< Hosea 7 >

1 “When I give healing to Israel, Then the iniquity of Ephraim is revealed, And the wickedness of Samaria, For they have worked falsehood, And a thief comes in, A troop has stripped off in the street,
Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
2 And they do not say to their heart, [That] I have remembered all their evil, Now their doings have surrounded them, They have been before My face.
Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
3 With their wickedness they make a king glad, And with their lies—princes.
“Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
4 All of them [are] adulterers, Like a burning oven of a baker, He ceases from stirring up after kneading the dough, until its leavening.
Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
5 A day of our king! Princes have defiled themselves [with] the poison of wine, He has drawn out his hand with scorners.
Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
6 For they have drawn near, Their heart [is] as an oven In their lying in wait—their baker sleeps all night, Morning! He is burning as a flaming fire.
Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
7 All of them are warm as an oven, And they have devoured their judges, All their kings have fallen, There is none calling to Me among them.
Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
8 Ephraim! He mixes himself among peoples, Ephraim has been an unturned cake.
“Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
9 Strangers have devoured his power, And he has not known, Also old age has sprinkled [itself] on him, And he has not known.
Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
10 And the excellence of Israel has been humbled to his face, And they have not turned back to their God YHWH, Nor have they sought Him for all this.
Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
11 And Ephraim is as a simple dove without heart, Egypt they called on—[to] Asshur they have gone.
“Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
12 When they go I spread over them My net, As the bird of the heavens I bring them down, I discipline them as their congregation has heard.
Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
13 Woe to them, for they wandered from Me, Destruction to them, for they transgressed against Me, And I ransom them, and they have spoken lies against Me,
Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
14 And have not cried to Me with their heart, but howl on their beds; They assemble themselves for grain and new wine, They turn aside against Me.
Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
15 And I instructed—I strengthened their arms, And concerning Me they think evil!
Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
16 They turn back—not to the Most High, They have been as a deceitful bow, Their princes fall by sword, From the insolence of their tongue, This [is] their derision in the land of Egypt!”
Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.

< Hosea 7 >