< Jeremiah 28 >

1 And it comes to pass, in that year, in the beginning of the reign of Zedekiah king of Judah, in the fourth year, in the fifth month, Hananiah son of Azur the prophet, who [is] of Gibeon, has spoken to me in the house of YHWH, before the eyes of the priests, and all the people, saying,
Chaka chomwecho mwezi wachisanu wa chaka chachinayi, poyambirira pa ulamuliro wa Zedekiya mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, amene amachokera ku Gibiyoni, anandiwuza ine mʼNyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti,
2 “Thus spoke YHWH of Hosts, God of Israel, saying, I have broken the yoke of the king of Babylon;
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.
3 within two years of days I am bringing back to this place all the vessels of the house of YHWH that Nebuchadnezzar king of Babylon has taken from this place, and carries to Babylon,
Pasanathe zaka ziwiri ndidzabweretsa pa malo ano ziwiya zonse za ku Nyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anazichotsa pa malo pano ndi kupita nazo ku Babuloni.
4 and Jeconiah son of Jehoiakim, king of Judah, and all the expulsion of Judah, who are entering Babylon, I am bringing back to this place—a declaration of YHWH; for I break the yoke of the king of Babylon.”
Ndidzabweretsanso pa malo pano Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda pamodzi ndi akapolo ena onse ochokera ku Yuda amene anapita ku Babuloni,’ akutero Yehova, ‘chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.’”
5 And Jeremiah the prophet says to Hananiah the prophet, before the eyes of the priests, and before the eyes of all the people who are standing in the house of YHWH,
Pamenepo mneneri Yeremiya anayankha mneneri Hananiya pamaso pa ansembe ndi anthu onse amene anasonkhana mʼNyumba ya Yehova.
6 indeed, Jeremiah the prophet says, “Amen! So may YHWH do; YHWH establish your words that you have prophesied, to bring back the vessels of the house of YHWH and all the expulsion from Babylon, to this place.
Anati, “Ameni! Yehova achitedi zomwezo! Yehova akwaniritse mawu amene waloserawo. Iye abweretsenso pa malo pano ziwiya za mʼNyumba ya Yehova ndi akapolo onse kuchokera ku Babuloni.
7 Only, please hear this word that I am speaking in your ears, and in the ears of all the people.
Komabe, tamvera zimene nditi ndikuwuze iweyo pamodzi ndi anthu onse:
8 The prophets who have been before me, and before you, from of old, even they prophesy concerning many lands, and concerning great kingdoms, of battle, and of calamity, and of pestilence.
Kunali aneneri kalelo, ine ndi iwe tisanabadwe. Iwowa analosera za nkhondo, mavuto ndi mliri kuti zidzagwera mayiko ambiri ndi maufumu amphamvu.
9 The prophet who prophesies of peace, by the word of the prophet coming to pass, the prophet is known [as] one whom YHWH has truly sent.”
Koma mneneri amene amalosera zamtendere adzadziwika kuti ndi woona ndi kuti watumidwa ndi Yehova ngati zimene wanenera zachitikadi.”
10 And Hananiah the prophet takes the yoke from off the neck of Jeremiah the prophet, and breaks it,
Pamenepo mneneri Hananiya anachotsa goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya nalithyola,
11 and Hananiah speaks before the eyes of all the people, saying, “Thus said YHWH: Thus I break the yoke of Nebuchadnezzar king of Babylon, within two years of days, from off the neck of all the nations”; and Jeremiah the prophet goes on his way.
ndipo anawuza anthu onse kuti, “Yehova akuti, ‘Umu ndi mmene ndidzathyolere goli la Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonse pasanathe zaka ziwiri.’” Zitatero, mneneri Yeremiya anachoka.
12 And there is a word of YHWH to Jeremiah after the breaking, by Hananiah the prophet, of the yoke from off the neck of Jeremiah the prophet, saying,
Patapita nthawi pangʼono, mneneri Hananiya atathyola goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
13 “Go, and you have spoken to Hananiah, saying, Thus said YHWH: You have broken yokes of wood, and I have made yokes of iron instead of them.
“Pita, kawuze mneneri Hananiya kuti, ‘Yehova akuti: Iwe wathyola goli lamtengo, mʼmalo mwake Ine ndidzayika goli lachitsulo.
14 For thus said YHWH of Hosts, God of Israel: I have put a yoke of iron on the neck of all these nations to serve Nebuchadnezzar king of Babylon, and they have served him, and I have also given the beast of the field to him.”
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonseyi kuti atumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo iwo adzamutumikiradi. Ndipo ndamupatsanso ulamuliro ngakhale pa nyama zakuthengo.’”
15 And Jeremiah the prophet says to Hananiah the prophet, “Now hear, O Hananiah; YHWH has not sent you, and you have caused this people to trust on falsehood.
Ndipo mneneri Yeremiya anawuza mneneri Hananiya kuti, “Tamvera, Hananiya! Iweyo Yehova sanakutume, koma iwe wanyenga anthuwa kuti akhulupirire zabodza.
16 Therefore, thus said YHWH: Behold, I am casting you from off the face of the ground; you die this year, for you have spoken apostasy concerning YHWH.”
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, ‘Ndatsala pangʼono kukuchotsa pa dziko lapansi. Iwe ufa chaka chino chisanathe, chifukwa wakhala ukulalikira zowukira Yehova.’”
17 And Hananiah the prophet dies in that year, in the seventh month.
Mʼmwezi wachisanu ndi chiwiri wa chaka chomwecho, mneneri Hananiya anamwaliradi.

< Jeremiah 28 >