< Job 38 >

1 And YHWH answers Job out of the whirlwind and says:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 “Who [is] this—darkening counsel, By words without knowledge?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Now gird your loins as a man, And I ask you, and you cause Me to know.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 Where were you when I founded the earth? Declare, if you have known understanding.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Who placed its measures—if you know? Or who has stretched out a line on it?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 On what have its sockets been sunk? Or who has cast its cornerstone—
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 In the singing together of [the] stars of morning, When all [the] sons of God shout for joy?
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 And He shuts up the sea with doors, In its coming forth, it goes out from the womb.
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 In My making a cloud its clothing, And thick darkness its swaddling band,
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 And I measure My statute over it, And place bar and doors,
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 And say, To here you come, and no more, And a command is placed On the pride of your billows.
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 Have you commanded morning since your days? Do you cause the dawn to know its place?
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 To take hold on the skirts of the earth, And the wicked are shaken out of it,
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 It turns itself as clay of a seal And they station themselves as clothed.
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 And their light is withheld from the wicked, And the arm lifted up is broken.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 Have you come to springs of the sea? And in searching the deep Have you walked up and down?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Were the gates of death revealed to you? And do you see the gates of death-shade?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 You have understanding, Even to the broad places of earth! Declare—if you have known it all.
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 Where [is] this—the way light dwells? And darkness, where [is] this—its place?
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 That you take it to its boundary, And that you understand the paths of its house.
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 You have known—for then you are born, And the number of your days [are] many!
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 Have you come to the treasure of snow? Indeed, do you see the treasures of hail,
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 That I have kept back for a time of distress, For a day of conflict and battle?
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 Where [is] this, the way light is apportioned? It scatters an east wind over the earth.
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Who has divided a conduit for the flood? And a way for the lightning of the voices?
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 To cause [it] to rain on a land [with] no man, A wilderness [with] no man in it.
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 To satisfy a desolate and ruined place, And to cause to shoot up The produce of the tender grass?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Does the rain have a father? Or who has begotten the drops of dew?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 From whose belly came forth the ice? And the hoarfrost of the heavens, Who has begotten it?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Waters are hidden as a stone, And the face of the deep is captured.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 Do you bind the chains of the Pleiades? Or do you open the cords of Orion?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Do you bring out the twelve signs in [their] season? And do you comfort the Great Bear over her sons?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Have you known the statutes of the heavens? Or do you appoint Its dominion in the earth?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 Do you lift up your voice to the cloud, And abundance of water covers you?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Do you send out lightnings, and they go And say to you, Behold us?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Who has put wisdom in the inward parts? Or who has given understanding to the covered part?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Who numbers the clouds by wisdom? And the bottles of the heavens, Who causes to lie down,
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 In the hardening of dust into hardness, And clods cleave together?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 Do you hunt prey for a lion? And fulfill the desire of young lions?
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 When they bow down in dens—Abide in a thicket for a covert?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Who prepares for a raven his provision, When his young ones cry to God? They wander without food.”
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Job 38 >