< Colossians 1 >

1 Paul, an apostle of Jesus Christ through the will of God, and Timotheus the brother,
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
2 to the holy ones in Colossae, and to the faithful brothers in Christ: Grace to you and peace from God our Father and the Lord Jesus Christ!
Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
3 We give thanks to the God and Father of our Lord Jesus Christ, always praying for you,
Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
4 having heard of your faith in Christ Jesus, and of the love that [is] to all the holy ones,
Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
5 because of the hope that is laid up for you in the heavens, which you heard of beforehand by the word of the truth of the good news,
Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
6 which has come to you, as also in all the world, and is bearing fruit, as also in you, from the day in which you heard, and knew the grace of God in truth,
umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
7 as you also learned from Epaphras, our beloved fellow-servant, who is a faithful servant of the Christ for you,
Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
8 who also declared to us your love in the Spirit.
Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
9 Because of this, we also, from the day in which we heard, do not cease praying for you, and asking that you may be filled with the full knowledge of His will in all wisdom and spiritual understanding,
Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
10 to walk worthily of the LORD, pleasing in all, being fruitful in every good work, and increasing in the knowledge of God,
Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
11 in all might being made mighty according to the power of His glory, to all endurance and long-suffering with joy.
Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
12 Giving thanks to the Father who has qualified us for the participation of the inheritance of the holy ones in the light,
ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
13 who rescued us out of the authority of the darkness, and translated [us] into the kingdom of the Son of His love,
Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
14 in whom we have the redemption [[through His blood]], the forgiveness of sins,
Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
15 who is the image of the invisible God, firstborn of all creation,
Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
16 because all things were created in Him, those in the heavens, and those on the earth, those visible, and those invisible, whether thrones, whether lordships, whether principalities, whether authorities; all things have been created through Him and for Him,
Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
17 and He is before all, and all things have consisted in Him.
Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
18 And He is the head of the body—the Assembly—who is a beginning, a firstborn out of the dead, that He might become first in all [things] Himself,
Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
19 because all the fullness was pleased to dwell in Him,
Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
20 and through Him to reconcile all things to Himself—having made peace through the blood of His Cross—through Him, whether the things on the earth, whether the things in the heavens.
Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
21 And you—once being alienated, and enemies in the mind, in the evil works, yet now He reconciled,
Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
22 in the body of His flesh through death, to present you holy, and unblemished, and unblameable before Himself,
Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
23 if you also remain in the faith, being founded and settled, and not moved away from the hope of the good news, which you heard, which was preached in all the creation that [is] under Heaven, of which I, Paul, became a servant.
ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
24 I now rejoice in my sufferings for you, and fill up the things lacking of the tribulations of the Christ in my flesh for His body, which is the Assembly,
Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
25 of which I became a servant according to the dispensation of God, that was given to me for you, to fulfill the word of God,
Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
26 the secret that has been hid from the ages and from the generations, but now was revealed to His holy ones, (aiōn g165)
chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
27 to whom God willed to make known what [is] the riches of the glory of this secret among the nations—which is Christ in you, the hope of the glory,
Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
28 whom we proclaim, warning every man, and teaching every man, in all wisdom, that we may present every man perfect in Christ Jesus,
Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
29 for which I also labor, striving according to His working that is working in me in power.
Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.

< Colossians 1 >