< Genesis 43 >

1 And the famine [is] severe in the land;
Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
2 and it comes to pass, when they have finished eating the grain which they brought from Egypt, that their father says to them, “Return, buy for us a little food.”
Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
3 And Judah speaks to him, saying, “The man protesting protested to us, saying, You do not see my face without your brother [being] with you;
Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
4 if you are sending our brother with us, we go down, and buy for you food,
Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
5 and if you are not sending—we do not go down, for the man said to us, You do not see my face without your brother [being] with you.”
Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
6 And Israel says, “Why did you do evil to me, by declaring to the man that you had yet a brother?”
Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
7 And they say, “The man asked diligently concerning us, and concerning our family, saying, Is your father yet alive? Have you a brother? And we declare to him according to the tenor of these things; do we certainly know that he will say, Bring down your brother?”
Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
8 And Judah says to his father Israel, “Send the youth with me, and we arise, and go, and live, and do not die, both we, and you, and our infants.
Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
9 I am guarantor [for] him, from my hand you require him; if I have not brought him to you, and set him before you—then I have sinned against you all the days;
Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
10 for if we had not lingered, surely now we had returned these two times.”
Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
11 And their father Israel says to them, “If so, now, do this: take of the praised thing of the land in your vessels, and take down to the man a present, a little balm, and a little honey, spices and myrrh, nuts and almonds;
Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
12 and double money take in your hand, even the money which is brought back in the mouth of your bags, you take back in your hand, it may be it [is] an oversight.
Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
13 And take your brother, and rise, return to the man;
Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
14 and God Almighty give to you mercies before the man, so that he has sent to you your other brother and Benjamin; and I, when I am bereaved—I am bereaved.”
Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
15 And the men take this present, double money also they have taken in their hand, and Benjamin; and they rise, and go down to Egypt, and stand before Joseph;
Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
16 and Joseph sees Benjamin with them and says to him who [is] over his house, “Bring the men into the house, and slaughter an animal, and make ready, for the men eat with me at noon.”
Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
17 And the man does as Joseph has said, and the man brings in the men into the house of Joseph,
Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
18 and the men are afraid because they have been brought into the house of Joseph, and they say, “For the matter of the money which was put back in our bags at the commencement are we brought in—to roll himself on us, and to throw himself on us, and to take us for servants—our donkeys also.”
Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
19 And they come near to the man who [is] over the house of Joseph, and speak to him at the opening of the house,
Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
20 and say, “O my lord, we really come down at the commencement to buy food;
“Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
21 and it comes to pass, when we have come to the lodging-place, and open our bags, that behold, each one’s money [is] in the mouth of his bag, our money in its weight, and we bring it back in our hand;
koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
22 and other money have we brought down in our hand to buy food; we have not known who put our money in our bags.”
Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
23 And he says, “Peace to you, do not fear: your God and the God of your father has given to you hidden treasure in your bags, your money came to me”; and he brings out Simeon to them.
Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
24 And the man brings in the men into Joseph’s house, and gives water, and they wash their feet; and he gives provender for their donkeys,
Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
25 and they prepare the present until the coming of Joseph at noon, for they have heard that there they eat bread.
Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
26 And Joseph comes into the house, and they bring to him the present which [is] in their hand, into the house, and bow themselves to him, to the earth;
Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
27 and he asks of them of peace and says, “Is your father well? The aged man of whom you have spoken, is he yet alive?”
Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
28 And they say, “Your servant our father [is] well, he is yet alive”; and they bow, and pay respect.
Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
29 And he lifts up his eyes and sees his brother Benjamin, his mother’s son, and says, “Is this your young brother, of whom you have spoken to me?” And he says, “God favor you, my son.”
Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
30 And Joseph hurries, for his bowels have been moved for his brother, and he seeks to weep, and enters the inner chamber, and weeps there;
Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
31 and he washes his face, and goes out, and refrains himself, and says, “Place bread.”
Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
32 And they place for him by himself, and for them by themselves, and for the Egyptians who are eating with him by themselves: for the Egyptians are unable to eat bread with the Hebrews, for it [is] an abomination to the Egyptians.
Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
33 And they sit before him, the firstborn according to his birthright, and the young one according to his youth, and the men wonder one at another;
Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
34 and he lifts up gifts from before him to them, and the gift of Benjamin is five hands more than the gifts of all of them; and they drink, indeed, they drink abundantly with him.
Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.

< Genesis 43 >