< Joshua 24 >
1 And Joshua gathers all the tribes of Israel to Shechem, and calls for [the] elderly of Israel, and for his heads, and for his judges, and for his authorities, and they station themselves before God.
Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
2 And Joshua says to all the people, “Thus said YHWH, God of Israel: Beyond the River your fathers have dwelt of old—Terah father of Abraham and father of Nachor—and they serve other gods;
Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
3 and I take your father Abraham from beyond the River, and cause him to go through all the land of Canaan, and multiply his seed, and give Isaac to him.
Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
4 And I give Jacob and Esau to Isaac; and I give Mount Seir to Esau, to possess it; and Jacob and his sons have gone down to Egypt.
ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
5 And I send Moses and Aaron, and plague Egypt, as I have done in its midst, and afterward I have brought you out.
“‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
6 And I bring out your fathers from Egypt, and you go to the sea, and the Egyptians pursue after your fathers, with chariot and with horsemen, to the Red Sea;
Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
7 and they cry to YHWH, and He sets thick darkness between you and the Egyptians, and brings the sea over him, and covers them, and your eyes see that which I have done in Egypt; and you dwell in a wilderness [for] many days.
Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
8 And I bring you into the land of the Amorite who is dwelling beyond the Jordan, and they fight with you, and I give them into your hand, and you possess their land, and I destroy them out of your presence.
“‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
9 And Balak son of Zippor, king of Moab, rises and fights against Israel, and sends and calls for Balaam son of Beor, to revile you,
Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
10 and I have not been willing to listen to Balaam, and he greatly blesses you, and I deliver you out of his hand.
Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
11 And you pass over the Jordan, and come to Jericho, and the possessors of Jericho fight against you—the Amorite, and the Perizzite, and the Canaanite, and the Hittite, and the Girgashite, the Hivite, and the Jebusite—and I give them into your hand.
“‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
12 And I send the hornet before you, and it casts them out from your presence—two kings of the Amorite—not by your sword, nor by your bow.
Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
13 And I give a land to you for which you have not labored, and cities which you have not built, and you dwell in them; you are eating of vineyards and olive-yards which you have not planted.
Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
14 And now, fear YHWH, and serve Him, in perfection and in truth, and turn aside the gods which your fathers served beyond the River, and in Egypt, and serve YHWH;
“Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
15 and if [it is] wrong in your eyes to serve YHWH—choose for yourselves today whom you serve—whether the gods whom your fathers served, which [are] beyond the River, or the gods of the Amorite in whose land you are dwelling; but me and my house—we serve YHWH.”
Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
16 And the people answer and say, “Far be it from us to forsake YHWH, to serve other gods;
Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
17 for our God YHWH [is] He who is bringing us and our fathers up out of the land of Egypt, out of a house of servants, and who has done these great signs before our eyes, and keeps us in all the way in which we have gone, and among all the peoples through whose midst we passed;
Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
18 and YHWH casts out the whole of the peoples, even the Amorite inhabiting the land, from our presence; we also serve YHWH, for He [is] our God.”
Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
19 And Joshua says to the people, “You are not able to serve YHWH, for He [is] a most holy God; He [is] a zealous God; He does not bear with your transgression and with your sins.
Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
20 When you forsake YHWH, and have served gods of a stranger, then He has turned back and done harm to you, and consumed you, after that He has done good to you.”
Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
21 And the people say to Joshua, “No, but we serve YHWH!”
Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
22 And Joshua says to the people, “You are witnesses against yourselves, that you have chosen YHWH for yourselves, to serve Him,” and they say, “Witnesses!”
Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
23 “And now, turn aside the gods of the stranger which [are] in your midst, and incline your heart to YHWH, God of Israel.”
Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
24 And the people say to Joshua, “We serve our God YHWH, and we listen to His voice.”
Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
25 And Joshua makes a covenant with the people on that day, and lays a statute and an ordinance on it, in Shechem.
Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
26 And Joshua writes these words in the Scroll of the Law of God, and takes a great stone, and raises it up there under the oak which [is] in the sanctuary of YHWH.
Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
27 And Joshua says to all the people, “Behold, this stone is for a witness against us, for it has heard all the sayings of YHWH which He has spoken with us, and it has been for a witness against you, lest you lie against your God.”
Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
28 And Joshua sends the people away, each to his inheritance.
Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
29 And it comes to pass, after these things, that Joshua son of Nun, servant of YHWH, dies, a son of one hundred and ten years,
Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
30 and they bury him in the border of his inheritance, in Timnath-Serah, which [is] in the hill-country of Ephraim, on the north of the hill of Gaash.
ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
31 And Israel serves YHWH all [the] days of Joshua, and all [the] days of the elderly who prolonged days after Joshua, and who knew all the work of YHWH which He did to Israel.
Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
32 And the bones of Joseph, which the sons of Israel brought up out of Egypt, they buried in Shechem, in the portion of the field which Jacob bought from the sons of Hamor father of Shechem, with one hundred kesitah; and they are for an inheritance to the sons of Joseph.
Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
33 And Eleazar son of Aaron died, and they bury him in a hill of his son Phinehas, which was given to him in the hill-country of Ephraim.
Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.