< Leviticus 19 >

1 And YHWH speaks to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Speak to all the congregation of the sons of Israel, and you have said to them: You are holy, because I, your God YHWH, [am] holy.
“Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Khalani oyera mtima chifukwa Ine, Yehova Mulungu wanu, ndine Woyera.
3 You each fear his mother and his father, and you keep My Sabbaths; I [am] your God YHWH.
“‘Aliyense mwa inu azilemekeza abambo ake ndi amayi ake. Ndipo muzisunga masabata anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
4 You do not turn to the idols, and you do not make a molten god for yourselves; I [am] your God YHWH.
“‘Musatembenukire ku mafano kapena kudzipangira nokha milungu ya zitsulo zosungunula. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 And when you sacrifice a sacrifice of peace-offerings to YHWH, you sacrifice it at your pleasure;
“‘Pamene mukupereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, muyipereke mwanjira yoti ilandiridwe.
6 it is eaten in the day of your sacrificing [it], and on the next day, and that which is left to the third day is burned with fire,
Nsembe izidyedwa tsiku lomwe mwayiperekalo kapena mmawa mwake. Chilichonse chotsala mpaka tsiku lachitatu chiyenera kutenthedwa.
7 and if it is really eaten on the third day, it [is] an abomination, it is not pleasing,
Ngati mudya choperekacho tsiku lachitatu, ndiye kuti mwachita chonyansa ndipo chakudyacho sichidzalandiridwa.
8 and he who is eating it bears his iniquity, for he has defiled the holy thing of YHWH, and that person has been cut off from his people.
Munthu aliyense amene adya chakudyacho adzasenza machimo ake chifukwa wayipitsa chinthu chimene ndi choyera kwa Yehova. Munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.
9 And in your reaping the harvest of your land you do not completely reap the corner of your field, and you do not gather the gleaning of your harvest,
“‘Pamene mukolola zinthu mʼmunda mwanu musakolole mpaka mʼmphepete mwa munda, ndipo musatole khunkha lake.
10 and you do not glean your vineyard, even the omitted part of your vineyard you do not gather, you leave them for the poor and for the sojourner; I [am] your God YHWH.
Musakolole mphesa zonse mʼmunda wanu wa mpesa kapena kutola mphesa zakugwa mʼmundamo. Zimenezi muzisiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wako.
11 You do not steal, nor feign, nor lie—each against his fellow.
“‘Musabe. “‘Musamanamizane. “‘Musachitirane zinthu mwachinyengo.
12 And you do not swear by My Name for falsehood, or you have defiled the Name of your God; I [am] YHWH.
“‘Musalumbire mʼdzina langa monyenga popeza kutero ndi kuyipitsa dzina la Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
13 You do not oppress your neighbor, nor take plunder; the wages of the hired worker do not remain with you until morning.
“‘Musapsinje mnzanu kapena kumulanda zinthu zake. “‘Musasunge malipiro a munthu wantchito usiku wonse mpaka mmawa.
14 You do not revile the deaf; and you do not put a stumbling block before the blind; and you have been afraid of your God; I [am] YHWH.
“‘Musatemberere wosamva kapena kuyikira munthu wosaona chinthu choti apunthwe nacho patsogolo pake, koma muziopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
15 You do not do perversity in judgment; you do not lift up the face of the poor, nor honor the face of the great; you judge your fellow in righteousness.
“‘Musamaweruze mopanda chilungamo. Musachite tsankho pakati pa osauka ndi olemera, koma muweruze mlandu wa mnzanu mwachilungamo.
16 You do not go slandering among your people; you do not stand against the blood of your neighbor; I [am] YHWH.
“‘Musamapite uku ndi uku kunena bodza pakati pa anthu anu. “‘Musachite kanthu kalikonse kamene kangadzetse imfa kwa mnzanu. Ine ndine Yehova.
17 You do not hate your brother in your heart; you certainly reprove your fellow, and do not permit sin on him.
“‘Musamude mʼbale wanu mu mtima mwanu. Koma mudzudzuleni mnzanu moona mtima kuti musakhale wolakwa.
18 You do not take vengeance, nor watch the sons of your people; and you have had love for your neighbor as yourself; I [am] YHWH.
“‘Musamubwezere mnzanu choyipa kapena kumusungira kanthu kunkhosi, koma konda mnansi wako monga iwe mwini. Ine ndine Yehova.
19 You keep My statutes. You do not cause your livestock to mate [with] two kinds; you do not sow your field with two kinds; and a garment of two kinds, mixed material, does not go up on you.
“‘Muzisunga malangizo anga. “‘Tsono musamalole kuti ngʼombe zanu zikwerane ndi chiweto cha mtundu wina. “‘Ndiponso musamadzale mbewu za mitundu iwiri mʼmunda umodzi. “‘Musavale chovala chopangidwa ndi nsalu za mitundu iwiri.
