< Hosea 8 >
1 “To your mouth—a horn, As an eagle against the house of YHWH, Because they transgressed My covenant, And against My law they have rebelled.
“Ika lipenga pakamwa pako. Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova chifukwa anthu aphwanya pangano langa ndiponso agalukira lamulo langa.
2 To Me they cry, My God, we—Israel—have known You.
Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 Israel has cast off good, an enemy pursues him.
Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.
4 They have made kings, and not by Me, They have made princes, and I have not known, Their silver and their gold they have made to them idols, So that they are cut off.
Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga. Amasankha akalonga popanda chilolezo changa. Amadzipangira mafano asiliva ndi agolide koma adzawonongeka nawo.
5 Your calf has cast off, O Samaria, My anger has burned against them; Until when are they not capable of purity?
Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe! Mkwiyo wanga wayakira anthuwo. Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 For even it [is] of Israel; a craftsman made it, And it [is] not God, For the calf of Samaria is fragments!
Mafanowa ndi ochokera ku Israeli! Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso; si Mulungu amene anamupanga. Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa, mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 For wind they sow, and a windstorm they reap, Stalk it has none—a shoot not yielding grain, If so be it yield—strangers swallow it up.
“Aisraeli amadzala mphepo ndipo amakolola kamvuluvulu. Tirigu alibe ngala; sadzabala chakudya. Akanabala chakudya alendo akanadya chakudyacho.
8 Israel has been swallowed up, Now they have been among nations, As a vessel in which is no delight.
Israeli wamezedwa, tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina ngati chinthu cha chabechabe.
9 For they have gone up [to] Asshur, A wild donkey alone by himself [is] Ephraim, They have hired lovers!
Pakuti iwo anapita ku Asiriya ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha. Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Also though they hire among nations, Now I gather them, and they are pained a little, From the burden of a king of princes.
Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu, Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi. Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 Because Ephraim multiplied altars to sin, They have been to him altars to sin.
“Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo, maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 I write for him numerous things of My law, As a strange thing they have been reckoned.
Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga, koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 The sacrifices of My offerings! They sacrifice flesh, and they eat, YHWH has not accepted them, Now He remembers their iniquity, And inspects their sin, They return [to] Egypt.
Amapereka nsembe za nyama kwa Ine ndipo iwo amadya nyamayo, koma Yehova sakondwera nazo. Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo: iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 And Israel forgets his Maker, and builds temples, And Judah has multiplied cities of defense, And I have sent a fire into his cities, And it has consumed their palaces!”
Israeli wayiwala Mlengi wake ndipo wamanga nyumba zaufumu; Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga. Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo, moto umene udzatenthe malinga awo.”