< Judges 1 >

1 And it comes to pass after the death of Joshua, that the sons of Israel ask of YHWH, saying, “Who goes up for us to the Canaanite, at the commencement, to fight against it?”
Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
2 And YHWH says, “Judah goes up; behold, I have given the land into his hand.”
Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
3 And Judah says to his brother Simeon, “Go up with me into my lot, and we fight against the Canaanite—and I have gone, even I, with you into your lot”; and Simeon goes with him.
Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
4 And Judah goes up, and YHWH gives the Canaanite and the Perizzite into their hand, and they strike them in Bezek—ten thousand men;
Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
5 and they find Adoni-Bezek in Bezek, and fight against him, and strike the Canaanite and the Perizzite.
Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
6 And Adoni-Bezek flees, and they pursue after him, and seize him, and cut off his thumbs and his great toes,
Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
7 and Adoni-Bezek says, “Seventy kings—their thumbs and their great toes cut off—have been gathering under my table; as I have done so God has repaid to me”; and they bring him to Jerusalem, and he dies there.
Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
8 And the sons of Judah fight against Jerusalem, and capture it, and strike it by the mouth of the sword, and they have sent the city into fire;
Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
9 and afterward the sons of Judah have gone down to fight against the Canaanite inhabiting the hill-country, and the south, and the low country;
Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
10 and Judah goes to the Canaanite who is dwelling in Hebron (and the name of Hebron [was] formerly Kirjath-Arba), and they strike Sheshai, and Ahiman, and Talmai.
Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
11 And he goes there to the inhabitants of Debir (and the name of Debir [was] formerly Kirjath-Sepher),
Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
12 and Caleb says, “He who strikes Kirjath-Sepher and has captured it—then I have given my daughter Achsah to him for a wife.”
Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
13 And Othniel son of Kenaz, younger brother of Caleb, captures it, and he gives his daughter Achsah to him for a wife.
Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
14 And it comes to pass in her coming in, that she persuades him to ask from her father the field, and she comes down off the donkey, and Caleb says to her, “What do you [want]?”
Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
15 And she says to him, “Give a blessing to me; when you have given me the south land—then you have given springs of water to me”; and Caleb gives the upper springs and the lower springs to her.
Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
16 And the sons of the Kenite, father-in-law of Moses, have gone up out of the city of palms with the sons of Judah [to] the wilderness of Judah, which [is] in the south of Arad, and they go and dwell with the people.
Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
17 And Judah goes with his brother Simeon, and they strike the Canaanite inhabiting Zephath, and devote it; and [one] calls the name of the city Hormah.
Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
18 And Judah captures Gaza and its border, and Askelon and its border, and Ekron and its border;
Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
19 and YHWH is with Judah, and he occupies the hill-country, but not to dispossess the inhabitants of the valley, for they have chariots of iron.
Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
20 And they give Hebron to Caleb, as Moses has spoken, and he dispossesses the three sons of Anak there.
Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
21 And the sons of Benjamin have not dispossessed the Jebusite inhabiting Jerusalem; and the Jebusite dwells with the sons of Benjamin, in Jerusalem, until this day.
Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
22 And the house of Joseph goes up—even they—to Beth-El, and YHWH [is] with them;
A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
23 and the house of Joseph causes [men] to spy out Beth-El (and the name of the city [was] formerly Luz),
Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
24 and the watchers see a man coming out from the city, and say to him, “Please show us the entrance of the city, and we have done kindness with you.”
Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
25 And he shows them the entrance of the city, and they strike the city by the mouth of the sword, and they have sent the man and all his family away;
Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
26 and the man goes to the land of the Hittites, and builds a city, and calls its name Luz—it [is] its name to this day.
Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
27 And Manasseh has not occupied Beth-Shean and its towns, and Taanach and its towns, and the inhabitants of Dor and its towns, and the inhabitants of Iblaim and its towns, and the inhabitants of Megiddo and its towns, and the Canaanite is desirous to dwell in that land;
Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
28 and it comes to pass, when Israel has been strong, that he sets the Canaanite to forced labor, and has not utterly dispossessed it.
Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
29 And Ephraim has not dispossessed the Canaanite who is dwelling in Gezer, and the Canaanite dwells in its midst, in Gezer.
Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
30 Zebulun has not dispossessed the inhabitants of Kitron, and the inhabitants of Nahalol, and the Canaanite dwells in its midst, and they become forced labor.
Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
31 Asher has not dispossessed the inhabitants of Accho, and the inhabitants of Sidon, and Ahlab, and Achzib, and Helbah, and Aphik, and Rehob;
A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
32 and the Asherite dwells in the midst of the Canaanite, the inhabitants of the land, for it has not dispossessed them.
Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
33 Naphtali has not dispossessed the inhabitants of Beth-Shemesh, and the inhabitants of Beth-Anath, and he dwells in the midst of the Canaanite, the inhabitants of the land; and the inhabitants of Beth-Shemesh and of Beth-Anath were for forced labor for them.
Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
34 And the Amorites press the sons of Dan to the mountain, for they have not permitted them to go down to the valley;
Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
35 and the Amorite is desirous to dwell in Mount Heres, in Aijalon, and in Shaalbim, and the hand of the house of Joseph is heavy, and they are for forced labor;
Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
36 and the border of the Amorite [is] from the ascent of Akrabbim, from the rock and upward.
Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.

< Judges 1 >