< Ezra 1 >

1 And in the first year of Cyrus king of Persia, at the completion of the word of YHWH from the mouth of Jeremiah, has YHWH awoken the spirit of Cyrus king of Persia, and he causes an intimation to pass over into all his kingdom, and also in writing, saying,
Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
2 “Thus said Cyrus king of Persia: YHWH, God of the heavens, has given all kingdoms of the earth to me, and He has laid a charge on me to build a house for Him in Jerusalem, that [is] in Judah;
Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
3 who [is] among you of all His people? His God is with him, and he goes up to Jerusalem, that [is] in Judah, and builds the house of YHWH, God of Israel (He [alone is] God), that [is] in Jerusalem.
Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
4 And everyone who is left, of any of the places where he [is] a sojourner, the men of his place assist him with silver, and with gold, and with goods, and with beasts, along with a free-will offering for the house of God, that [is] in Jerusalem.”
Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
5 And heads of the fathers of Judah and Benjamin rise, and the priests and the Levites, even everyone whose spirit God has awoken, to go up to build the house of YHWH, that [is] in Jerusalem;
Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
6 and all those around them have strengthened [them] with their hands, with vessels of silver, with gold, with goods, and with beasts, and with precious things, apart from all that has been offered willingly.
Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
7 And King Cyrus has brought out the vessels of the house of YHWH that Nebuchadnezzar has brought out of Jerusalem, and puts them in the house of his gods;
Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
8 indeed, Cyrus king of Persia brings them out by the hand of Mithredath the treasurer, and numbers them to Sheshbazzar the prince of Judah.
Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
9 And this [is] their number: dishes of gold thirty, dishes of silver one thousand, knives twenty-nine,
Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
10 basins of gold thirty, basins of silver (seconds) four hundred and ten, other vessels one thousand.
timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
11 All the vessels of gold and of silver [are] five thousand and four hundred; the whole has Sheshbazzar brought up with the going up of the expulsion from Babylon to Jerusalem.
Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.

< Ezra 1 >