< Job 40 >

1 And YHWH answers Job and says:
Yehova anati kwa Yobu:
2 “Is the striver with the Mighty instructed? The reprover of God, let him answer it.”
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 And Job answers YHWH and says:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 “Behold, I have been vile, What do I return to You? I have placed my hand on my mouth.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 I have spoken once, and I do not answer, And twice, and I do not add.”
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 And YHWH answers Job out of the whirlwind and says:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 “Now gird your loins as a man, I ask you, and you cause Me to know.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Do you also make My judgment void? Do you condemn Me, That you may be righteous?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 And do you have an arm like God? And do you thunder with a voice like His?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Now put on excellence and loftiness, Indeed, put on splendor and beauty.
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Scatter abroad the wrath of your anger, And see every proud one, and make him low.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 See every proud one—humble him, And tread down the wicked in their place.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Hide them in the dust together, Bind their faces in secret.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 And even I praise you, For your right hand gives salvation to you.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Now behold, behemoth, That I made with you: He eats grass as an ox.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Now behold, his power [is] in his loins, And his strength in the muscles of his belly.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 He bends his tail as a cedar, The sinews of his thighs are wrapped together,
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 His bones [are] tubes of bronze, His bones [are] as a bar of iron.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 He [is] a beginning of the ways of God, His Maker [alone] brings His sword near;
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 For mountains bear food for him, And all the beasts of the field play there.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 He lies down under shades, In a secret place of reed and marsh.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Shades cover him, [with] their shadow, Willows of the brook cover him.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Behold, a flood oppresses—he does not hurry, He is confident though Jordan Comes forth to his mouth.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Does [one] take him by his eyes? Does [one] pierce the nose with snares?”
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Job 40 >