< Job 19 >

1 And Job answers and says:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Until when do you afflict my soul, And bruise me with words?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 These ten times you put me to shame, you do not blush. You make yourselves strange to me—
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 And also—truly, I have erred, My error remains with me.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 If, truly, you magnify yourselves over me, And decide my reproach against me;
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Know now, that God turned me upside down, And has set around His net against me,
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Behold, I cry out—violence, and am not answered, I cry aloud, and there is no judgment.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 He hedged up my way, and I do not pass over, And He places darkness on my paths.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 He has stripped my honor from off me, And He turns the crown from my head.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 He breaks me down all around, and I go, And removes my hope like a tree.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 And He kindles His anger against me, And reckons me to Him as His adversaries.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 His troops come in together, And they raise up their way against me, And encamp around my tent.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 He has put my brothers far off from me, And my acquaintances have surely been estranged from me.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 My neighbors have ceased And my familiar friends have forgotten me,
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Sojourners of my house and my maids, Reckon me for a stranger; I have been an alien in their eyes.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 I have called to my servant, And he does not answer, With my mouth I make supplication to him.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 My spirit is strange to my wife, And my favors to the sons of my [mother’s] womb.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Also sucklings have despised me, I rise, and they speak against me.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 All the men of my counsel detest me, And those I have loved, Have been turned against me.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 To my skin and to my flesh My bone has cleaved, And I deliver myself with the skin of my teeth.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Pity me, pity me, you my friends, For the hand of God has struck against me.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Why do you pursue me as God? And are not satisfied with my flesh?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Who grants now, that my words may be written? Who grants that they may be inscribed in a scroll?
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 With a pen of iron and lead—They may be hewn in a rock forever.
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 That—I have known my Redeemer, The Living and the Last, For He raises the dust.
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 And after my skin has surrounded this [body], Then from my flesh I see God—
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Whom I see on my side, And my eyes have beheld, and not a stranger, My reins have been consumed in my bosom.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 But you say, Why do we pursue after him? And the root of the matter has been found in me.
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Be afraid because of the sword, For the punishments of the sword [are] furious, That you may know that [there is] a judgment.”
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< Job 19 >