< 2 Corinthians 6 >
1 And also working together we call on [you] that you do not receive the grace of God in vain—
Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe.
2 for He says, “In an acceptable time I heard you, and in a day of salvation I helped you, behold, now [is] a well-accepted time; behold, now, a day of salvation.”
Pakuti akunena kuti, “Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera, ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza. Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”
3 In nothing giving any cause of offense, that the ministry may not be blamed,
Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke.
4 but in everything recommending ourselves as God’s servants; in much patience, in tribulations, in necessities, in distresses,
Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa.
5 in stripes, in imprisonments, in insurrections, in labors, in watchings, in fastings,
Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya;
6 in pureness, in knowledge, in long-suffering, in kindness, in the Holy Spirit, in unhypocritical love,
pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi
7 in the word of truth, in the power of God, through the armor of righteousness, on the right and on the left,
ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo.
8 through glory and dishonor, through evil report and good report, as leading astray, and true;
Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza.
9 as unknown, and recognized; as dying, and behold, we live; as disciplined, and not put to death;
Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa.
10 as sorrowful, and always rejoicing; as poor, and making many rich; as having nothing, and possessing all things.
Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.
11 Our mouth has been open to you, O Corinthians, our heart has been enlarged!
Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu.
12 You are not restricted in us, and you are restricted in your [own] yearnings,
Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife.
13 and [as] a repayment of the same kind (as to children I say [it]), be enlarged—also you!
Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.
14 Do not become yoked with others—unbelievers, for what partaking [is there] to righteousness and lawlessness?
Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima?
15 And what fellowship to light with darkness? And what concord to Christ with Belial? Or what part to a believer with an unbeliever?
Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira?
16 And what agreement to the temple of God with idols? For you are a temple of the living God, according as God said, “I will dwell in them, and will walk among [them], and I will be their God, and they will be My people,
Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti, “Ndidzakhala mwa iwo ndipo ndidzayendayenda pakati pawo, ndipo ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo adzakhala anthu anga.”
17 for this reason, come forth out of the midst of them, and be separated, says the LORD, and do not touch an unclean thing, and I will receive you,
Nʼchifukwa chake “Tulukani pakati pawo ndi kudzipatula, akutero Ambuye. Musakhudze chodetsedwa chilichonse, ndipo ndidzakulandirani.”
18 and I will be for a Father to you, and you will be sons and daughters to Me, says the LORD Almighty.”
Ndipo “Ndidzakhala Atate anu, ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi, akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”