< Acts 8 >
1 And Saul was assenting to his death, and there came in that day a great persecution on the Assembly in Jerusalem, all were also scattered abroad in the regions of Judea and Samaria, except the apostles;
Ndipo Saulo anavomerezana nawo pa imfa ya Stefano. Tsiku lomwelo, mpingo wa mu Yerusalemu unayamba kuzunzidwa, ndipo onse, kupatulapo atumwi, anabalalikira ku madera onse a Yudeya ndi Samariya.
2 and devout men carried Stephen away, and made great lamentation over him;
Anthu okonda Mulungu anayika maliro a Stefano ndipo anamulira kwambiri.
3 and Saul was making havoc of the Assembly, entering into every house, and dragging away men and women, giving them up to prison;
Koma Saulo anayamba kuwononga mpingo. Amapita nyumba ndi nyumba, ndipo amagwira amuna ndi amayi ndi kukawatsekera ku ndende.
4 they then indeed, having been scattered, went abroad proclaiming good news—the word.
Okhulupirira amene anabalalika amalalikira konse kumene amapita.
5 And Philip having gone down to a city of Samaria, was preaching the Christ to them;
Filipo anapita ku mzinda wa ku Samariya ndipo analalikira za Khristu kumeneko.
6 the multitudes were also giving heed to the things spoken by Philip, with one accord, in their hearing and seeing the signs that he was doing,
Gulu la anthu litamva Filipo akulalikira komanso kuona zizindikiro zozizwitsa zimene ankazichita, onse anamvetsetsa zimene iye amanena.
7 for unclean spirits came forth from many who were possessed, crying with a loud voice, and many who have been paralytic and lame were healed,
Mizimu yoyipa inatuluka mwa anthu ambiri ikufuwula kwambiri ndipo ambiri amene anali akufa ziwalo ndi olumala anachiritsidwa.
8 and there was great joy in that city.
Kotero munali chimwemwe chachikulu mu mzindawo.
9 And a certain man, by name Simon, was previously in the city using magic, and amazing the nation of Samaria, saying himself to be a certain great one,
Koma mu mzindawo munali munthu dzina lake Simoni, amene amachita za matsenga ndi kudabwitsa anthu a mu Samariya. Iye amadzitamandira kuti ndi wopambana,
10 to whom they were all giving heed, from small to great, saying, “This one is the great power of God”;
ndipo anthu onse, aakulu ndi aangʼono anamumvera ndi kunena kuti, “Munthu uyu ndi mphamvu ya Mulungu yotchedwa Mphamvu yayikulu.”
11 and they were giving heed to him, because of his having amazed them for a long time with deeds of magic.
Anthu amamutsata chifukwa kwa nthawi yayitali amawadabwitsa ndi matsenga akewo.
12 And when they believed Philip, proclaiming good news, the things concerning the Kingdom of God and the Name of Jesus Christ, they were immersed—both men and women;
Koma atakhulupirira Filipo akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ndiponso dzina la Yesu Khristu, anthuwo anabatizidwa amuna ndi amayi.
13 and Simon himself also believed, and having been immersed, he was continuing with Philip, beholding also signs and mighty acts being done, he was amazed.
Nayenso Simoni anakhulupirira ndipo anabatizidwa, natsatira Filipo kulikonse, ndipo anadabwa kwambiri pamene anaona zizindikiro zazikulu ndi zozizwitsa.
14 And the apostles in Jerusalem having heard that Samaria has received the word of God, sent Peter and John to them,
Atumwi a ku Yerusalemu atamva kuti anthu a ku Samariya analandira Mawu a Mulungu, anatumiza Petro ndi Yohane.
15 who having come down prayed concerning them, that they may receive the Holy Spirit—
Atafika anawapempherera kuti alandire Mzimu Woyera,
16 for as yet He was fallen on none of them, and only they have been immersed—into the Name of the Lord Jesus;
chifukwa Mzimu Woyera anali asanafike pa wina aliyense wa iwo; anali atangobatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu.
17 then they were laying hands on them, and they received the Holy Spirit.
Ndipo Petro ndi Yohane anasanjika manja awo pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.
18 And Simon, having beheld that through the laying on of the hands of the apostles the Holy Spirit is given, brought money before them,
Simoni ataona kuti Mzimu anaperekedwa kwa iwo atumwi atawasanjika manja, iye anafuna kuwapatsa ndalama ndipo anati,
19 saying, “Give also to me this authority, that on whomsoever I may lay the hands, he may receive the Holy Spirit.”
“Inenso ndipatseni mphamvu imeneyi kuti aliyense amene ndimusanjika manja anga azilandira Mzimu Woyera.”
20 And Peter said to him, “Your silver with you—may it be to destruction! Because you thought to possess the gift of God through money;
Petro anayankha kuti, “Ndalama zako utayike nazo pamodzi, chifukwa unaganiza kuti ungathe kugula mphatso ya Mulungu ndi ndalama!
21 you have neither part nor lot in this thing, for your heart is not right before God;
Ulibe gawo kapena mbali pa utumikiwu, chifukwa mtima wako suli wolungama pamaso pa Mulungu.
22 convert, therefore, from this your wickedness, and implore God, if then the purpose of your heart may be forgiven you,
Lapa zoyipa zakozi ndipo upemphere kwa Ambuye. Mwina adzakukhululukira maganizo a mu mtima mwako.
