< 2 Chronicles 10 >

1 And Rehoboam goes to Shechem, for all of Israel has come [to] Shechem to cause him to reign.
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse anapita kumeneko kuti akamulonge ufumu.
2 And it comes to pass, at Jeroboam son of Nebat—who [is] in Egypt because he has fled from the face of Solomon the king—hearing, that Jeroboam turns back out of Egypt;
Yeroboamu mwana wa Nebati atamva zimenezi (Iye anali ku Igupto, kumene anapita pothawa mfumu Solomoni) anabwerako kuchokera ku Igupto.
3 and they send and call for him, and Jeroboam comes in, and all of Israel, and they speak to Rehoboam, saying,
Kotero anthu anakayitana Yeroboamu ndipo iye ndi Aisraeli onse anapita kwa Rehobowamu ndi kumuwuza kuti,
4 “Your father made our yoke sharp, and now, make light [some] of the sharp service of your father, and [some] of his heavy yoke that he put on us, and we serve you.”
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma tsopano mutipeputsire ntchito yolemetsayi ndi goli lolemerali limene analiyika pa ife ndipo ifeyo tidzakutumikirani.”
5 And he says to them, “Yet three days—then return to me”; and the people go.
Rehobowamu anayankha kuti, “Mukabwerenso pakapita masiku atatu.” Choncho anthuwo anachoka.
6 And King Rehoboam consults with the aged men who have been standing before his father Solomon in his being alive, saying, “How are you counseling to answer this people?”
Kenaka mfumu Rehobowamu anafunsira nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira abambo ake, Solomoni, pamene anali moyo. Iye anafunsa kuti, “Kodi inu mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu awa?”
7 And they speak to him, saying, “If you become good to this people, and have been pleased with them, and spoken to them good words, then they have been servants to you [for] all the days.”
Iwo anayankha kuti, “Ngati inu muwakomera mtima anthu awa ndi kuwasangalatsa ndiponso kuwayankha mawu abwino, iwo adzakutumikirani nthawi zonse.”
8 And he forsakes the counsel of the aged men that they counseled him, and consults with the boys who have grown up with him, those standing before him,
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakulu anamupatsa ndipo anakafunsira nzeru kwa anyamata amene anakula naye pamodzi komanso amamutumikira.
9 and he says to them, “What are you counseling, and we answer this people that have spoken to me, saying, Make light [some] of the yoke that your father put on us?”
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ndi otani? Kodi tiwayankhe chiyani anthu amene akunena kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anayika pa ife?’”
10 And the boys who have grown up with him speak with him, saying, “Thus you say to the people who have spoken to you, saying, Your father made our yoke heavy, and you, make light [some] of our yoke; thus you say to them, My little finger is thicker than the loins of my father;
Anyamata amene anakula pamodzi naye anamuyankha kuti, “Anthu amene anena kwa inu kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma inu mupeputse goli lathu,’ muwawuze kuti, ‘Chala changa chachingʼono ndi chachikulu kuposa chiwuno cha abambo anga.
11 and now, my father laid a heavy yoke on you, and I add to your yoke; my father disciplined you with whips, and I—with scorpions.”
Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 And Jeroboam comes in, and all the people, to Rehoboam on the third day, as the king spoke, saying, “Return to me on the third day.”
Tsiku lachitatu Yeroboamu ndi anthu onse anabwerera kwa Rehobowamu monga ananenera mfumu kuti, “Mukabwerenso kwa ine pakapita masiku atatu.”
13 And the king answers them sharply, and King Rehoboam forsakes the counsel of the aged men,
Mfumu inawayankha mwankhanza, pokana malangizo a akuluakulu aja.
14 and speaks to them according to the counsel of the boys, saying, “My father made your yoke heavy, and I add to it; my father disciplined you with whips, and I—with scorpions.”
Iye anatsatira malangizo a anyamata ndipo anati, “Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 And the king has not listened to the people, for the revolution has been from God, for the sake of YHWH’s establishing His word that He spoke by the hand of Abijah the Shilonite to Jeroboam son of Nebat.
Kotero mfumu sinamvere anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Mulungu, kukwaniritsa mawu amene Yehova ananena kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 And all Israel have seen that the king has not listened to them, and the people send back [word to] the king, saying, “What portion do we have in David? Indeed, there is no inheritance in a son of Jesse; [go], each to your tents, O Israel! Now see your house, O David!” And all [in] Israel go to their tents.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kuwamvera, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, gawo lanji mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli! Pitani kwanu. Iwe Davide! Yangʼana banja lako.” Kotero Aisraeli onse anapita kwawo.
17 As for the sons of Israel who are dwelling in the cities of Judah—Rehoboam reigns over them.
Koma Rehobowamu anakhala akulamulirabe Aisraeli amene amakhala mʼmizinda ya Yuda.
18 And King Rehoboam sends Hadoram, who [is] over the tribute, and the sons of Israel cast stones at him, and he dies; and King Rehoboam has strengthened himself to go up into a chariot to flee to Jerusalem;
Mfumu Rehobowamu inatuma Hadoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli anamugenda miyala ndi kumupha. Koma mfumu Rehobowamu anakwera galeta lake ndi kuthawira ku Yerusalemu.
19 and Israel transgresses against the house of David to this day.
Motero Israeli wakhala akuwukira banja la Davide mpaka lero lino.

< 2 Chronicles 10 >