wabulu ali kunja mu msewu waukulu atamumangirira pa chipata. Pamene anamumasula,
5 and certain of those standing there said to them, “What do you—loosing the colt?”
anthu ena amene anayima pomwepo anafunsa kuti, “Mukuchita chiyani, kumasula mwana wabuluyo?”
6 And they said to them as Jesus commanded, and they permitted them.
Iwo anayankha monga mmene Yesu anawawuzira, ndipo anthu aja anawalola kuti apite.
7 And they brought the colt to Jesus, and cast their garments on it, and He sat on it,
Atafika naye mwana wabulu kwa Yesu, nayika mikanjo yawo pa buluyo, Iye anakwerapo.
8 and many spread their garments in the way, and others were cutting down branches from the trees, and were strewing in the way.
Anthu ambiri anayala mikanjo yawo pa msewu, pamene ena anayala nthambi zomwe anadula mʼminda.
9 And those going before and those following were crying out, saying, “Hosanna! Blessed [is] He who is coming in the Name of the LORD;
Amene anatsogola ndi iwo amene ankatsatira ankafuwula kuti, “Hosana! “Odala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye!”
10 blessed is the coming kingdom, in the Name of the LORD, of our father David; Hosanna in the highest!”
“Odala ndi ufumu umene ukubwera wa abambo athu Davide!” “Hosana Mmwambamwamba!”
11 And Jesus entered into Jerusalem, and into the temple, and having looked around on all things, it being now evening, He went forth to Bethany with the Twelve.
Yesu analowa mu Yerusalemu napita ku Nyumba ya Mulungu. Anayangʼana zonse, koma popeza kuti nthawi inali itapita, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.
12 And on the next day, they having come forth from Bethany, He hungered,
Mmawa mwake pamene amachoka ku Betaniya, Yesu anamva njala.
13 and having seen a fig tree far off having leaves, He came, if perhaps He will find anything in it, and having come to it, He found nothing except leaves, for it was not a time of figs,
Ataonera patali mtengo wamkuyu uli ndi masamba, anapita kuti akaone ngati unali ndi chipatso chilichonse. Atafika, sanapezemo kanthu koma masamba, chifukwa sinali nthawi ya nkhuyu.
14 and Jesus answering said to it, “No longer from you—throughout the age—may any eat fruit”; and His disciples were hearing. (aiōn )
Ndipo Iye anati kwa mtengo, “Palibe amene adzadyenso chipatso kuchokera kwa iwe.” Ndipo ophunzira ake anamva Iye akunena izi. (aiōn )
15 And they come to Jerusalem, and Jesus having gone into the temple, began to cast forth those selling and buying in the temple, and He overthrew the tables of the money-changers and the seats of those selling the doves,
Atafika ku Yerusalemu, Yesu analowa mʼbwalo lakunja la Nyumba ya Mulungu ndipo anayamba kupirikitsa anthu amene amagula ndi kugulitsa mʼmenemo. Anagubuduza matebulo a osintha ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda,
16 and He did not permit that any might carry a vessel through the temple,
ndipo Iye sanalole aliyense kugulitsa malonda mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu.
17 and He was teaching, saying to them, “Has it not been written: My house will be called a house of prayer for all the nations? And you made it a den of robbers!”
Ndipo pamene ankawaphunzitsa, Iye anati, “Kodi sikunalembedwe kuti, ‘Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba ya mapemphero kwa anthu a mitundu yonse?’ Koma inu mwayisandutsa ‘phanga la achifwamba.’”
18 And the scribes and the chief priests heard, and they were seeking how they will destroy Him, for they were afraid of Him, because all the multitude was astonished at His teaching;
Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo anamva izi ndipo anayamba kufuna njira yoti amuphere Iye, pakuti amamuopa, chifukwa gulu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.
19 and when evening came, He was going forth outside the city.
Pofika madzulo, iwo anatuluka mu mzindamo.
20 And in the morning, passing by, they saw the fig tree having been dried up from the roots,
Mmamawa, pamene ankayenda, anaona mtengo wamkuyu uja utafota kuyambira ku mizu.
21 and Peter having remembered says to Him, “Rabbi, behold, the fig tree that You cursed is dried up.”
Petro anakumbukira nati kwa Yesu, “Aphunzitsi, taonani! Mtengo wamkuyu munawutemberera uja wafota!”
22 And Jesus answering says to them, “Have faith from God;
Yesu anayankha kuti, “Khalani ndi chikhulupiriro mwa Mulungu.
23 for truly I say to you that whoever may say to this mountain, Be taken up, and be cast into the sea, and may not doubt in his heart, but may believe that the things that he says come to pass, it will be to him whatever he may say.
Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati wina aliyense angalamule phiri ili kuti, ‘Pita, kadziponye mʼnyanja,’ ndipo wosakayika mu mtima mwake koma kukhulupirira kuti chimene akunena chidzachitika, chidzachitikadi kwa iyeyo.
24 Because of this I say to you, all whatever—praying—you ask, believe that you receive, and it will be to you.
Nʼchifukwa chake ndikukuwuzani kuti chilichonse chimene mupempha mʼpemphero, khulupirirani kuti mwalandira, ndipo chidzakhala chanu.
25 And whenever you may stand praying, forgive, if you have anything against anyone, that your Father who is in the heavens may also forgive you your trespasses;
Pamene muyimirira kupemphera, ngati muli ndi chifukwa ndi wina, mukhululukireni, kuti Atate anu akumwamba akukhululukireni machimo anu.”
26 [[and, if you do not forgive, neither will your Father who is in the heavens forgive your trespasses.”]]
(Koma ngati simukhululukirana, ngakhale Atate anu akumwamba sadzakhululukira machimo anu).
27 And they come again to Jerusalem, and in the temple, as He is walking, there come to Him the chief priests, and the scribes, and the elders,
Iwo anafikanso ku Yerusalemu, ndipo pamene Yesu amayenda mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
28 and they say to Him, “By what authority do You do these things? And who gave You this authority that You may do these things?”
Iwo anafunsa kuti, “Mukuchita izi ndi ulamuliro wanji? Ndipo anakupatsani ulamuliro umenewu ndi ndani?”
29 And Jesus answering said to them, “I will question you—I also—one word; and answer Me, and I will tell you by what authority I do these things;
Yesu anayankha kuti, “Ndikufunsani funso limodzi. Mundiyankhe, ndipo ndikuwuzani ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira izi.
30 the immersion of John—was it from Heaven or from men? Answer Me.”
Ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena kwa anthu? Ndiwuzeni.”
31 And they were reasoning with themselves, saying, “If we may say, From Heaven, He will say, Why then did you not believe him?
Iwo anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Wochokera kumwamba,’ atifunsa kuti, ‘Nanga nʼchifukwa chiyani simunamukhulupirire?’
32 But if we may say, From men…” They were fearing the people, for all were holding that John was indeed a prophet;
Koma ife tikati, ‘Wochokera kwa anthu.’” (Amaopa anthu, pakuti aliyense amakhulupirira kuti Yohane analidi mneneri).
33 and answering they say to Jesus, “We have not known”; and Jesus answering says to them, “Neither do I tell you by what authority I do these things.”
Ndipo anamuyankha Yesu kuti, “Sitikudziwa.” Yesu anati, “Nanenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji ndichitira zimenezi.”