20 And when a man lies with a woman with seed [from] intercourse, and she [is] a maidservant, betrothed to a man, and not really ransomed, or freedom has not been given to her, there is an investigation; they are not put to death, for she [is] not free.
“‘Ngati munthu agonana ndi kapolo wamkazi amene wafunsidwa mbeta ndi munthu wina, koma sanawomboledwe kapenanso kulandira ufulu wake, alangidwe. Koma onsewa asaphedwe, chifukwa mkaziyo anali asanalandire ufulu wake.
21 And he has brought in his guilt-offering to YHWH, to the opening of the Tent of Meeting, a ram [for] a guilt-offering,
Koma mwamunayo abwere ndi nsembe yopepesera kupalamula kwa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna
22 and the priest has made atonement for him with the ram of the guilt-offering before YHWH, for his sin which he has sinned, and it has been forgiven him because of his sin which he has sinned.
ndipo wansembe achite nayo mwambo wopepesera chifukwa cha kupalamula kumene anachita pamaso pa Yehova. Akatero tchimo lake lidzakhululukidwa.
23 And when you come into the land and have planted all [kinds] of trees [for] food, then you have reckoned its fruit as uncircumcised, it is uncircumcised to you [for] three years, it is not eaten,
“‘Mukadzalowa mʼdzikomo ndi kudzala mtengo wa mtundu uliwonse wa zipatso, zipatso zakezo mudzaziyese ngati zodetsedwa. Ndiye kuti kwa zaka zitatu zidzakhale zoletsedwa kwa inu. Musadzazidye nthawi imeneyi.
24 and in the fourth year all its fruit is holy—praises for YHWH.
Chaka chachinayi, zipatso zake zonse zidzakhala zopatulika, ndipo zidzakhala chopereka cha matamando kwa Yehova.
25 And in the fifth year you eat its fruit—to add to you its increase; I [am] your God YHWH.
Koma chaka chachisanu, mudzatha kudya zipatso zake kuti mitengoyo idzakubalireni zochuluka. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26 You do not eat with the blood. You do not enchant, nor observe clouds.
“‘Musadye nyama ya magazi. “‘Musamawombeze kapena kuchita zamatsenga.
27 You do not round the corner of your head, nor destroy the corner of your beard.
“‘Musamamete mduliro kapena kumeta mʼmphepete mwa ndevu zanu.
28 And you do not put a cutting for the soul in your flesh; and a writing, a cross-mark, you do not put on yourself; I [am] YHWH.
“‘Musadzichekecheke pathupi panu chifukwa cha munthu wakufa kapena kudzitema mphini pa thupi lanu. Ine ndine Yehova.
29 You do not defile your daughter to cause her to go whoring, that the land does not go whoring, and the land has been full of wickedness.
“‘Musamuyipitse mwana wanu wamkazi pomusandutsa mkazi wachiwerewere. Mukatero dziko lidzasanduka la anthu achiwerewere ndi lodzaza ndi zoyipa.
30 You keep My Sabbaths and you revere My sanctuary; I [am] YHWH.
“‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga opatulika. Ine ndine Yehova.
31 You do not turn to those having familiar spirits, and you do not seek for wizards, to become unclean by them; I [am] your God YHWH.
“‘Musamapite kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kapena kwa owombeza. Musamawafunefune kuti angakuyipitseni. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
32 You rise up at the presence of grey hairs, and you have honored the presence of an old man, and have been afraid of your God; I [am] YHWH.
“‘Muzikhala mwa ulemu pamaso pa munthu wachikulire, ndipo muzichitira ulemu munthu wokalamba. Kumeneko ndiye kuopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
33 And when a sojourner sojourns with you in your land, you do not oppress him;
“‘Pamene mlendo akhala nanu mʼdziko mwanu, musamuzunze.
34 the sojourner who is sojourning with you is to you as a native among you, and you have had love for him as for yourself, for you have been sojourners in the land of Egypt; I [am] your God YHWH.
Mlendo amene akhala nanu akhale ngati mmodzi mwa mbadwa zanu. Mumukonde monga momwe mumadzikondera inu nomwe. Paja inu munali alendo mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
35 You do not do perversity in the judgment, in the measure, in the weight, and in the liquid measure;
“‘Musamachite za chinyengo poweruza mlandu, kapena poyeza utali, kulemera ngakhalenso kuchuluka kwa zinthu.
36 you have righteous balances, righteous weights, a righteous ephah, and a righteous hin; I [am] your God YHWH, who has brought you out from the land of Egypt;
Miyeso ya sikelo, miyeso yoyezera kulemera kwa zinthu, miyeso yotchedwa efa ndi miyeso yotchedwa hini zikhale zolungama. Ine ndine Yehova, Mulungu wanu amene ndinakutulutsani ku dziko la Igupto.
37 and you have observed all my statutes, and all my judgments, and have done them; I [am] YHWH.”
“‘Choncho muzisunga malangizo ndi malamulo angawa ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.’”

< Leviticus 19 >