< John 6 >

1 After these things Jesus went away beyond the Sea of Galilee (of Tiberias),
Nthawi ina zitatha izi, Yesu anawolokera ku gombe la kutali la nyanja ya Galileya (iyi ndi nyanja ya Tiberiya),
2 and there was following Him a great multitude, because they were seeing His signs that He was doing on the ailing;
ndipo gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye chifukwa linaona zizindikiro zodabwitsa zimene anazichita pa odwala.
3 and Jesus went up to the mountain, and He was sitting with His disciples there,
Kenaka Yesu anakwera pa phiri nakhala pansi ndi ophunzira ake.
4 and the Passover was near, the celebration of the Jews.
Tsopano phwando la Paska la Ayuda linali pafupi.
5 Jesus then having lifted up [His] eyes and having seen that a great multitude comes to Him, says to Philip, “From where will we buy loaves, that these may eat?”
Yesu atakweza maso ndi kuona gulu lalikulu la anthu likubwera kwa Iye, anati kwa Filipo, “Kodi tingagule kuti buledi kuti anthu awa adye?”
6 And this He said, trying him, for He Himself had known what He was about to do.
Iye anafunsa izi kumuyesa chabe, pakuti Iye ankadziwa chimene ankayenera kuchita.
7 Philip answered Him, “Two hundred denarii worth of loaves are not sufficient to them, that each of them may receive some little”;
Filipo anamuyankha Iye kuti, “Malipiro a miyezi isanu ndi itatu sangathe kugula buledi okwanira aliyense kuti adye!”
8 one of His disciples—Andrew, the brother of Simon Peter—says to Him,
Mmodzi wa ophunzira ake, Andreya, mʼbale wa Simoni Petro, anati,
9 “There is one little boy here who has five barley loaves and two fishes, but these—what are they to so many?”
“Pano pali mnyamata amene ali ndi buledi musanu wabarele ndi tinsomba tiwiri, kodi zingakwane onsewa?”
10 And Jesus said, “Make the men to sit down”; and there was much grass in the place, the men then sat down, in number, as it were, five thousand,
Yesu anati, “Awuzeni anthuwa akhale pansi.” Pamalo pamenepa panali udzu wambiri ndipo amuna amene anakhala pansi anali osachepera 5,000.
11 and Jesus took the loaves, and having given thanks He distributed [them] to the disciples, and the disciples to those reclining, in like manner, also of the little fishes as much as they wished.
Kenaka Yesu anatenga bulediyo, atayamika anagawira iwo amene anakhala pansi, chimodzimodzinso nsombazo monga momwe iwo anafunira.
12 And when they were filled, He says to His disciples, “Gather together the broken pieces that are left over, that nothing may be lost”;
Ndipo atakhuta, Iye anati kwa ophunzira ake, “Tolani zotsala kuti pasawonongeke kanthu.”
13 they gathered together, therefore, and filled twelve hand-baskets with broken pieces, from the five barley loaves that were over to those having eaten.
Choncho iwo anasonkhanitsa makombo nadzaza madengu khumi ndi awiri.
14 The men, then, having seen the sign that Jesus did, said, “This is truly the Prophet who is coming into the world”;
Pambuyo pake anthu ataona chizindikiro chodabwitsa chimene Yesu anachita, iwo anati, “Zoonadi uyu ndi Mneneri wakudzayo mʼdziko la pansi.”
15 Jesus, therefore, having known that they are about to come, and to seize Him by force that they may make Him king, retired again to the mountain Himself alone.
Yesu atadziwa kuti iwo amafuna kubwera kudzamuwumiriza kuti akhale mfumu, anachoka napita ku phiri pa yekha.
16 And when evening came, His disciples went down to the sea,
Pofika madzulo, ophunzira ake anatsikira ku nyanja,
17 and having entered into the boat, they were going over the sea to Capernaum, and darkness had already come, and Jesus had not come to them,
kumene iwo analowa mʼbwato ndi kuyamba kuwoloka nyanja kupita ku Kaperenawo. Tsopano kunali kutada ndipo Yesu anali asanabwerere kwa iwo.
18 the sea also—a great wind blowing—was being raised,
Mphepo yamphamvu inawomba ndipo nyanja inalusa.
19 having pushed onward, therefore, about twenty-five or thirty stadia, they behold Jesus walking on the sea, and coming near to the boat, and they were afraid;
Iwo atayenda makilomita asanu kapena asanu ndi limodzi, anaona Yesu akuyandikira bwatolo, akuyenda pa madzi; ndipo anachita mantha.
