< Job 28 >
1 “Surely there is a source for silver, And a place for the gold they refine;
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Iron is taken from the dust, And bronze [from] the firm stone.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 He has set an end to darkness, And he is searching to all perfection, A stone of darkness and death-shade.
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 A stream has broken out from a sojourner, Those forgotten of the foot, They were low, they wandered from man.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 The earth! Bread comes forth from it, And its under-part is turned like fire.
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 A place of the sapphire [are] its stones, And it has dust of gold.
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 A path—a ravenous bird has not known it, Nor has an eye of the falcon scorched it,
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 Nor have the sons of pride trodden it, The fierce lion has not passed over it.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 He sent forth his hand against the flint, He overturned mountains from the root.
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 Among rocks, he has cleaved brooks, And his eye has seen every precious thing.
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 He has bound overflowing rivers, And the hidden thing brings out [to] light.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 And the wisdom—from where is it found? And where [is] this, the place of understanding?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Man has not known its arrangement, Nor is it found in the land of the living.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 The deep has said, It [is] not in me, And the sea has said, It is not with me.
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 Gold is not given for it, Nor is silver weighed—its price.
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 It is not valued with pure gold of Ophir, With precious onyx and sapphire,
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Gold and crystal do not equal it, Nor [is] its exchange a vessel of fine gold.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 Corals and pearl are not remembered, The acquisition of wisdom [is] above rubies.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 The topaz of Cush does not equal it, It is not valued with pure gold.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 And the wisdom—from where does it come? And where [is] this, the place of understanding?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 It has been hid from the eyes of all living. And from the bird of the heavens It has been hidden.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 Destruction and death have said: With our ears we have heard its fame.
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 God has understood its way, And He has known its place.
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 For He looks to the ends of the earth, He sees under the whole heavens,
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 To make a weight for the wind, And He meted out the waters in measure.
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 In His making for the rain a limit, And a way for the brightness of the voices,
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 Then He has seen and declares it, He has prepared it, and also searched it out,
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 And He says to man: Behold, fear of the Lord, that [is] wisdom, And to turn from evil [is] understanding.”
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”