< Ezekiel 33 >

1 And there is a word of YHWH to me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
2 “Son of man, speak to the sons of your people, and you have said to them: When I bring a sword on a land, And the people of the land have taken one man out of their borders, And made him their watchman,
“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
3 And he has seen the sword coming against the land, And has blown with a horn, and has warned the people,
Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
4 And the hearer has heard the voice of the horn, and he has not taken warning, And the sword comes in, and takes him away, His blood is on his [own] head.
Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
5 The voice of the horn he heard, And he has not taken warning, his blood is on him, And he who took warning has delivered his soul.
Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
6 And the watchman, when he sees the sword coming in, And he has not blown with a horn, And the people have not been warned, And a sword comes in, And takes away a soul from them, He is taken away in his iniquity, And I require his blood from the hand of the watchman.
Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
7 And you, son of man, I gave you [as] a watchman for the house of Israel, And you have heard a word from My mouth, And you have warned them from Me.
“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
8 In My saying to the wicked, O wicked one—you surely die, And you have not spoken to warn the wicked from his way, He—the wicked—dies in his iniquity, And I require his blood from your hand.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
9 And you, when you have warned the wicked of his way, to turn back from it, And he has not turned back from his way, He dies in his iniquity, And you have delivered your soul.
Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
10 And you, son of man, say to the house of Israel: You have spoken correctly, saying, Surely our transgressions and our sins [are] on us, And we are wasting away in them, How, then, do we live?
“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
11 Say to them, [As] I live—a declaration of Lord YHWH, I do not delight in the death of the wicked, But in the turning of the wicked from his way, and he has lived. Turn back, turn back, from your evil ways! Indeed, why do you die, O house of Israel?
Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
12 And you, son of man, say to the sons of your people: The righteousness of the righteous does not deliver him in the day of his transgression, And the wickedness of the wicked, He does not stumble for it in the day of his turning from his wickedness, And the righteous is not able to live in it in the day of his sinning.
“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
13 In My saying of the righteous: He surely lives, And—he has trusted on his righteousness, And he has done perversity, All his righteous acts are not remembered, And for his perversity that he has done, He dies for it.
Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
14 And in My saying to the wicked: You surely die, And—he has turned back from his sin, And has done judgment and righteousness,
Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
15 (The wicked restores a pledge, he repays [for] plunder), He has walked in the statutes of life, So as not to do perversity, He surely lives—he does not die.
monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
16 All his sin—his sins that he has sinned—are not remembered against him, He has done judgment and righteousness, He surely lives.
Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
17 And the sons of your people have said: The way of the Lord is not pondered, As for them—their way is not pondered.
“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
18 In the turning back of the righteous from his righteousness, And he has done perversity—he dies for it.
Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
19 And in the turning back of the wicked from his wickedness, And he has done judgment and righteousness—he lives by them.
Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
20 And you have said, The way of the Lord is not pondered; I judge each of you according to his ways, O house of Israel.”
Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
21 And it comes to pass, in the twelfth year—in the tenth [month], in the fifth of the month—of our removal, one who is escaped from Jerusalem comes to me, saying, “The city has been struck.”
Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
22 And the hand of YHWH has been to me in the evening, before the coming in of the escaped one, and He opens my mouth until [his] coming to me in the morning, and my mouth is opened, and I have not been silent again.
Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
23 And there is a word of YHWH to me, saying,
Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
24 “Son of man, the inhabitants of these ruins on the ground of Israel are speaking, saying, Abraham has been alone—and he possesses the land, and we [are] many—the land has been given to us for a possession.
“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
25 Therefore say to them, Thus said Lord YHWH: You eat with the blood, And you lift up your eyes to your idols, And you shed blood, Should you then inherit the land?
Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
26 You have stood on your sword, You have done abomination, You have each defiled the wife of his neighbor, Should you then possess the land?
Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
27 Thus you say to them, Thus said Lord YHWH: [As] I live—do they who [are] in the ruins not fall by the sword? And they who [are] on the face of the field, I have given for food to the beast, And they who are in strongholds and in caves die by pestilence.
“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
28 And I have made the land a desolation and an astonishment, And the excellence of its strength has ceased, And mountains of Israel have been desolated, Without anyone passing through.
Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
29 And they have known that I [am] YHWH, In My making the land a desolation and an astonishment, For all their abominations that they have done.
Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
30 And you, son of man, The sons of your people who are speaking about you, By the walls, and in openings of the houses, Have spoken with one another, each with his brother, Saying, Please come in, And hear what the word [is] that comes out from YHWH.
“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
31 And they come in to you as the coming in of a people, And they sit before you—My people, And have heard your words, and they do not do them, For they are making unhealthy loves with their mouth, Their heart is going after their dishonest gain.
Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
32 And behold, you [are] as a singer of unhealthy loves to them, A beautiful voice, and playing well on an instrument, And they have heard your words, and they are not doing them.
Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
33 And in its coming in—behold, it has come, And they have known that a prophet has been in their midst!”
“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”

< Ezekiel 33 >