20 and He says to them, “I AM; do not be afraid”;
Koma Iye anawawuza kuti, “Ndine, musaope.”
21 they were willing then to receive Him into the boat, and immediately the boat came to the land to which they were going.
Ndipo iwo analola kumutenga mʼbwatomo, nthawi yomweyo bwatolo linafika ku gombe la nyanja kumene ankapita.
22 On the next day, the multitude that was standing on the other side of the sea, having seen that there was no other little boat there except one—that into which His disciples entered—and that Jesus did not go in with His disciples into the little boat, but His disciples went away alone
Pa tsiku lotsatira gulu la anthu limene linatsala kumbali ina yanyanjayo linaona kuti panali bwato limodzi lokha, ndipo kuti Yesu sanalowe mʼbwatomo pamodzi ndi ophunzira ake, koma kuti ophunzirawo anapita okha.
23 (and other little boats came from Tiberias, near the place where they ate the bread, the LORD having given thanks),
Kenaka mabwato ena ochokera ku Tiberiya anafika pafupi ndi pamalo pamene anthu anadya buledi Ambuye atayamika.
24 when therefore the multitude saw that Jesus is not there, nor His disciples, they also entered into the boats themselves, and came to Capernaum seeking Jesus;
Nthawi yomwe gulu la anthu linaona kuti Yesu kapena ophunzira ake sanali pamenepo, ilo linalowanso mʼmabwatowo ndi kupita ku Kaperenawo kukamufunafuna Yesu.
25 and having found Him on the other side of the sea, they said to Him, “Rabbi, when have You come here?”
Atamupeza mbali ina ya nyanjayo, iwo anamufunsa Iye kuti, “Rabi, mwafika nthawi yanji kuno?”
26 Jesus answered them and said, “Truly, truly, I say to you, you seek Me, not because you saw signs, but because you ate of the loaves, and were satisfied;
Yesu anawayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mukundifuna, osati chifukwa munaona zizindikiro zodabwitsa koma chifukwa munadya chakudya ndi kukhuta.
27 do not work for the food that is perishing, but for the food that is remaining to continuous life, which the Son of Man will give to you, for the Father sealed Him—[even] God.” (aiōnios g166)
Gwirani ntchito, osati chifukwa cha chakudya chimene chimawonongeka koma chifukwa cha chakudya chimene sichiwonongeka mpaka ku moyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani. Mulungu Atate anamusindikiza chizindikiro chomuvomereza.” (aiōnios g166)
28 Therefore they said to Him, “What may we do that we may work the works of God?”
Kenaka anamufunsa Iye kuti, “Kodi tichite chiyani kuti tigwire ntchito za Mulungu?”
29 Jesus answered and said to them, “This is the work of God, that you may believe in Him whom He sent.”
Yesu anayankha kuti, “Ntchito ya Mulungu ndi iyi: Kukhulupirira Iye amene anamutuma.”
30 Therefore they said to Him, “What sign, then, do You do, that we may see and may believe You? What do You work?
Choncho iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi mudzatipatsa chizindikiro chodabwitsa chotani kuti ife tichione ndi kukhulupirira Inu? Kodi mudzachita chiyani?
31 Our fathers ate the manna in the wilderness, according as it is having been written: He gave them bread out of Heaven to eat.”
Makolo athu akale anadya mana mʼchipululu; monga zalembedwa: ‘anawapatsa buledi wochokera kumwamba kuti adye.’”
32 Jesus, therefore, said to them, “Truly, truly, I say to you, Moses did not give you the bread out of Heaven, but My Father gives you the true bread out of Heaven;
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti si Mose amene ankakupatsani chakudya chochokera kumwamba, koma ndi Atate anga amene ankakupatsani chakudya chenicheni chochokera kumwamba.
33 for the bread of God is Him coming down out of Heaven, and giving life to the world.”
Pakuti chakudya cha Mulungu ndi Iye amene wabwera kuchokera kumwamba ndi kupereka moyo ku dziko la pansi.”
34 Therefore they said to Him, “Lord, always give us this bread.”
Iwo anati, “Ambuye, kuyambira tsopano muzitipatsa buledi ameneyu.”
35 And Jesus said to them, “I AM the bread of life; he who is coming to Me may not hunger, and he who is believing in Me may not thirst—at any time;
Kenaka Yesu ananenetsa kuti, “Ine ndine chakudya chamoyo. Iye amene abwera kwa Ine sadzamva njala, ndipo iye amene akhulupirira Ine sadzamva ludzu.
