< Lamentations 4 >

1 [ALEPH-BET] How the gold has become dim, Changed the best—the pure gold! Stones of the sanctuary are poured out At the head of all out-places.
Haa! Golide wathimbirira, golide wosalala wasinthikiratu! Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika pamphambano ponse pa mzinda.
2 The precious sons of Zion, Who are comparable with fine gold, How they have been reckoned earthen bottles, Work of the hands of a potter.
Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali amene kale anali ngati golide, tsopano ali ngati miphika ya dothi, ntchito ya owumba mbiya!
3 Even dragons have drawn out the breast, They have suckled their young ones, The daughter of my people has become cruel, Like the ostriches in a wilderness.
Ngakhale nkhandwe zimapereka bere kuyamwitsa ana ake, koma anthu anga asanduka ankhanza ngati nthiwatiwa mʼchipululu.
4 The tongue of a suckling has cleaved to his palate with thirst, Infants asked for bread, they have no dealer [of it] out.
Lilime la mwana lakangamira kukhosi chifukwa cha ludzu, ana akupempha chakudya, koma palibe amene akuwapatsa.
5 Those eating of delicacies have been desolate in out-places, Those supported on scarlet have embraced dunghills.
Iwo amene kale ankadya zonona akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda. Iwo amene kale ankavala zokongola tsopano akugona pa phulusa.
6 And greater is the iniquity of the daughter of my people, Than the sin of Sodom, That was overturned as [in] a moment, And no hands were stayed on her.
Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu kuposa anthu a ku Sodomu, amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa popanda owathandiza.
7 Purer were her Nazarites than snow, Whiter than milk, ruddier of body than rubies, Of sapphire their form.
Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana ndi oyera kuposa mkaka. Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi, maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.
8 Their face has been darker than blackness, They have not been known in out-places, Their skin has cleaved to their bone, It has withered—it has been as wood.
Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye; palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda. Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo; lawuma gwaa ngati nkhuni.
9 Better have been the pierced of a sword Than the pierced of famine, For these flow away, pierced through, Without the increase of the field.
Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa amene anafa ndi njala; chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.
10 The hands of merciful women have boiled their own children, They have been for food to them, In the destruction of the daughter of my people.
Amayi achifundo afika pophika ana awo enieni, ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu anga anali kuwonongeka.
11 YHWH has completed His fury, He has poured out the fierceness of His anger, And He kindles a fire in Zion, And it devours her foundations.
Yehova wakwaniritsa ukali wake; wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa. Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni kuti uwononge maziko ake.
12 The kings of earth did not believe, And any of the inhabitants of the world, That an adversary and enemy would come Into the gates of Jerusalem.
Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire, kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse, kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa pa zipata za Yerusalemu.
13 Because of the sins of her prophets, The iniquities of her priests, Who are shedding in her midst the blood of the righteous,
Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake ndi mphulupulu za ansembe ake, amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.
14 They have wandered naked in out-places, They have been defiled with blood, Without [any] being able to touch their clothing,
Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda ngati anthu osaona. Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.
15 “Turn aside—unclean,” they called to them, “Turn aside, turn aside, do not touch,” For they fled—indeed, they have wandered, They have said among nations: “They do not add to sojourn.”
Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!” “Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!” Akamathawa ndi kumangoyendayenda, pakati pa anthu a mitundu yonse amati, “Asakhalenso ndi ife.”
16 The face of YHWH has divided them, He does not add to behold them, They have not lifted up the face of priests, They have not favored [the] old and elderly.
Yehova mwini wake wawabalalitsa; Iye sakuwalabadiranso. Ansembe sakulandira ulemu, akuluakulu sakuwachitira chifundo.
17 While we exist—consumed are our eyes for our vain help, In our watchtower we have watched for a nation [that] does not save.
Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana, chithandizo chosabwera nʼkomwe, kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu wa anthu umene sukanatipulumutsa.
18 They have hunted our steps from going in our broad-places, Near has been our end, fulfilled our days, For our end has come.
Anthu ankalondola mapazi athu, choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda. Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka, chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.
19 Swifter have been our pursuers, Than the eagles of the heavens, On the mountains they have burned [after] us, In the wilderness they have laid wait for us.
Otilondola akuthamanga kwambiri kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga; anatithamangitsa mpaka ku mapiri ndi kutibisalira mʼchipululu.
20 The breath of our nostrils—the anointed of YHWH, Has been captured in their pits, of whom we said: “We live among nations in his shadow.”
Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo, anakodwa mʼmisampha yawo. Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake pakati pa mitundu ya anthu.
21 Rejoice and be glad, O daughter of Edom, Dwelling in the land of Uz, Even to you a cup passes over, You are drunk, and make yourself naked.
Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu. Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso chikho chidzakupeza; udzaledzera mpaka kukhala maliseche.
22 Completed [is] your iniquity, daughter of Zion, He does not add to remove you, He has inspected your iniquity, O daughter of Edom, He has removed [you] because of your sins!
Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha; Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo. Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu, ndi kuyika poyera mphulupulu zako.

< Lamentations 4 >