< Jeremiah 44 >

1 The word that has been to Jeremiah concerning all the Jews who are dwelling in the land of Egypt—who are dwelling in Migdol, and in Tahpanhes, and in Noph, and in the land of Pathros—saying,
Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
2 “Thus said YHWH of Hosts, God of Israel: You have seen all the calamity that I have brought in on Jerusalem, and on all the cities of Judah, and behold, they [are] a desolation to this day, and there is none dwelling in them,
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
3 because of their wickedness that they have done, by provoking Me to anger, by going to make incense, by serving other gods, that they did not know, they, you, and your fathers.
Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
4 And I send to you all My servants the prophets, rising early and sending, saying, Please do not do this abomination that I have hated—
Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
5 and they have not listened nor inclined their ear to turn back from their wickedness, not to make incense to other gods,
Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
6 and My fury is poured out, and My anger, and it burns in cities of Judah, and in streets of Jerusalem, and they are for a ruin, for a desolation, as [at] this day.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
7 And now, thus said YHWH of Hosts, God of Israel: Why are you doing great evil to your own souls, to cut off man and woman, infant and suckling, from you, from the midst of Judah, so as not to leave a remnant to you:
“Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
8 by provoking Me to anger by the works of your hands, by making incense to other gods in the land of Egypt, to where you are going to sojourn, so as to cut yourselves off, and so as to your being for a reviling and for a reproach among all nations of the earth?
Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
9 Have you forgotten the wickedness of your fathers, and the wickedness of the kings of Judah, and the wickedness of their wives, and your own wickedness, and the wickedness of your wives, that they have done in the land of Judah, and in streets of Jerusalem?
Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
10 They have not been humbled to this day, nor have they been afraid, nor have they walked in My law, and in My statutes, that I have set before you and before your fathers.
Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
11 Therefore, thus said YHWH of Hosts, God of Israel: Behold, I am setting My face against you for calamity, even to cut off all Judah,
“Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
12 and I have taken the remnant of Judah, who have set their faces to enter the land of Egypt to sojourn there, and they have all been consumed in the land of Egypt; they fall by sword [and] are consumed by famine, from the least even to the greatest, they die by sword and by famine, and they have been for an execration, for an astonishment, and for a reviling, and for a reproach.
Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
13 And I have seen after those dwelling in the land of Egypt, as I saw after Jerusalem, with sword, with famine, and with pestilence,
Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
14 and there is not an escaped and remaining one of the remnant of Judah, who are entering into the land of Egypt to sojourn there, even to turn back to the land of Judah, to where they are lifting up their soul to return to dwell, for they do not turn back, except those escaping.”
Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
15 And they answer Jeremiah—all the men who are knowing that their wives are making incense to other gods, and all the women who are remaining, a great assembly, even all the people who are dwelling in the land of Egypt, in Pathros—saying:
Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
16 “The word that you have spoken to us in the Name of YHWH—we are not listening to you;
“Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
17 for we certainly do everything that has gone out of our mouth, to make incense to the queen of the heavens, and to pour out drink-offerings to her, as we have done, we, and our fathers, our kings, and our heads, in cities of Judah, and in streets of Jerusalem, and—we are satisfied with bread, and we are well, and we have not seen calamity.
Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
18 And from the time we have ceased to make incense to the queen of the heavens, and to pour out drink-offerings to her, we have lacked all, and we have been consumed by sword and by famine,
Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
19 and when we are making incense to the queen of the heavens, and pouring out drink-offerings to her—have we made cakes for her to idolize her, and to pour out drink-offerings to her, without our husbands?”
Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
20 And Jeremiah says to all the people, concerning the men and concerning the women, and concerning all the people who are answering him, saying,
Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
21 “The incense that you made in the cities of Judah, and in the streets of Jerusalem, you, and your fathers, your kings, and your heads, and the people of the land, has YHWH not remembered it? Indeed, it comes up on His heart.
“Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
22 And YHWH is not able to accept [you] anymore, because of the evil of your doings, because of the abominations that you have done, and your land is for a ruin, and for an astonishment, and for a reviling, without inhabitant, as [at] this day.
Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
23 Because that you have made incense, and because you have sinned against YHWH, and have not listened to the voice of YHWH, and have not walked in His law, and in His statutes, and in His testimonies, therefore this calamity has met you as [at] this day.”
Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
24 And Jeremiah says to all the people, and to all the women, “Hear a word of YHWH, all Judah who [are] in the land of Egypt:
Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
25 Thus spoke YHWH of Hosts, God of Israel, saying, You and your wives both speak with your mouth, and with your hands have fulfilled, saying, We certainly execute our vows that we have vowed, to make incense to the queen of the heavens, and to pour out drink-offerings to her. You certainly establish your vows, and certainly execute your vows.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
26 Therefore, hear a word of YHWH, all Judah who are dwelling in the land of Egypt: Behold, I have sworn by My great Name, said YHWH, My Name is no longer proclaimed by the mouth of any man of Judah, saying, Lord YHWH lives—in all the land of Egypt.
Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
27 Behold, I am watching over them for calamity, and not for good, and all the men of Judah who [are] in the land of Egypt have been consumed by sword and by famine, until their consumption.
Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
28 And the escaped of the sword turn back out of the land of Egypt to the land of Judah, few in number, and all the remnant of Judah, who are coming into the land of Egypt to sojourn there, have known whose word is established, Mine or theirs.
Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
29 And this [is] the sign to you—a declaration of YHWH—that I am seeing after you in this place, so that you know that My words are certainly established against you for calamity—
“Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
30 thus said YHWH: Behold, I am giving Pharaoh-Hophra king of Egypt into the hand of his enemies, and into the hand of those seeking his life, as I have given Zedekiah king of Judah into the hand of Nebuchadnezzar king of Babylon, his enemy, and who is seeking his life.”
Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”

< Jeremiah 44 >