< Deuteronomy 29 >
1 These [are] the words of the covenant which YHWH has commanded Moses to make with the sons of Israel in the land of Moab, apart from the covenant which He made with them in Horeb.
Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
2 And Moses calls to all Israel and says to them, “You have seen all that which YHWH has done before your eyes in the land of Egypt, to Pharaoh, and to all his servants, and to all his land—
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
3 the great trials which your eyes have seen, the signs, and those great wonders.
Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
4 And YHWH has not given to you a heart to know, and eyes to see, and ears to hear, until this day.
Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
5 And I cause you to go in a wilderness [for] forty years; your garments have not been consumed from off you, and your shoe has not worn away from off your foot;
Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
6 you have not eaten bread, and you have not drunk wine and strong drink, so that you know that I [am] your God YHWH.
Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
7 And you come to this place, and Sihon king of Heshbon—also Og king of Bashan—comes out to meet us to battle, and we strike them,
Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
8 and take their land, and give it for an inheritance to the Reubenite, and to the Gadite, and to the half of the tribe of the Manassite;
Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
9 and you have kept the words of this covenant and done them, so that you cause all that you do to prosper.
Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
10 You are standing today, all of you, before your God YHWH: your heads, your tribes, your elderly, and your authorities, every man of Israel,
Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
11 your infants, your wives, and your sojourner who [is] in the midst of your camps, from the hewer of your wood to the drawer of your water,
pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
12 for your passing over into the covenant of your God YHWH, and into His oath which your God YHWH is making with you today,
Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
13 in order to establish you to Himself for a people today, and He Himself is your God, as He has spoken to you, and as He has sworn to your fathers, to Abraham, to Isaac, and to Jacob.
kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
14 And I am not making this covenant and this oath with you alone,
Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
15 but with him who is here with us, standing before our God YHWH today, and with him who is not here with us today,
amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
16 for you have known how you dwelt in the land of Egypt, and how we passed by through the midst of the nations which you have passed by;
Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
17 and you see their abominations, and their idols of wood and stone, silver and gold, which [are] with them,
Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
18 lest there be among you a man or woman, or family or tribe, whose heart is turning from our God YHWH today, to go to serve the gods of those nations, lest there be in you a root bearing the fruit of gall and wormwood;
Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
19 and it has been, in his hearing the words of this oath, that he has blessed himself in his heart, saying, I have peace, though I go on in the stubbornness of my heart—in order to sweep away the watered with the thirsty.
Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
20 YHWH is not willing to be propitious to him, for then the anger of YHWH smokes, also His zeal, against that man, and all the oath which is written in this scroll has lain down on him, and YHWH has blotted out his name from under the heavens,
Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
21 and YHWH has separated him for calamity out of all the tribes of Israel, according to all the oaths of the covenant which is written in this Scroll of the Law.
Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
22 And the latter generation of your sons who rise after you, and the stranger who comes in from a far-off land, have said, when they have seen the strokes of that land and its sicknesses which YHWH has sent into it:
Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
23 The whole land is burned [with] brimstone and salt, it is not sown, nor does it shoot up, nor does any herb go up on it there, like the overthrow of Sodom and Gomorrah, Admah and Zeboim, which YHWH overturned in His anger and in His fury.
Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
24 Indeed, all the nations have said, Why has YHWH done thus to this land? Why the heat of this great anger?
Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
25 And they have said, Because that they have forsaken the covenant of YHWH, God of their fathers, which He made with them in His bringing them out of the land of Egypt,
Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
26 and they go and serve other gods, and bow themselves to them—gods which they have not known, and which He has not apportioned to them;
Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
27 and the anger of YHWH burns against that land, to bring in on it all the reviling that is written in this scroll,
Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
28 and YHWH plucks them from off their ground in anger, and in fury, and in great wrath, and casts them into another land, as [at] this day.
Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
29 The things hidden [belong] to our God YHWH, and the things revealed [belong] to us and to our sons for all time, to do all the words of this law.”
Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.