< 2 Chronicles 2 >
1 And Solomon says to build a house for the Name of YHWH, and a house for his kingdom,
Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu.
2 and Solomon numbers seventy thousand men bearing burden, and eighty thousand men hewing in the mountain, and three thousand and six hundred overseers over them.
Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.
3 And Solomon sends to Huram king of Tyre, saying, “When you have dealt with my father David, then you send cedars to him to build a house for him to dwell in;
Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo: “Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo.
4 behold, I am building a house for the Name of my God YHWH, to sanctify [it] to Him, to make incense before Him, incense of spices, and a continual arrangement, and burnt-offerings at morning and at evening, at Sabbaths, and at new moons, and at appointed times of our God YHWH; this [is] on Israel for all time.
Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.
5 And the house that I am building [is] great, for our God [is] greater than all gods;
“Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse.
6 and who retains strength to build a house for Him, since the heavens, even the heavens of the heavens, do not contain Him? And who [am] I that I build a house for Him, except to make incense before Him?
Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?
7 And now, send a wise man to me to work in gold, and in silver, and in bronze, and in iron, and in purple, and crimson, and blue, and knowing to engrave engravings with the wise men who [are] with me in Judah and in Jerusalem, whom my father David prepared;
“Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.
8 and send to me cedar-trees, firs, and algums from Lebanon, for I have known that your servants know to cut down trees of Lebanon, and behold, my servants [are] with your servants,
“Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu
9 even to prepare trees in abundance for me, for the house that I am building [is] great and wonderful.
kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola.
10 And behold, I have given to your servants, to hewers, to those cutting the trees, twenty thousand cors of beaten wheat, and twenty thousand cors of barley, and twenty thousand baths of wine, and twenty thousand baths of oil.”
Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”
11 And Huram king of Tyre answers in writing, and sends [it] to Solomon: “In the love of YHWH for His people, He has set you [as] king over them.”
Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti, “Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”
12 And Huram says, “Blessed [is] YHWH, God of Israel, who made the heavens and the earth, who has given a wise son to David the king, knowing wisdom and understanding, who builds a house for YHWH, and a house for his kingdom.
Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti, “Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.
13 And now, I have sent a wise man having understanding, of [my] father Huram
“Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu,
14 (son of a woman of the daughters of Dan, and his father a man of Tyre), knowing to work in gold, and in silver, in bronze, in iron, in stones, and in wood, in purple, in blue, and in fine linen, and in crimson, and to engrave any engraving, and to devise any invention that is given to him, with your wise men, and the wise men of my lord, your father David.
amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.
15 And now, the wheat, and the barley, the oil, and the wine, as my lord said, let him send to his servants,
“Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza,
16 and we cut trees out of Lebanon, according to all your need, and bring them to you—floats by sea, to Joppa, and you take them up to Jerusalem.”
ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”
17 And Solomon numbers all the men, the sojourners who [are] in the land of Israel, after the numbering with which his father David numbered them, and they are found [to be] one hundred and fifty thousand and three thousand and six hundred;
Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600.
18 and he makes from them seventy thousand burden-bearers, and eighty thousand hewers in the mountain, and three thousand and six hundred overseers, to cause the people to work.
Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.