< Acts 19 >
1 And it came to pass, in Apollos being in Corinth, Paul having gone through the upper parts, came to Ephesus, and having found certain disciples,
Apolo ali ku Korinto, Paulo anadutsa mʼmayiko a ku mtunda ndipo anafika ku Efeso. Kumeneko anapeza ophunzira ena.
2 he said to them, “Having believed, did you receive the Holy Spirit?” And they said to him, “But we did not even hear whether there is any Holy Spirit”;
Iye anawafunsa kuti, “Kodi munalandira Mzimu Woyera pamene munakhulupirira?” Iwo anayankha kuti, “Ayi, ife sitinamvepo kuti kuli Mzimu Woyera.”
3 and he said to them, “Into what, then, were you immersed?” And they said, “Into John’s immersion.”
Tsono Paulo anawafunsa kuti, “Nanga munabatizidwa ndi ubatizo wotani?” Iwo anati, “Ubatizo wa Yohane.”
4 And Paul said, “John, indeed, immersed with an immersion of conversion, saying to the people that they should believe in Him who is coming after him—that is, in the Christ—Jesus”;
Paulo anati, “Ubatizo wa Yohane unali wa kutembenuka mtima. Iye anawuza anthu kuti akhulupirire amene amabwera, ameneyo ndiye Yesu.”
5 and they, having heard, were immersed into the Name of the Lord Jesus,
Atamva zimenezi, anabatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu.
6 and Paul having laid [his] hands on them, the Holy Spirit came on them, they were also speaking with tongues, and prophesying,
Pamene Paulo anawasanjika manja, Mzimu Woyera anadza pa iwo ndipo anayankhula mʼmalilime ndipo ananenera.
7 and all the men were, as it were, twelve.
Anthu onsewo analipo khumi ndi awiri.
8 And having gone into the synagogue, he was speaking boldly for three months, reasoning and persuading the things concerning the Kingdom of God,
Paulo analowa mʼsunagoge ndipo anayankhula molimba mtima kwa miyezi itatu, kuwatsutsa mowakopa za ufumu wa Mulungu.
9 and when certain were hardened and were disbelieving, speaking evil of The Way before the multitude, having departed from them, he separated the disciples, reasoning every day in the school of a certain Tyrannus.
Koma ena anawumitsa mitima; anakana kukhulupirira ndipo ananyoza Njirayo pa gulu la anthu. Kotero Paulo anawasiya. Iye anatenga ophunzirawo ndipo amakambirana tsiku ndi tsiku mʼsukulu ya Turano.
10 And this happened for two years so that all those dwelling in Asia heard the word of the Lord Jesus, both Jews and Greeks,
Izi zinachitika kwa zaka ziwiri, kotero kuti Ayuda onse ndi Agriki amene amakhala ku Asiya anamva Mawu a Ambuye.
11 also mighty works—not common—God was working through the hands of Paul,
Mulungu anachita zodabwitsa zapadera kudzera mwa Paulo.
12 so that even to the ailing were brought from his body handkerchiefs or aprons, and the diseases departed from them; the evil spirits also went forth from them.
Kotero kuti mipango yopukutira thukuta ndi yovala pogwira ntchito, zomwe zinakhudza thupi la Paulo amapita nazo kwa odwala ndipo amachiritsidwa ndiponso mizimu yoyipa mwa iwo imatuluka.
13 And certain of the wandering exorcist Jews, took on [them] to name over those having the evil spirits the Name of the Lord Jesus, saying, “We adjure you by Jesus, whom Paul preaches”;
Ayuda ena amene ankayendayenda kutulutsa mizimu yoyipa anayesa kugwiritsa ntchito dzina la Ambuye Yesu pa amene anali ndi ziwanda. Iwo popemphera amati, “Ine ndikulamulira utuluke, mʼdzina la Yesu amene Paulo amamulalikira.”
14 and there were certain—seven sons of Sceva, a Jew, a chief priest—who are doing this thing;
Amene ankachita zimenezi anali ana asanu ndi awiri a Skeva, mkulu wa ansembe wa Chiyuda.
15 and the evil spirit, answering, said, “I know Jesus, and I am acquainted with Paul; and you—who are you?”