36 but I said to you that you also have seen Me, and you do not believe;
Monga ndakuwuzani kale, ngakhale kuti mwandiona simukukhulupirirabe.
37 all that the Father gives to Me will come to Me; and him who is coming to Me, I will never cast outside,
Zonse zimene Atate andipatsa zidzabwera kwa Ine, ndipo aliyense amene adzabwera kwa Ine sindidzamutaya kunja.
38 because I have come down out of Heaven, not that I may do My will, but the will of Him who sent Me.
Pakuti Ine ndinatsika kuchokera kumwamba osati kudzachita chifuniro changa koma cha Iye amene anandituma Ine.
39 And this is the will of the Father who sent Me, that all that He has given to Me, I may lose none of it, but may raise it up in the last day;
Ndipo chifuniro cha Iye amene anandituma Ine nʼchakuti ndisatayepo ngakhale ndi mmodzi yemwe mwa onse amene Iye wandipatsa, koma kuti ndidzawaukitse kwa akufa pa tsiku lomaliza.
40 and this is the will of Him who sent Me, that everyone who is beholding the Son, and is believing in Him, may have continuous life, and I will raise him up in the last day.” (aiōnios g166)
Pakuti chifuniro cha Atate anga ndi chakuti aliyense amene aona Mwanayo namukhulupirira akhale ndi moyo wosatha, ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.” (aiōnios g166)
41 The Jews, therefore, were murmuring at Him, because He said, “I AM the bread that came down out of Heaven”;
Pamenepo Ayuda anayamba kungʼungʼudza chifukwa anati, “Ine ndine chakudya chotsika kuchokera kumwamba.”
42 and they said, “Is this not Jesus, the Son of Joseph, whose father and mother we have known? How then does this One say, I have come down out of Heaven?”
Iwo anati, “Kodi uyu si Yesu, mwana wa Yosefe, amene abambo ake ndi amayi ake timawadziwa? Nanga Iyeyu akunena bwanji kuti, ‘Ine ndinatsika kuchokera kumwamba?’”
43 Jesus answered, therefore, and said to them, “Do not murmur with one another;
Yesu anayankha kuti, “Musangʼungʼudze pakati panu.”
44 no one is able to come to Me if the Father who sent Me may not draw him, and I will raise him up in the last day;
Palibe munthu amene angabwere kwa Ine, ngati Atate amene anandituma Ine samubweretsa. Ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.
45 it is having been written in the Prophets: And they will all be taught of God; everyone, therefore, who heard from the Father, and learned, comes to Me;
Aneneri analemba kuti, “Onse adzaphunzitsidwa ndi Mulungu! Aliyense amene amamva Atate ndi kuphunzira kwa Iye amabwera kwa Ine.
46 not that anyone has seen the Father, except He who is from God, He has seen the Father.
Palibe amene anaona Atate koma yekhayo amene achokera kwa Mulungu; yekhayo ndiye anaona Atate.
47 Truly, truly, I say to you, he who is believing in Me has continuous life; (aiōnios g166)
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Iye amene akhulupirira ali nawo moyo wosatha. (aiōnios g166)
48 I AM the bread of life;
Ine ndine chakudya chamoyo.
49 your fathers ate the manna in the wilderness and they died;
Makolo anu akale anadya mana mʼchipululu, komabe anafa.
50 this is the bread that is coming down out of Heaven, that anyone may eat of it, and not die.
Koma pano pali chakudya chochokera kumwamba, chimene munthu akadya sangafe.
51 I AM the living bread that came down out of Heaven; if anyone may eat of this bread he will live—throughout the age; and the bread also that I will give is My flesh, that I will give for the life of the world.” (aiōn g165)
Ine ndine chakudya chamoyo chochokera kumwamba. Ngati munthu adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi zonse. Chakudya chimenechi ndi thupi langa, limene Ine ndidzalipereka kuti anthu pa dziko lapansi akhale ndi moyo.” (aiōn g165)
52 The Jews, therefore, were striving with one another, saying, “How is this One able to give us [His] flesh to eat?”
Kenaka Ayuda anayamba kutsutsana kwambiri pakati pawo kuti, “Kodi munthu uyu angathe kutipatsa bwanji thupi lake kuti tidye?”
53 Jesus, therefore, said to them, “Truly, truly, I say to you, if you may not eat the flesh of the Son of Man, and may not drink His blood, you have no life in yourselves;
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ngati simungadye thupi la Mwana wa Munthu ndi kumwa magazi ake, simungakhale ndi moyo mwa inu.
