< Exodus 11 >

1 And YHWH says to Moses, “One more plague I bring in on Pharaoh and on Egypt, afterward he sends you away from this; when he is sending you away, he surely casts you out from this [place] altogether;
Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani.
2 now speak in the ears of the people, and they ask—each man from his neighbor, and each woman from her neighbor—[for] vessels of silver and vessels of gold.”
Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.”
3 And YHWH gives the grace of the people in the eyes of the Egyptians; also the man Moses [is] very great in the land of Egypt, in the eyes of the servants of Pharaoh, and in the eyes of the people.
Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.
4 And Moses says, “Thus said YHWH: About midnight I am going out into the midst of Egypt,
Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto.
5 and every firstborn in the land of Egypt has died, from the firstborn of Pharaoh who is sitting on his throne, to the firstborn of the maidservant who [is] behind the millstones, and all the firstborn of beasts;
Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto.
6 and there has been a great cry in all the land of Egypt, such as there has not been, and such as there is not again;
Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso.
7 and against all the sons of Israel a dog does not sharpen its tongue, from man even to beast, so that you know that YHWH makes a separation between the Egyptians and Israel.
Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli.
8 And all these servants of yours have come down to me, and bowed themselves to me, saying, Go out, you and all the people who [are] at your feet; and afterward I go out”; and he goes out from Pharaoh in the heat of anger.
Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.
9 And YHWH says to Moses, “Pharaoh does not listen to you, so as to multiply My wonders in the land of Egypt”;
Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.”
10 and Moses and Aaron have done all these wonders before Pharaoh, and YHWH strengthens Pharaoh’s heart, and he has not sent the sons of Israel out of his land.
Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.

< Exodus 11 >