Tsiku lina mzimu woyipa unawayankha kuti, “Yesu ndimamudziwa ndiponso Paulo ndimamudziwa, nanga inu ndinu ndani?”
16 And the man, in whom was the evil spirit, leaping on them, and having overcome them, prevailed against them, so that they fled naked and wounded out of that house,
Pamenepo munthu amene anali ndi mzimu woyipa anawalumphira nawagwira onse. Iye anawamenya kwambiri, kotero kuti anathawa mʼnyumbamo ali maliseche, akutuluka magazi.
17 and this became known to all, both Jews and Greeks, who are dwelling at Ephesus, and fear fell on them all, and the Name of the Lord Jesus was being magnified;
Ayuda ndi Agriki okhala ku Efeso atamva zimenezi, anachita mantha, ndipo anthu anachitira ulemu dzina la Ambuye Yesu koposa.
18 many also of those who believed were coming, confessing and declaring their acts,
Ambiri a iwo amene tsopano anakhulupirira anafika ndi kuvomereza poyera ntchito zawo zoyipa.
19 and many of those who had practiced the superfluous arts, having brought the scrolls together, were burning [them] before all; and they reckoned together the prices of them, and found [it] fifty thousand pieces of silver,
Ambiri amene amachita za matsenga anasonkhanitsa mabuku awo pamodzi nawatentha pamaso pa anthu onse. Atawonkhetsa mtengo wa mabukuwo, unakwanira ndalama zasiliva 50,000.
20 so powerfully was the word of God increasing and prevailing.
Kotero Mawu a Ambuye anapitirira kufalikira ndipo anagwira ntchito mwamphamvu.
21 And when these things were fulfilled, Paul purposed in the Spirit, having gone through Macedonia and Achaia, to go on to Jerusalem, saying, “After my being there, it is also necessary for me to see Rome”;
Zonsezi zitachitika Paulo anatsimikiza zopita ku Yerusalemu kudzera ku Makedoniya ndi ku Akaya. Iye anati, “Kuchokera kumeneko, ndiyenera kukafikanso ku Roma.”
22 and having sent to Macedonia two of those ministering to him—Timotheus and Erastus—he himself stayed a time in Asia.
Iye anatuma anthu awiri amene amamuthandiza, Timoteyo ndi Erasto ku Makedoniya, pamene iye anakhalabe ku Asiya kwa kanthawi.
23 And there came, at that time, not a little stir about The Way,
Pa nthawi yomweyo panachitika chipolowe chachikulu chifukwa cha Njira ya Ambuye.
24 for a certain one, Demetrius by name, a worker in silver, making silver sanctuaries of Artemis, was bringing to the craftsmen not a little gain,
Mmisiri wantchito zasiliva, dzina lake Demetriyo, amene amapanga mafano asiliva a Atemi ankabweretsa phindu lalikulu kwa amisiri a kumeneko.
25 whom, having brought in a crowd together, and those who worked around such things, he said, “Men, you know that by this work we have our wealth;
Iye anasonkhanitsa pamodzi amisiriwo, pamodzinso ndi anthu ena ogwira ntchito yomweyo ndipo anati, “Anthu inu, mukudziwa kuti ife timapeza chuma chathu kuchokera pa ntchito imeneyi.
26 and you see and hear, that not only at Ephesus, but almost in all Asia, this Paul, having persuaded, turned away a great multitude, saying that they who are made by hands are not gods;
Ndipo inu mukuona ndi kumva kuti munthu uyu Paulo wakopa ndi kusokoneza anthu ambiri a ku Efeso ndiponso pafupifupi dziko lonse la Asiya. Iye akunena kuti milungu yopangidwa ndi anthu si milungu ayi.
27 and not only is this department in danger for us of coming into disregard, but also, that of the great goddess Artemis, the temple is to be reckoned for nothing, and also her greatness is about to be brought down, whom all Asia and the world worships.”
Choopsa ndi chakuti sikungowonongeka kwa ntchito yathu yokha ayi, komanso kuti nyumba ya mulungu wamkulu wamkazi Atemi idzanyozedwa ndipo mulungu wamkazi weniweniyo amene amapembedzedwa ku Asiya konse ndi dziko lapansi, ukulu wake udzawonongekanso.”
