< Ezekiel 11 >
1 And [the] Spirit lifts me up, and it brings me to the east gate of the house of YHWH, that is facing the east, and behold, at the opening of the gate [are] twenty-five men, and I see in their midst Jaazaniah son of Azzur, and Pelatiah son of Benaiah, heads of the people.
Pamenepo Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kubwera nane ku chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Kumeneko pa khomo la chipata panali anthu 25, ndipo ndinaona pakati pawo atsogoleri awa: Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya.
2 And He says to me, “Son of man, these [are] the men who are devising iniquity, and who are giving evil counsel in this city;
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi anthu amene akukonza zoyipa ndi kupereka malangizo oyipa mu mzindamo.
3 who are saying, It [is] not near—to build houses, it [is] the pot, and we [are] the flesh.
Iwo amawuza anthu kuti, ‘Nthawi sinafike yoti timange Nyumba? Mzindawu uli ngati mʼphika umene uli pa moto ndipo ife tili ngati nyama mu mʼphikamo.
4 Therefore prophesy concerning them, prophesy, son of man.”
Choncho iwe mwana wa munthu, unenere mowadzudzula. Nenera ndithu.’”
5 And [the] Spirit of YHWH falls on me, and He says to me, “Say, Thus said YHWH: You have said correctly, O house of Israel, And I have known the steps of your spirit.
Ndipo Mzimu wa Yehova unandigwera ndipo unandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Yehova ndi izi. Iye akuti. ‘Izi ndi zimene mukunena, Inu Aisraeli, koma Ine ndikudziwa zimene zili mu mtima mwanu.’
6 You multiplied your wounded in this city, And filled its out-places with the wounded.
Mwapha anthu ambiri mu mzinda muno ndipo mwadzaza misewu yake ndi mitembo.
7 Therefore, thus said Lord YHWH: Your wounded whom you placed in its midst, They [are] the flesh, and it [is] the pot, And He has brought you out from its midst.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mitembo imene mwayiponya mʼmisewuyo ndiyo nyama ndipo mzinda uno ndiwo mʼphika, koma Ine ndidzakuthamangitsanimo.
8 You have feared a sword, And I bring in a sword against you, A declaration of Lord YHWH.
Inu mumaopa lupanga, koma lupangalo ndi limene ndidzakubweretsereni, akutero Ambuye.
9 And I have brought you out of its midst, And given you into the hand of strangers, And I have done judgments among you.
Ine ndidzakuthamangitsani mu mzinda ndipo ndidzakuperekani mʼdzanja la alendo kuti akulangeni.
10 You fall by the sword, I judge you on the border of Israel, And you have known that I [am] YHWH.
Mudzaphedwa ndi lupanga ndipo ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
11 It is not for a pot for you, Nor are you for flesh in its midst, I judge you at the border of Israel.
Mzinda uno sudzakhala ngati mʼphika wokutetezani ndipo simudzakhalanso ngati nyama ya mʼmenemo. Ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli.
12 And you have known that I [am] YHWH, For you have not walked in My statutes, And you have not done My judgments, And according to the judgments of the nations Who are around you, you have done!”
Ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Inu simunatsatire malangizo anga kapena kusunga malamulo anga koma mwakhala mukutsata zochita za mitundu ina ya anthu imene yakuzungulirani.’”
13 And it comes to pass, at my prophesying, that Pelatiah son of Benaiah is dying, and I fall on my face, and cry—a loud voice—and say, “Aah! Lord YHWH, You are making an end of the remnant of Israel.”
Tsono pamene ndinkanenera, Pelatiya mwana wa Benaya anafa. Pomwepo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba ndipo ndinafuwula ndi mawu aakulu kuti “Mayo, Ambuye Yehova! Kodi mudzawatheratu Aisraeli onse otsala?”
14 And there is a word of YHWH to me, saying,
Yehova anayankhula nane kuti,
15 “Son of man, your brothers, your brothers, men of your family, and all the house of Israel—all of it—[are] they to whom inhabitants of Jerusalem have said, Keep far off from YHWH;
“Anthu okhala ku Yerusalemu akuwanena abale ako, anthu a ku ukapolo, onse a banja la Israeli, kuti, ‘Anthu onse amene anatengedwa ukapolo ali kutali ndi Yehova. Dziko lanu Yehova anatipatsa kuti likhale lathulathu.’”
16 it [is] ours, the land has been given for an inheritance; therefore say, Thus said Lord YHWH: Because I put them far off among nations, And because I scattered them through lands, I am also for a little sanctuary to them, In lands to where they have gone in.
“Nʼchifukwa chake nena kwa anzako a ku ukapolo kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Ine ndinawatumiza kutali pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinawabalalitsa ku mayiko ambiri. Komabe ndakhala ndikuwasunga ku mayiko kumene anapitako!’
17 Therefore say, Thus said Lord YHWH: And I have assembled you from the peoples, And I have gathered you from the lands, Into which you have been scattered, And I have given the ground of Israel to you.
“Nʼchifukwa chake uwawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kuti, Ndidzawasonkhanitsa kuchokera kwa anthu a mitundu inayo ndi kuwasonkhanitsira pamodzi kuchokera ku mayiko kumene ndinawabalalitsirako. Pambuyo pake ndidzawapatsa dziko la Israeli.
18 And they have gone in there, And turned aside all its detestable things, And all its abominations—out of it.
“Akadzalowa mʼdzikomo adzachotsa mafano awo onse oyipa ndi onyansa.
19 And I have given one heart to them, And I give a new spirit in your midst, And I have turned the heart of stone out of their flesh, And I have given a heart of flesh to them.
Ndidzawapatsa mtima watsopano ndipo ndidzayika mzimu watsopano mwa iwo. Ndidzachotsa mtima wowuma ngati mwala mwa iwo, ndipo ndidzawapatsa mtima wofewa ngati mnofu.
20 So that they walk in My statutes, And keep My judgments, and have done them, And they have been to Me for a people, And I am to them for God.
Motero adzatsata malamulo anga ndipo adzasunga mosamala malamulo anga. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
21 As for those whose heart is going to the heart Of their detestable things and their abominations, I have put their way on their head, A declaration of Lord YHWH.”
Koma kunena za amene akupembedza mafano oyipa ndi onyansa, ndidzawalanga chifukwa cha zimene achita. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
22 And the cherubim lift up their wings, and the wheels [are] alongside them, and the glory of the God of Israel [is] over them above.
Tsono akerubi aja anatambasula mapiko awo kuyamba kuwuluka, mikombero ili mʼmbali mwawo. Ulemerero wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
23 And the glory of YHWH goes up from off the midst of the city, and stands on the mountain, that [is] on the east of the city.
Ulemerero wa Yehova unakwera ndi kusiya mzindawo ndipo unakayima pa phiri cha kummawa kwake kwa mzindawo.
24 And [the] Spirit has lifted me up, and brings me to Chaldea, to the expulsion, in a vision, by [the] Spirit of God, and the vision that I have seen goes up from off me;
Pambuyo pake Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kukandifikitsa. Zimenezi zinkachitika mʼmasomphenya monga mmene Mzimu wa Mulungu unkandionetsera. Kenaka masomphenya amene ndinkawaonawo anayamba kuzimirira.
25 and I speak to the expulsion all the matters of YHWH that He has showed me.
Ndipo ndinafotokozera akapolowo zonse zimene Yehova anandionetsa.