< Esther 3 >
1 After these things has King Ahasuerus exalted Haman son of Hammedatha the Agagite, and lifts him up, and sets his throne above all the heads who [are] with him,
Zitachitika izi, mfumu Ahasiwero anamukweza Hamani mwana wa Hamedata Mwagagi, anamulemekeza ndikumupatsa mpando wa ulemu kuposa nduna zina zonse.
2 and all servants of the king, who [are] in the gate of the king, are bowing and doing homage to Haman, for so the king has commanded for him; and Mordecai does not bow nor pay respect.
Atumiki onse a mfumu amene anali pa chipata cha nyumba ya mfumu ankagwadira ndi kuweramira Hamani monga mwa lamulo la mfumu. Koma Mordekai sankamugwadira kapena kumuweramira.
3 And the servants of the king, who [are] in the gate of the king, say to Mordecai, “Why [are] you transgressing the command of the king?”
Kenaka atumiki a mfumu amene anali pa chipata anafunsa Mordekai kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani sumvera lamulo la mfumu?”
4 And it comes to pass, in their speaking to him, day by day, and he has not listened to them, that they declare [it] to Haman, to see whether the words of Mordecai stand, for he has declared to them that he [is] a Jew.
Tsiku ndi tsiku ankayankhula naye koma iye sanamverebe. Choncho anamuwuza Hamani kuti aone ngati angavomereze khalidwe lotere la Mordekai, popeza anawawuza kuti anali Myuda.
5 And Haman sees that Mordecai is not bowing and doing homage to him, and Haman is full of fury,
Hamani ataona kuti Mordekai sankamugwadira kapena kumuweramira, anapsa mtima kwambiri.
6 and it is contemptible in his eyes to put forth a hand on Mordecai by himself, for they have declared to him the people of Mordecai, and Haman seeks to destroy all the Jews who [are] in all the kingdom of Ahasuerus—the people of Mordecai.
Hamani atamva kuti Mordekai anali Myuda, anatsimikiza kuti ndi kosakwanira kulanga Mordekai yekha. Mʼmalo mwake anapeza njira yowonongera Ayuda onse okhala mʼdziko lonse limene mfumu Ahasiwero ankalamulira.
7 In the first month—it [is] the month of Nisan—in the twelfth year of King Ahasuerus, has one caused to fall Pur (that [is] the lot) before Haman, from day to day, and from month to month, [to] the twelfth, it [is] the month of Adar.
Mwezi woyamba, umene ndi mwezi wa Nisani, chaka cha khumi ndi chiwiri cha ufumu wa Ahasiwero anachita maere, otchedwa Purimu pamaso pa Hamani kuti apeze tsiku ndi mwezi woyenera. Ndipo maere anagwera pa mwezi wa khumi ndi chiwiri ndiwo mwezi wa Adara.
8 And Haman says to King Ahasuerus, “There is one people scattered and separated among the peoples, in all provinces of your kingdom, and their laws [are] diverse from all people, and the laws of the king they are not doing, and for the king it is not profitable to permit them;
Kenaka Hamani anakawuza mfumu Ahasiwero kuti, “Pali mtundu wina wa anthu umene unabalalika ndipo wamwazikana pa mitundu ina mʼzigawo zonse za ufumu wanu umene miyambo yawo ndi yosiyana ndi ya anthu ena onse ndiponso amene safuna kumvera malamulo a mfumu, kotero si chinthu cha phindu kuti mfumu iwalekerere anthu otere.
9 if to the king [it be] good, let it be written to destroy them, and ten thousand talents of silver I weigh into the hands of those doing the work, to bring [it] into the treasuries of the king.”
Ngati chingakukomereni mfumu, ikani lamulo kuti tiwawononge, ndipo ndidzalipira matalente 10,000 asiliva mosungiramo chuma cha mfumu za anthu amene adzachite ntchito imeneyi.”
10 And the king turns aside his signet from off his hand, and gives it to Haman son of Hammedatha the Agagite, adversary of the Jews;
Choncho mfumu inavula mphete yodindira ku chala chake ndi kumupatsa Hamani mwana wa Hamedata Mwagagi, mdani wa Ayuda.
11 and the king says to Haman, “The silver is given to you, and the people, to do with it as [it is] good in your eyes.”
Mfumu inati kwa Hamani, “Sunga ndalamazo, ndipo uchite ndi anthuwo monga ufunira.”
12 And scribes of the king are called, on the first month, on the thirteenth day of it, and it is written according to all that Haman has commanded, to lieutenants of the king, and to the governors who [are] over province and province, and to the heads of people and people, province and province, according to its writing, and people and people according to its tongue, in the name of King Ahasuerus it has been written and sealed with the signet of the king,
Alembi analemba zonse zimene Hamani analamula mʼmakalata opita kwa akazembe a mfumu, abwanamkubwa a zigawo zonse ndi kwa oyangʼanira mtundu uliwonse wa anthu. Kalatazo zinali za mʼchiyankhulo cha mtundu uliwonse ndipo zinalembedwa mʼdzina la Mfumu Ahasiwero ndi kusindikizidwa ndi mphete yake.
13 and letters to be sent by the hand of the runners to all provinces of the king, to cut off, to slay, and to destroy all the Jews, from young even to old, infant and women, on one day, on the thirteenth of the twelfth month—it [is] the month of Adar—and to seize their spoil,
Makalatawa anawatumiza amithenga ku zigawo zonse za mfumu kuti awononge, aphe ndi kufafaniziratu a Yuda onse, anyamata, anthu okalamba, ana ndi amayi, pa tsiku limodzi la 13 la mwezi wa Adara ndipo alande katundu wawo.
14 a copy of the writing to be made law in each and every province is revealed to all the peoples, to be ready for this day.
Mwachidule kalatayi inanena kuti mawu olembedwamowo anayenera kuperekedwa ngati lamulo mʼchigawo chilichonse ndi kuti anthu a mtundu uliwonse adziwe ndi kukhala okonzeka pa tsikulo.
15 The runners have gone forth, hurried by the word of the king, and the law has been given in Shushan the palace, and the king and Haman have sat down to drink, and the city Shushan is perplexed.
Potsata lamulo la mfumu, amithenga aja anapita mwachangu ndipo lamuloli linaperekedwanso ku Susa, likulu la dziko. Mfumu ndi Hamani anakhala pansi ndikumamwa, koma mzinda onse wa Susa unasokonezeka.