< John 17 >
1 These things Jesus spoke, and lifted up His eyes to the sky, and said, “Father, the hour has come, glorify Your Son, that Your Son may also glorify You,
Yesu atatha kunena izi, anayangʼana kumwamba ndipo anapemphera: “Atate, nthawi yafika. Lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanuyo akulemekezeni Inu.
2 according as You gave to Him authority over all flesh, that—all that You have given to Him—He may give to them continuous life; (aiōnios )
Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. (aiōnios )
3 and this is the continuous life, that they may know You, the only true God, and Him whom You sent—Jesus Christ; (aiōnios )
Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. (aiōnios )
4 I glorified You on the earth, having completed the work that You have given Me, that I should do.
Ine ndabweretsa ulemerero wanu pa dziko pamene ndamaliza ntchito imene munandipatsa kuti ndi igwire.
5 And now, glorify Me, You Father, with Yourself, with the glory that I had with You before the world was;
Ndipo tsopano, Atate, ndilemekezeni Ine pamaso panu ndi ulemerero uja umene ndinali nawo kwa Inu dziko lapansi lisanayambe.
6 I revealed Your Name to the men whom You have given to Me out of the world; they were Yours, and You have given them to Me, and they have kept Your word;
“Ine ndawadziwitsa za Inu anthu amene munandipatsa mʼdziko lapansi. Iwo anali anu. Inu munawapereka kwa Ine ndipo amvera mawu anu.
7 now they have known that all things, as many as You have given to Me, are from You,
Tsopano akudziwa kuti zonse zimene munandipatsa nʼzochokera kwa Inu.
8 because the sayings that You have given to Me, I have given to them, and they themselves received, and have known truly, that I came forth from You, and they believed that You sent Me.
Pakuti Ine ndiwapatsa mawu amene Inu munandipatsa ndipo awalandira. Iwo akudziwa ndithu kuti Ine ndinachokera kwa Inu, ndipo akukhulupirira kuti Inu ndiye amene munandituma Ine.
9 I ask in regard to them; I do not ask in regard to the world, but in regard to those whom You have given to Me, because they are Yours,
Ine ndikuwapempherera. Ine sindikupempherera dziko lapansi, koma anthu amene Inu mwandipatsa, pakuti ndi anu.
10 and all Mine are Yours, and Yours [are] Mine, and I have been glorified in them;
Zonse zimene Ine ndili nazo ndi zanu, ndipo zonse zimene Inu muli nazo ndi zanga. Choncho Ine ndalemekezedwa mwa iwowo.
11 and I am no longer in the world, and these are in the world, and I come to You. Holy Father, keep them in Your Name, whom You have given to Me, that they may be one as We [are one];
Ine sindikukhalanso mʼdziko lapansi nthawi yayitali, koma iwo akanali mʼdziko lapansi. Ine ndikubwera kwa Inu. Atate Woyera, atetezeni ndi mphamvu za dzina lanu. Dzina limene munandipatsa Ine, kuti iwo akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
12 when I was with them in the world, I was keeping them in Your Name; I guarded those whom You have given to Me, and none of them were destroyed, except the son of the destruction, that the Writing may be fulfilled.
Pamene ndinali nawo, ndinawateteza ndi kuwasunga mosamala mʼdzina limene munandipatsa. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatayika kupatula yekhayo amene anayenera kuwonongeka kuti malemba akwaniritsidwe.
13 And now I come to You, and these things I speak in the world, that they may have My joy fulfilled in themselves;
“Tsopano ndikubwera kwa Inu. Ndikunena izi ndikanali mʼdziko lapansi, kuti iwo akhale ndi muyeso wodzaza wachimwemwe changa mʼkati mwawo.
14 I have given Your word to them, and the world hated them, because they are not of the world, as I am not of the world;
Ine ndawapatsa mawu anu ndipo dziko lapansi likudana nawo, pakuti sali a dziko lapansi monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
15 I do not ask that You may take them out of the world, but that You may keep them out of the evil.
Sindikupempha kuti muwachotse mʼdziko lapansi koma kuti muwateteze kwa woyipayo.
16 They are not of the world, as I am not of the world;
Iwo si a dziko lapansi, monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
17 sanctify them in Your truth, Your word is truth;
Ayeretseni ndi choonadi chanu. Mawu anu ndiye choonadi.
18 as You sent Me into the world, I also sent them into the world;
Monga Inu munandituma Ine mʼdziko lapansi, Inenso ndikuwatuma mʼdziko lapansi.
19 and I sanctify Myself for them, that they also may be sanctified in truth themselves.
Chifukwa cha iwowa Ine ndikudziyeretsa, kuti iwo ayeretsedwenso kwenikweni.
20 And I do not ask in regard to these alone, but also in regard to those who will be believing in Me through their word,
“Ine sindikupempherera iwo okhawa, komanso amene adzandikhulupirira chifukwa cha uthenga wawo.
21 that they all may be one, as You Father [are] in Me, and I in You, that they also may be one in Us, that the world may believe that You sent Me.
Ndikuwapempherera kuti onsewa akhale amodzi. Monga Inu Atate muli mwa Ine ndi Ine mwa Inu, iwonso akhale mwa Ife kuti dziko lapansi likhulupirire kuti Inu munandituma Ine.
22 And I have given to them the glory that You have given to Me, that they may be one as We are one—
Ine ndawapatsa ulemerero umene munandipatsa Ine, kuti akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
23 I in them, and You in Me, that they may be perfected into one, and that the world may know that You sent Me, and loved them as You loved Me.
Ine ndikhale mwa iwo ndipo Inu mwa Ine kuti umodzi wawo ukhale wangwiro. Choncho dziko lapansi lidzadziwa kuti Inu munandituma Ine ndipo Inu mwawakonda iwowa monga momwe Inu munandikondera Ine.
24 Father, those whom You have given to Me, I will that where I am they also may be with Me, that they may behold My glory that You gave to Me, because You loved Me before the foundation of the world.
“Atate, Ine ndikufuna kuti anthu amene mwandipatsa Ine adzakhale ndi Ine kumene kuli Ine, ndi kuona ulemerero wanga, ulemerero umene munandipatsa chifukwa Inu munandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.
25 Righteous Father, also the world did not know You, and I knew You, and these have known that You sent Me,
“Atate wolungama, ngakhale kuti dziko lapansi silikudziwani Inu, Ine ndimakudziwani, ndipo iwo amadziwa kuti Inu munandituma Ine.
26 and I made known to them Your Name, and will make known, that the love with which You loved Me may be in them, and I in them.”
Ine ndawadziwitsa dzina lanu, ndipo ndidzapitiriza kuwadziwitsa dzina lanulo, kuti chikondi chomwe munandikonda nacho chikhale mwa iwo, ndipo Ine mwa iwo.”