< 2 Samuel 23 >
1 And these [are] the last words of David: “A declaration of David son of Jesse, And a declaration of the man raised up—Concerning the anointed of the God of Jacob, And the sweetness of the songs of Israel:
Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
2 The Spirit of YHWH has spoken by me, And His word [is] on my tongue.
“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
3 He said—the God of Israel—to me, He spoke—the Rock of Israel: He who is ruling over man [is] righteous, He is ruling in the fear of God.
Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
4 And he rises as the light of morning, A morning sun [with] no clouds! By the shining, by the rain, Tender grass of the earth!
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
5 For though my house [is] not so with God; So He made a perpetual covenant with me, Arranged in all things, and kept; For all my salvation, and all desire, For He has not caused [it] to spring up.
“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
6 As for the worthless—All of them [are] driven away as a thorn, For they are not taken away by hand;
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
7 And the man who comes against them Is filled with iron and the staff of a spear, And they are utterly burned with fire In the cessation.”
Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
8 These [are] the names of the mighty ones whom David has: sitting in the seat [is] the Tachmonite, head of the captains—he [is] Adino, who hardened himself against eight hundred—wounded at one time.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
9 And after him [is] Eleazar son of Dodo, son of Ahohi, of the three mighty men with David; in their exposing themselves among the Philistines—they have been gathered there to battle, and the men of Israel go up—
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
10 he has arisen, and strikes among the Philistines until his hand has been weary, and his hand cleaves to the sword, and YHWH works a great salvation on that day, and the people turn back after him only to strip off.
Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
11 And after him [is] Shammah son of Agee the Hararite, and the Philistines are gathered into a company, and there is a portion of the field full of lentils there, and the people have fled from the presence of the Philistines,
Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
12 and he stations himself in the midst of the portion, and delivers it, and strikes the Philistines, and YHWH works a great salvation.
Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
13 And three of the thirty heads go down and come to the harvest, to David, to the cave of Adullam, and the company of the Philistines are encamping in the Valley of Rephaim,
Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
14 and David [is] then in a fortress, and the station of the Philistines [is] then in Beth-Lehem,
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
15 and David longs and says, “Who gives me a drink of the water of the well of Beth-Lehem, which [is] by the gate?”
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
16 And the three mighty ones cleave through the camp of the Philistines, and draw water out of the well of Beth-Lehem, which [is] by the gate, and take [it] up, and bring [it] to David; and he was not willing to drink it, and pours it out to YHWH,
Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
17 and says, “Far be it from me, O YHWH, to do this; is it the blood of the men who are going with their lives?” And he was not willing to drink it; the three mighty ones did these [things].
Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
18 And Abishai brother of Joab, son of Zeruiah, he [is] head of three, and he is lifting up his spear against three hundred—wounded, and he has a name among three.
Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
19 Is he not the honored of the three? And he becomes their head; and he has not come to the [first] three.
Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
20 And Benaiah son of Jehoiada (son of a man of valor, great in deeds from Kabzeel), has struck two lion-like men of Moab, and he has gone down and struck the lion in the midst of the pit in a day of snow.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
21 And he has struck the Egyptian man, a man of appearance, and a spear [is] in the hand of the Egyptian, and he goes down to him with a rod, and takes the spear violently away out of the hand of the Egyptian, and slays him with his own spear.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
22 Benaiah son of Jehoiada has done these [things], and has a name among the three mighty ones.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
23 He is honored more than the thirty, but he did not come to the three; and David sets him over his guard.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
24 Asahel brother of Joab [is] of the thirty; Elhanan son of Dodo of Beth-Lehem,
Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
25 Shammah the Harodite, Elika the Harodite,
Sama Mharodi, Elika Mherodi,
26 Helez the Paltite, Ira son of Ikkesh the Tekoite,
Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
27 Abiezer the Annethothite, Mebunnai the Hushathite,
Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
28 Zalmon the Ahohite, Maharai the Netophathite,
Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
29 Heleb son of Baanah the Netophathite, Ittai son of Ribai from Gibeah of the sons of Benjamin,
Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
30 Benaiah the Pirathonite, Hiddai of the brooks of Gaash,
Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
31 Abi-Albon the Arbathite, Azmaveth the Barhumite,
Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
32 Eliahba the Shaalbonite, of the sons of Jashen, Jonathan,
Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
33 Shammah the Hararite, Ahiam son of Sharar the Hararite,
mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
34 Eliphelet son of Ahasbai, son of the Maachathite, Eliam son of Ahithophel the Gilonite,
Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
35 Hezrai the Carmelite, Paarai the Arbite,
Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
36 Igal son of Nathan from Zobah, Bani the Gadite,
Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
37 Zelek the Ammonite, Naharai the Beerothite, bearer of the weapons of Joab son of Zeruiah,
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
38 Ira the Ithrite, Gareb the Ithrite,
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
39 Uriah the Hittite: thirty-seven in all.
ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.