54 he who is eating My flesh, and is drinking My blood, has continuous life, and I will raise him up in the last day; (aiōnios g166)
Aliyense amene adya thupi langa ndi kumwa magazi anga ali ndi moyo wosatha ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. (aiōnios g166)
55 for My flesh is truly food, and My blood is truly drink;
Pakuti thupi langa ndi chakudya chenicheni ndipo magazi anga ndi chakumwa chenicheni.
56 he who is eating My flesh, and is drinking My blood, remains in Me, and I in him.
Aliyense amene adya thupi langa ndi kumwa magazi anga amakhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye.
57 According as the living Father sent Me, and I live because of the Father, he also who is eating Me, even that one will live because of Me;
Monga Atate amoyo anandituma Ine, ndipo ndili ndi moyo chifukwa cha Atatewo, chomwechonso amene adya thupi langa adzakhala ndi moyo chifukwa cha Ine.
58 this is the bread that came down out of Heaven; not as your fathers ate the manna, and died; he who is eating this bread will live—throughout the age.” (aiōn g165)
Ichi ndiye chakudya chimene chinatsika kuchokera kumwamba. Makolo athu akale anadya mana ndi kufa, koma iye amene adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi yonse.” (aiōn g165)
59 He said these things in a synagogue, teaching in Capernaum;
Iye ankanena izi pamene ankaphunzitsa mʼsunagoge mu Kaperenawo.
60 many, therefore, of His disciples having heard, said, “This word is hard; who is able to hear it?”
Pakumva izi ambiri a ophunzira ake anati, “Ichi ndi chiphunzitso chovuta. Angachilandire ndani?”
61 And Jesus having known in Himself that His disciples are murmuring about this, said to them, “Does this stumble you?
Pozindikira kuti ophunzira ake ankangʼungʼudza, Yesu anawafunsa kuti, “Kodi izi zikukukhumudwitsani?
62 If then you may behold the Son of Man going up where He was before?
Nanga mutaona Mwana wa Munthu akukwera kupita kumene Iye anali poyamba!
63 It is the Spirit that is giving life; the flesh does not profit anything; the sayings that I speak to you are spirit, and they are life;
Mzimu Woyera apereka moyo, thupi silipindula kanthu. Mawu amene ndayankhula kwa inu ndiwo mzimu ndipo ndi moyo.
64 but there are certain of you who do not believe”; for Jesus had known from the beginning who they are who are not believing, and who is he who will deliver Him up,
Komabe alipo ena mwa inu amene sakukhulupirira.” Pakuti Yesu ankadziwa kuyambira pachiyambi ena mwa iwo amene samakhulupirira ndi amene adzamupereka Iye.
65 and He said, “Because of this I have said to you, No one is able to come to Me if it may not have been given him from My Father.”
Iye anapitiriza kunena kuti, “Ichi ndi chifukwa chake ndinakuwuzani kuti palibe wina angabwere kwa Ine pokhapokha Atate atamuthandiza.”
66 From this [time] many of His disciples went away backward, and were no longer walking with Him,
Kuyambira nthawi imeneyi ophunzira ake ambiri anabwerera ndipo sanamutsatenso Iye.
67 Jesus, therefore, said to the Twelve, “Do you also wish to go away?”
Yesu anafunsa khumi ndi awiriwo kuti, “Kodi inu mukufuna kuchokanso?”
68 Simon Peter, therefore, answered Him, “Lord, to whom will we go? You have sayings of continuous life; (aiōnios g166)
Simoni Petro anamuyankha Iye kuti, “Ambuye, ife tidzapita kwa yani? Inu muli ndi mawu amoyo wosatha. (aiōnios g166)
69 and we have believed, and we have known, that You are the Christ, the Son of the living God.”
Ife tikhulupirira ndi kudziwa kuti Inu ndinu Woyerayo wa Mulungu.”
70 Jesus answered them, “Did I not choose you—the Twelve? And of you—one is a devil.”
Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi Ine sindinakusankheni inu khumi ndi awiri? Komabe mmodzi wa inu ndi mdierekezi.”
71 And He spoke of Judas, [son] of Simon Iscariot, for he was about to deliver Him up, being one of the Twelve.
(Iye amanena Yudasi, mwana wa Simoni Isikarioti amene ngakhale anali mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anali woti adzamupereka).

< John 6 >