< Leviticus 14 >

1 And YHWH speaks to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “This is a law of the leper, in the day of his cleansing, that he has been brought to the priest,
“Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
3 and the priest has gone out to the outside of the camp, and the priest has seen, and behold, the plague of leprosy has ceased from the leper,
Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
4 and the priest has commanded, and he has taken for him who is to be cleansed, two clean living birds, and cedar wood, and scarlet, and hyssop.
wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
5 And the priest has commanded, and he has slaughtered one bird on an earthen vessel, over running water;
Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
6 [as for] the living bird, he takes it, and the cedar wood, and the scarlet, and the hyssop, and has dipped them and the living bird in the blood of the slaughtered bird, over the running water,
Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
7 and he has sprinkled on him who is to be cleansed from the leprosy seven times, and has pronounced him clean, and has sent out the living bird over the face of the field.
Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
8 And he who is to be cleansed has washed his garments, and has shaved all his hair, and has bathed with water, and has been clean, and afterward he comes into the camp, and has dwelt at the outside of his tent [for] seven days.
“Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
9 And it has been, on the seventh day—he shaves all his hair, his head, and his beard, and his eyebrows, even all his hair he shaves, and he has washed his garments, and has bathed his flesh with water, and has been clean.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
10 And on the eighth day he takes two lambs, perfect ones, and one ewe-lamb, daughter of a year, a perfect one, and three-tenth parts of flour [for] a present, mixed with oil, and one log of oil.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
11 And the priest who is cleansing has caused the man who is to be cleansed to stand with them before YHWH, at the opening of the Tent of Meeting,
Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
12 and the priest has taken one male lamb, and has brought it near for a guilt-offering, also the log of oil, and has waved them [as] a wave-offering before YHWH.
“Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
13 And he has slaughtered the lamb in the place where he slaughters the sin-offering and the burnt-offering, in the holy place; for like the sin-offering, the guilt-offering is for the priest; it [is] most holy.
Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
14 And the priest has taken of the blood of the guilt-offering, and the priest has put [it] on the tip of the right ear of him who is to be cleansed, and on the thumb of his right hand, and on the great toe of his right foot;
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
15 and the priest has taken of the log of oil, and has poured [it] on the left palm of the priest,
Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
16 and the priest has dipped his right finger in the oil which [is] on his left palm, and has sprinkled of the oil with his finger seven times before YHWH.
aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
17 And of the remainder of the oil which [is] on his palm, the priest puts [it] on the tip of the right ear of him who is to be cleansed, and on the thumb of his right hand, and on the great toe of his right foot, on the blood of the guilt-offering;
Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
18 and the remnant of the oil which [is] on the palm of the priest, he puts [it] on the head of him who is to be cleansed, and the priest has made atonement for him before YHWH.
Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
19 And the priest has made the sin-offering, and has made atonement for him who is to be cleansed from his uncleanness, and afterward he slaughters the burnt-offering;
“Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
20 and the priest has caused the burnt-offering to ascend, also the present, on the altar, and the priest has made atonement for him, and he has been clean.
ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
21 And if he [is] poor, and his hand is not reaching [these things], then he has taken one lamb [for] a guilt-offering, for a wave-offering, to make atonement for him, and one-tenth part of flour mixed with oil for a present, and a log of oil,
“Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
22 and two turtle-doves, or two young pigeons, which his hand reaches to, and one has been a sin-offering and one a burnt-offering;
Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
23 and he has brought them in on the eighth day for his cleansing to the priest, to the opening of the Tent of Meeting, before YHWH.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
24 And the priest has taken the lamb of the guilt-offering, and the log of oil, and the priest has waved them [as] a wave-offering before YHWH;
Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
25 and he has slaughtered the lamb of the guilt-offering, and the priest has taken of the blood of the guilt-offering, and has put [it] on the tip of the right ear of him who is to be cleansed, and on the thumb of his right hand, and on the great toe of his right foot;
Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
26 and the priest pours of the oil on the left palm of the priest;
Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
27 and the priest has sprinkled with his right finger of the oil which [is] on his left palm, seven times before YHWH.
ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
28 And the priest has put of the oil which [is] on his palm, on the tip of the right ear of him who is to be cleansed, and on the thumb of his right hand, and on the great toe of his right foot, on the place of the blood of the guilt-offering;
Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
29 and he puts the remnant of the oil which [is] on the palm of the priest on the head of him who is to be cleansed, to make atonement for him, before YHWH.
Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
30 And he has made one of the turtle-doves or of the young pigeons (from that which his hand reaches to,
Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
31 [even] that which his hand reaches to), one a sin-offering and one a burnt-offering, besides the present, and the priest has made atonement for him who is to be cleansed before YHWH.
imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
32 This [is] a law of him in whom [is] a plague of leprosy, whose hand does not reach to his cleansing.”
“Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
33 And YHWH speaks to Moses and to Aaron, saying,
“Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
34 “When you come into the land of Canaan, which I am giving to you for a possession, and I have put a plague of leprosy in a house [in] the land of your possession,
Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
35 then he whose the house [is] has come in and declared [it] to the priest, saying, Some plague has appeared to me in the house;
mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
36 and the priest has commanded, and they have prepared the house before the priest comes in to see the plague (that all which [is] in the house is not unclean), and afterward the priest comes in to see the house;
Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
37 and he has seen the plague, and behold, the plague [is] in the walls of the house, hollow streaks, greenish or reddish, and their appearance [is] lower than the wall,
Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
38 and the priest has gone out of the house to the opening of the house, and has shut up the house [for] seven days.
wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
39 And the priest has turned back on the seventh day, and has seen, and behold, the plague has spread in the walls of the house,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
40 and the priest has commanded, and they have drawn out the stones in which the plague [is], and have cast them to the outside of the city, to an unclean place;
wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
41 and he causes the house to be scraped all around inside, and they have poured out the clay which they have scraped off, at the outside of the city, at an unclean place;
Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
42 and they have taken other stones, and brought [them] to the place of the stones, and he takes other clay and has coated the house.
Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
43 And if the plague returns, and has broken out in the house, after he has drawn out the stones, and after the scraping of the house, and after the coating,
“Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
44 then the priest has come in and seen, and behold, the plague has spread in the house; it [is] a fretting leprosy in the house; it [is] unclean.
wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
45 And he has broken down the house, its stones, and its wood, and all the clay of the house, and he has brought [them] forth to the outside of the city, to an unclean place.
Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
46 And he who is going into the house all the days he has shut it up, is unclean until the evening;
“Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
47 and he who is lying in the house washes his garments; and he who is eating in the house washes his garments.
Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
48 And if the priest certainly comes in, and has seen, and behold, the plague has not spread in the house after the coating of the house, then the priest has pronounced the house clean, for the plague has been healed.
“Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
49 And he has taken two birds, and cedar wood, and scarlet, and hyssop for the cleansing of the house;
Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
50 and he has slaughtered one bird on an earthen vessel, over running water;
Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
51 and he has taken the cedar wood, and the hyssop, and the scarlet, and the living bird, and has dipped them in the blood of the slaughtered bird, and in the running water, and has sprinkled against the house seven times.
Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
52 And he has cleansed the house with the blood of the bird, and with the running water, and with the living bird, and with the cedar wood, and with the hyssop, and with the scarlet;
Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
53 and he has sent the living bird away to the outside of the city to the face of the field, and has made atonement for the house, and it has been clean.
Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
54 This [is] the law for every plague of the leprosy and for scale,
Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
55 and for leprosy of a garment, and of a house,
nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
56 and for a rising, and for a scab, and for a bright spot—
khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
57 to direct in the day of being unclean, and in the day of being clean; this [is] the law of the leprosy.”
kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.

< Leviticus 14 >