< Acts 2 >

1 And in the day of the Pentecost being fulfilled, they were all with one accord at the same place,
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 and there came suddenly out of the sky a sound as of a violent rushing wind, and it filled all the house where they were sitting,
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 and there appeared to them divided tongues, as it were of fire; it also sat on each one of them,
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 and they were all filled with the Holy Spirit, and began to speak with other tongues, according as the Spirit was giving them to declare.
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 And there were Jews dwelling in Jerusalem, devout men from every nation of those under the heaven,
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 and the rumor of this having come, the multitude came together, and was confounded, because they were, each one, hearing them speaking in his proper dialect,
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 and they were all amazed, and wondered, saying to one another, “Behold, are not all these who are speaking Galileans?
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 And how do we hear, each in our proper dialect, in which we were born?
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 Parthians, and Medes, and Elamites, and those dwelling in Mesopotamia, in Judea also, and Cappadocia, Pontus, and Asia,
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 Phrygia also, and Pamphylia, Egypt, and the parts of Libya that [are] along Cyrene, and the strangers of Rome, both Jews and proselytes,
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 Cretes and Arabians, we heard them speaking the great things of God in our tongues.”
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 And they were all amazed, and were in doubt, saying to one another, “What would this wish to be?”
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 And others mocking said, “They are full of sweet wine”;
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 and Peter having stood up with the Eleven, lifted up his voice and declared to them: “Men—Jews, and all those dwelling in Jerusalem! Let this be known to you, and listen to my sayings,
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 for these are not drunken, as you take it up, for it is the third hour of the day.
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 But this is that which has been spoken through the prophet Joel:
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 And it will be in the last days, says God, I will pour out of My Spirit on all flesh, And your sons and your daughters will prophesy, And your young men will see visions, And your old men will dream dreams;
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 And also on My menservants, and on My maidservants, In those days, I will pour out of My Spirit, And they will prophesy;
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 And I will give wonders in the sky above, And signs on the earth beneath—Blood, and fire, and vapor of smoke,
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 The sun will be turned to darkness, And the moon to blood, Before the coming of the Day of the LORD—the great and conspicuous;
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 And it will be, everyone who, if he may have called on the Name of the LORD, will be saved.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 Men, Israelites! Hear these words: Jesus the Nazarene, a man approved of God among you by mighty works, and wonders, and signs, that God did through Him in the midst of you, according as also you yourselves have known,
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 this One, by the determinate counsel and foreknowledge of God, being given out, having been taken by lawless hands, having been crucified—you slew,
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 whom God raised up, having loosed the travails of death, because it was not possible for Him to be held by it;
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 for David says in regard to Him: I foresaw the LORD always before me—Because He is on my right hand—That I may not be moved;
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 Because of this was my heart cheered, And my tongue was glad, And yet—my flesh will also rest on hope,
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 Because You will not leave my soul to Hades, Nor will You give Your Holy One to see corruption; (Hadēs g86)
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
28 You made known to me ways of life, You will fill me with joy with Your countenance.
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 Men, brothers! It is permitted to speak with freedom to you concerning the patriarch David, that he both died and was buried, and his tomb is among us to this day;
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 therefore, being a prophet, and knowing that God swore to him with an oath, out of the fruit of his loins, according to the flesh, to raise up the Christ, to sit on his throne,
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 having foreseen, he spoke concerning the resurrection of the Christ, that His soul was not left to Hades, nor did His flesh see corruption. (Hadēs g86)
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
32 God raised up this Jesus, of which we are all witnesses;
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 then having been exalted at the right hand of God—also having received the promise of the Holy Spirit from the Father—He poured forth this which you now see and hear;
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 for David did not go up into the heavens, and he says himself: The LORD says to my Lord, Sit at My right hand,
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 Until I make Your enemies Your footstool;
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 assuredly, therefore, let all the house of Israel know that God made Him both Lord and Christ—this Jesus whom you crucified.”
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 And having heard, they were pricked to the heart; they also say to Peter and to the rest of the apostles, “What will we do, men, brothers?”
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 And Peter said to them, “Convert, and each of you be immersed on the Name of Jesus Christ, for forgiveness of sins, and you will receive the gift of the Holy Spirit,
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 for the promise is to you and to your children, and to all those far off, as many as the LORD our God will call.”
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 Also with many more other words he was testifying and exhorting, saying, “Be saved from this perverse generation”;
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 then those, indeed, who gladly received his word were immersed, and there were added on that day, as it were, three thousand souls,
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 and they were continuing steadfastly in the teaching of the apostles, and the fellowship, and the breaking of the bread, and the prayers.
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 And fear came on every soul, also many wonders and signs were being done through the apostles,
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 and all those believing were at the same place, and had all things common,
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 and they were selling the possessions and the goods, and were parting them to all, according as anyone had need.
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 Also continuing daily with one accord in the temple, also breaking bread at every house, they were partaking of food in gladness and simplicity of heart,
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 praising God, and having favor with all the people, and the LORD was adding those being saved every day to the Assembly.
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.

< Acts 2 >