23 for in the gall of bitterness, and bond of unrighteousness, I perceive you being.”
Pakuti ine ndikuona kuti ndiwe wowawidwa mtima ndiponso kapolo wa tchimo.”
24 And Simon answering, said, “Implore for me to the LORD, that nothing may come on me of the things you have spoken.”
Ndipo Simoni anayankha, “Mundipempherere kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.”
25 They indeed, therefore, having testified fully, and spoken the word of the LORD, turned back to Jerusalem; they also proclaimed good news in many villages of the Samaritans.
Atatha kuchitira umboni ndi kulalikira mawu a Ambuye, Petro ndi Yohane anabwerera ku Yerusalemu, atalalikira Uthenga Wabwino mʼmidzi yambiri ya Asamariya.
26 And a messenger of the LORD spoke to Philip, saying, “Arise, and go on toward the south, on the way that is going down from Jerusalem to Gaza.” (This is desolate.)
Mngelo wa Ambuye anati kwa Filipo, “Nyamuka pita chakummwera, ku msewu wa ku chipululu wopita ku Gaza kuchokera ku Yerusalemu.”
27 And having arisen, he went on, and behold, a man of Ethiopia, a eunuch, a man of rank, of Candace the queen of the Ethiopians, who was over all her treasure, who had come to Jerusalem to worship;
Ndipo ananyamuka napita, ndipo akuyenda anakumana ndi munthu wa ku Etiopia wa udindo waukulu woyangʼanira chuma cha Kandake, mfumu yayikazi ya ku Etiopia. Munthu ameneyu anapita ku Yerusalemu kukapembedza Mulungu,
28 he was also returning, and is sitting on his chariot, and he was reading the prophet Isaiah.
ndipo akubwerera kwawo atakwera pa galeta lake amawerenga buku la mneneri Yesaya.
29 And the Spirit said to Philip, “Go near, and be joined to this chariot”;
Mzimu anamuwuza Filipo kuti, “Pita pa galeta ilo ndipo ukakhale pafupi nalo.”
30 and Philip having run near, heard him reading the prophet Isaiah and said, “Do you then know what you read?”
Pamenepo Filipo anathamangira ku galeta ndipo anamva munthuyo akuwerenga buku la mneneri Yesaya. Filipo anamufunsa kuti, “Kodi mukumvetsa zimene mukuwerengazi?”
31 And he said, “Why, how am I able, if someone may not guide me?” He called Philip also, having come up, to sit with him.
Iye anayankha kuti, “Ndingamvetse bwanji popanda wina wondimasulira?” Ndipo iye anayitana Filipo kuti abwere ndikukhala naye mʼgaleta.
32 And the passage of the Writing that he was reading was this: “He was led as a sheep to slaughter, And as a lamb before his shearer is silent, So He does not open His mouth;
Mawu amene ndunayo imawerenga anali awa: “Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
33 In His humiliation His judgment was taken away, And His generation—who will declare? Because His life is taken from the earth.”
Iye ananyozedwa ndipo panalibe chilungamo pa mlandu wake. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?”
34 And the eunuch answering Philip said, “I beg you, about whom does the prophet say this? About himself, or about some other one?”
Ndunayo inamufunsa Filipo kuti, “Chonde, uzeni, kodi mneneri akuyankhula za ndani, za iye mwini kapena za munthu wina?”
35 And Philip having opened his mouth, and having begun from this Writing, proclaimed good news to him—Jesus.
Pamenepo Filipo anayambira pa malemba omwewo kumuwuza za Uthenga Wabwino wa Yesu.
36 And as they were going on the way, they came on some water, and the eunuch said, “Behold, water; what hinders me to be immersed?”
Akuyenda mu msewu anafika pamalo pamene panali madzi ndipo ndunayo inati, “Taonani madzi awa. Kodi pali chondiletsa kuti ndibatizidwe?”
37 [[And Philip said, “If you believe out of all the heart, it is lawful”; and he answering said, “I believe Jesus Christ to be the Son of God”; ]]
Filipo anati, “Ngati mukhulupirira ndi mtima wanu wonse mukhoza kubatizidwa.” Ndunayo inayankha kuti, “Ine ndikukhulupirira kuti Yesu Khristu ndi Mwana wa Mulungu.”
38 and he commanded the chariot to stand still, and they both went down to the water, both Philip and the eunuch, and he immersed him;
Ndipo analamulira galeta kuti liyime. Onse awiriwo, Filipo ndi Ndunayo anatsika ndi kulowa mʼmadzi ndipo Filipo anamubatiza.
39 and when they came up out of the water, the Spirit of the LORD snatched up Philip, and the eunuch saw him no more, for he was going on his way rejoicing;
Pamene iwo anatuluka mʼmadzimo, Mzimu wa Ambuye anamukwatula Filipo, ndipo Ndunayo sinamuonenso, koma inapitiriza ulendo wake ikusangalala.
40 and Philip was found at Azotus, and passing through, he was proclaiming good news to all the cities, until his coming to Caesarea.
Koma Filipo anapezeka kuti ali ku Azoto ndipo anazungulira konse, kulalikira Uthenga Wabwino mʼmizinda yonse mpaka anakafika ku Kaisareya.