< Deuteronomy 8 >

1 “All the command which I am commanding you today you observe to do, so that you live, and have multiplied, and gone in, and possessed the land which YHWH has sworn to your fathers;
Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
2 and you have remembered all the way which your God YHWH has caused you to go these forty years in the wilderness, in order to humble you to try you, to know that which [is] in your heart, whether you keep His commands or not.
Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
3 And He humbles you, and causes you to hunger, and causes you to eat the manna (which you have not known, even your fathers have not known), in order to cause you to know that man does not live by bread alone, but man lives by everything proceeding [from] the mouth of YHWH.
Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
4 Your raiment has not worn out from off you, and your foot has not swelled these forty years,
Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
5 and you have known with your heart that as a man disciplines his son, your God YHWH is disciplining you,
Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
6 and you have kept the commands of your God YHWH, to walk in His ways and to fear Him.
Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
7 For your God YHWH is bringing you into a good land, a land of brooks of waters, of fountains, and of depths coming out in valley and in mountain;
Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
8 a land of wheat, and barley, and vine, and fig, and pomegranate; a land of oil olive and honey;
dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
9 a land in which you eat bread without scarcity—you do not lack anything in it; a land whose stones [are] iron, and you dig bronze out of its mountains.
dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
10 And you have eaten and been satisfied, and have blessed your God YHWH on the good land which he has given to you.
Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
11 Take heed to yourself lest you forget your God YHWH so as not to keep His commands, and His judgments, and His statutes which I am commanding you today;
Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
12 lest you eat and have been satisfied, and build good houses and have inhabited [them],
kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
13 and your herd and your flock are multiplied, and silver and gold are multiplied to you, and all that is yours is multiplied,
ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
14 and your heart has been high, and you have forgotten your God YHWH who is bringing you out of the land of Egypt, out of a house of servants;
mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
15 who is causing you to go in the great and the terrible wilderness [with] burning serpent, and scorpion, and thirst—where there is no water; who is bringing out waters to you from the flinty rock;
Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
16 who is causing you to eat manna in the wilderness, which your fathers have not known, in order to humble you, and in order to try you, to do you good in your latter end;
Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
17 and you have said in your heart, My power and the might of my hand have made this wealth for me.
Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
18 And you have remembered your God YHWH, for it [is] He who is giving power to you to make wealth, in order to establish His covenant which He has sworn to your fathers, as [at] this day.
Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
19 And it has been, if you really forget your God YHWH, and have gone after other gods, and served them, and bowed yourself to them, I have testified against you today that you utterly perish.
Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
20 As the nations whom YHWH is destroying from your presence, so you perish, because you do not listen to the voice of your God YHWH.”
Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.

< Deuteronomy 8 >