< 2 Thessalonians 3 >
1 As to the rest, pray, brothers, concerning us, that the word of the LORD may run and may be glorified, as also with you,
Potsiriza, abale, mutipempherere kuti uthenga wa Ambuye ufalikire msanga ndi kulemekezedwa monga momwe munachitira inu.
2 and that we may be delivered from the unreasonable and evil men, for not all [are] of the faith;
Ndipo pempherani kuti tilanditsidwe mʼmanja mwa anthu ovuta ndi oyipa, pakuti si onse amene ali nacho chikhulupiriro.
3 but faithful is the LORD who will establish you, and will guard [you] from the evil [one];
Koma Ambuye ndi wokhulupirika, ndipo adzakulimbikitsani ndi kukutetezani kwa woyipayo.
4 and we now have confidence in the LORD, that which we command you both do and will do;
Tili ndi chikhulupiriro mwa Ambuye kuti mukuchita zonse ndipo mudzapitirira kuchita zimene tinakulamulirani.
5 and the LORD direct your hearts to the love of God, and to the endurance of the Christ.
Ambuye atsogolere mitima yanu kuti mudziwe chikondi cha Mulungu ndiponso kupirira kumene Khristu amapereka.
6 And we command you, brothers, in the Name of our Lord Jesus Christ, to withdraw yourselves from every brother walking disorderly, and not after the tradition that you received from us,
Abale, tikukulamulani mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, kuti mupewe mʼbale aliyense amene ndi waulesi ndi wachisokonezo, wosafuna kutsata zimene tinakuphunzitsani.
7 for you have known how it is necessary to imitate us, because we did not act disorderly among you;
Pakuti inu mukudziwa zimene muyenera kuchita pofuna kutitsatira. Ife sitinali alesi pamene tinali nanu
8 nor did we eat bread of anyone for nothing, but in labor and in travail, working night and day, not to be chargeable to any of you;
ndipo sitinadye chakudya cha aliyense osalipira. Komatu tinkagwira ntchito mwamphamvu usiku ndi usana kuti tisakhale cholemetsa kwa aliyense.
9 not because we have no authority, but that we might give ourselves to you [as] a pattern, to imitate us;
Sitinachite zimenezi chifukwa choti tinalibe mphamvu zolamula kuti mutithandize koma kuti tikhale chitsanzo choti mutsatire.
10 for even when we were with you, this we commanded you, that if anyone is not willing to work, neither let him eat,
Pakuti ngakhale pamene tinali nanu, tinakupatsani lamulo lakuti, “Munthu wosafuna kugwira ntchito, asadye.”
11 for we hear of some walking disorderly among you, working nothing, but being busybodies,
Ife tikumva kuti pakati panu pali ena amene ndi alesi. Iwo safuna kugwira ntchito, koma amangolowerera pa za eni.
12 and such we command and exhort through our Lord Jesus Christ, that working with quietness, they may eat their own bread;
Mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, tikuwalamula ndi kuwakakamiza kuti azigwira ntchito mwabata ndi kumadya chakudya chodzigwirira ntchito okha.
13 and you, brothers, may you not be weary doing well,
Koma inu abale, musatope nʼkuchita zabwino.
14 and if anyone does not obey our word through the letter, note this one, and have no company with him, that he may be ashamed,
Ngati wina aliyense akana kumvera malangizo athu a mʼkalatayi, mumuonetsetse ameneyo ndipo musayanjane naye kuti achite manyazi.
15 and do not count as an enemy, but admonish as a brother;
Komatu musamutenge kukhala mdani, koma muchenjezeni ngati mʼbale.
16 and may the LORD of peace Himself always give to you peace in every way; the LORD [is] with you all!
Tsopano Ambuye mwini mtendere akupatseni mtendere nthawi zonse mwa njira iliyonse. Ambuye akhale ndi inu nonse.
17 The salutation by the hand of me, Paul, which is a sign in every letter; thus I write.
Ine Paulo, ndikulemba malonje awa ndi dzanja langa, chimene ndi chizindikiro chodziwika mʼmakalata anga onse. Umo ndi mmene ndimalembera.
18 The grace of our Lord Jesus Christ [is] with you all! Amen.
Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.