28 And having heard, and having become full of wrath, they were crying out, saying, “Great [is] the Artemis of the Ephesians!”
Atamva zimenezi, anakwiya kwambiri ndipo anayamba kufuwula kuti, “Wamkulu ndi Atemi.”
29 And the whole city was filled with confusion; they rushed also with one accord into the theater, having caught Gaius and Aristarchus, Macedonians, Paul’s fellow-travelers.
Nthawi yomweyo mu mzinda wonse munabuka chipolowe. Anthu anagwira Gayo ndi Aristariko, anzake a Paulo a ku Makedoniya, ndipo anathamangira nawo ku bwalo la masewero.
30 And on Paul’s resolving to enter in to the populace, the disciples were not permitting him,
Paulo anafuna kulowa pakati pa gulu la anthu, koma ophunzira anamuletsa.
31 and also some of the chief men of Asia, being his friends, having sent to him, were pleading [with] him not to venture into the theater himself.
Ngakhale olamulira ena aderalo, amene anali abwenzi a Paulo, anatumiza uthenga kumuletsa kuti asayesere kulowa mʼbwalomo.
32 Some indeed, therefore, were calling out one thing, and some another, for the assembly was confused, and the greater part did not know for what they had come together;
Munali chisokonezo mʼbwalomo pakuti ena amafuwula zina, enanso zina. Anthu ambiri sanadziwe ngakhale chomwe anasonkhanira.
33 and out of the multitude they put forward Alexander—the Jews thrusting him forward—and Alexander having beckoned with the hand, wished to make defense to the populace,
Ayuda anamukankhira Alekisandro kutsogolo, ndipo ena anafuwula kumulangiza iye. Iye anatambasula dzanja kuti anthu akhale chete kuti afotokozere anthu nkhaniyo.
34 and having known that he is a Jew, one voice came out of all, for about two hours, crying, “Great [is] the Artemis of the Ephesians!”
Koma pamene anthuwo anazindikira kuti ndi Myuda, onse pamodzi kwa maora awiri anafuwula kuti, “Wamkulu ndi Atemi wa ku Efeso!”
35 And the public clerk having quieted the multitude, says, “Men, Ephesians, why, who is the man that does not know that the city of the Ephesians is temple-keeper of the great goddess Artemis, and of that which fell down from Zeus?
Mlembi wa mzindawo anakhazikitsa bata gulu la anthuwo ndipo anati, “Anthu a ku Efeso, kodi ndani pa dziko lonse lapansi amene sadziwa kuti mzinda wa Efeso umayangʼanira nyumba ya mulungu wamkulu Atemi ndi fanizo lake, limene linagwa kuchokera kumwamba?
36 These things, then, being undeniable, it is necessary for you to be quiet, and to do nothing rashly.
Chifukwa chake popeza zinthu izi palibe amene angazikane, inu mukuyenera kukhala chete osachita kanthu kalikonse mofulumira.
37 For you brought these men, who are neither temple-robbers nor slandering of your goddess;
Inu mwabweretsa anthu awa pano, ngakhale kuti iwo sanabe mʼnyumba zathu zamapemphero kapena kunenera chipongwe mulungu wathu wamkazi.
38 if indeed, therefore, Demetrius and the craftsmen with him have a matter with anyone, court [days] are held, and there are proconsuls; let them accuse one another.
Ngati tsono Demetriyo ndi amisiri anzake ali ndi nkhani ndi munthu wina aliyense, mabwalo a milandu alipo, oweruza aliponso. Akhoza kukapereka nkhaniyo kwa oweruza milanduwo.
39 And if you seek after anything concerning other matters, it will be determined in the legal assembly;
Ngati mukufuna kubweretsa kanthu kali konse, ziyenera kukatsimikizidwa ndi bwalo lovomerezeka.
40 for we are also in peril of being accused of insurrection in regard to this day, there being no occasion by which we will be able to give an account of this concourse”;
Monga mmene zililimu, ife titha kuzengedwa mlandu woyambitsa chipolowe chifukwa cha zimene zachitika lerozi. Motero ife sitingathe kufotokoza za chipolowechi popeza palibe nkhani yake.”
41 and having said these things, he dismissed the assembly.
Iye atatha kunena zimenezi anawuza gulu la anthulo kuti libalalike.