< Mark 1 >
1 A beginning of the good news of Jesus Christ, Son of God.
Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
2 As it has been written in the Prophets: “Behold, I send My messenger before Your face, Who will prepare Your way before You.
monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
3 A voice of one calling in the wilderness: Prepare the way of the LORD, Make His paths straight.”
“Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
4 John came immersing in the wilderness, and proclaiming an immersion of conversion for forgiveness of sins,
Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
5 and there were going forth to him all the region of Judea, and they of Jerusalem, and they were all immersed by him in the river Jordan, confessing their sins.
Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
6 And John was clothed with camel’s hair, and a girdle of skin around his loins, and eating locusts and honey of the field,
Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
7 and he proclaimed, saying, “He comes—who is mightier than I—after me, of whom I am not worthy—having stooped down—to loose the strap of His sandals;
Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
8 I indeed immersed you in water, but He will immerse you in the Holy Spirit.”
Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
9 And it came to pass in those days, Jesus came from Nazareth of Galilee, and was immersed by John in the Jordan;
Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
10 and immediately coming up from the water, He saw the heavens dividing, and the Spirit coming down on Him as a dove;
Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
11 and a voice came out of the heavens, “You are My Son, the Beloved, in whom I delighted.”
Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
12 And immediately the Spirit puts Him forth into the wilderness,
Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
13 and He was there in the wilderness forty days, being tempted by Satan, and He was with the beasts, and the messengers were ministering to Him.
ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
14 And after the delivering up of John, Jesus came to Galilee, proclaiming the good news of the Kingdom of God,
Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
15 and saying, “The time has been fulfilled, and the Kingdom of God has come near, convert and believe in the good news.”
“Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
16 And walking by the Sea of Galilee, He saw Simon, and his brother Andrew, casting a drag into the sea, for they were fishers,
Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
17 and Jesus said to them, “Come after Me, and I will make you to become fishers of men”;
Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
18 and immediately, having left their nets, they followed Him.
Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
19 And having gone on there a little, He saw James of Zebedee, and his brother John, and they were in the boat refitting the nets,
Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
20 and immediately He called them, and having left their father Zebedee in the boat with the hired servants, they went away after Him.
Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
21 And they go on to Capernaum, and immediately, on the Sabbaths, having gone into the synagogue, He was teaching,
Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
22 and they were astonished at His teaching, for He was teaching them as having authority, and not as the scribes.
Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
23 And there was in their synagogue a man with an unclean spirit, and he cried out,
Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
24 saying, “What [regards] us and You, Jesus the Nazarene? You came to destroy us; I have known You, who You are—the Holy One of God.”
“Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
25 And Jesus rebuked him, saying, “Be silenced, and come forth out of him,”
Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
26 and the unclean spirit having convulsed him, and having cried with a great voice, came forth out of him,
Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
27 and they were all amazed, so as to reason among themselves, saying, “What is this? What new teaching [is] this? That with authority He also commands the unclean spirits, and they obey Him!”
Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
28 And the fame of Him went forth immediately to all the region of Galilee.
Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
29 And immediately, having come forth out of the synagogue, they went into the house of Simon and Andrew, with James and John,
Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
30 and the mother-in-law of Simon was lying fevered, and immediately they tell Him about her,
Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
31 and having come near, He raised her up, having laid hold of her hand, and the fever left her immediately, and she was ministering to them.
Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
32 And evening having come, when the sun set, they brought to Him all who were ill and who were demoniacs,
Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
33 and the whole city was gathered together near the door,
Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
34 and He healed many who were ill of manifold diseases, and He cast forth many demons, and was not permitting the demons to speak, because they knew Him.
Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
35 And very early, it being yet night, having risen, He went forth, and went away to a desolate place, and was praying there;
Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
36 and Simon and those with him went in quest of Him,
Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
37 and having found Him, they say to Him, “All seek You”;
ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
38 and He says to them, “We may go into the next towns, that there also I may preach, for—for this I came forth.”
Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
39 And He was preaching in their synagogues, in all Galilee, and is casting out the demons,
Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
40 and there comes to Him a leper, calling on Him, and kneeling to Him, and saying to Him, “If You may will, You are able to cleanse me.”
Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
41 And Jesus having been moved with compassion, having stretched forth the hand, touched him and says to him, “I will, be cleansed”;
Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
42 and He having spoken, immediately the leprosy went away from him, and he was cleansed.
Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
43 And having sternly charged him, immediately He put him forth,
Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
44 and says to him, “See [that] you may say nothing to anyone, but go away, show yourself to the priest, and bring near for your cleansing the things Moses directed, for a testimony to them.”
“Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
45 And he, having gone forth, began to proclaim much, and to spread the thing abroad, so that He was no longer able to openly enter into the city, but He was outside in desolate places, and they were coming to Him from every quarter.
Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.