< 1 Samuel 25 >
1 And Samuel dies, and all Israel is gathered, and mourns for him, and buries him in his house, in Ramah; and David rises and goes down to the wilderness of Paran.
Samueli anamwalira, ndipo Aisraeli onse anasonkhana kudzalira maliro ake ndipo anamuyika mʼmanda ku mudzi kwawo ku Rama. Ndipo Davide anapita ku chipululu cha Parani.
2 And [there is] a man in Maon, and his work [is] in Carmel; and the man [is] very great, and he has three thousand sheep and one thousand goats; and he is shearing his flock in Carmel.
Kunali munthu wina wolemera kwambiri ku Maoni amene malo ake a ntchito anali ku Karimeli. Iyeyu anali ndi mbuzi 1,000 ndi nkhosa 3,000.
3 And the name of the man [is] Nabal, and the name of his wife [is] Abigail, and the woman [is] of good understanding, and of beautiful form, and the man [is] hard and evil [in his] doings; and he [is] a Calebite.
Dzina lake linali Nabala ndipo anali wa fuko la Kalebe. Dzina la mkazi wake linali Abigayeli. Anali mkazi wanzeru ndi wokongola, koma mwamuna wake, wa banja la Kalebe, anali wowuma mtima ndi wamwano pa zochita zake.
4 And David hears in the wilderness that Nabal is shearing his flock,
Davide anamva akanali ku chipululu kuti Nabala akumeta nkhosa.
5 and David sends ten young men, and David says to the young men, “Go up to Carmel, and you have come to Nabal, and asked of him in my name of welfare,
Choncho anatuma anyamata khumi nawawuza kuti, “Pitani kwa Nabala ku Karimeli ndipo mukamulonjere mʼdzina langa.
6 and said thus to the living: And peace to you, and peace to your house, and peace to all that you have!
Mukamuwuze kuti, ‘Mtendere ukhale ndi inu, banja lanu pamodzi ndi zonse zimene muli nazo.
7 And now, I have heard that you have shearers; now, the shepherds whom you have have been with us, we have not put them to shame, nor has anything been looked after by them, all the days of their being in Carmel.
“‘Tsono ndamva kuti muli ndi anthu ometa nkhosa. Pamene abusa anu anali nafe kuno, sitinawachite china chilichonse choyipa, ndipo sanasowe kanthu pa nthawi yonse imene anali ku Karimeli.
8 Ask your young men, and they declare [it] to you, and the young men find grace in your eyes, for we have come on a good day; please give that which your hand finds to your servants and to your son, to David.”
Muwafunse antchito anu ndipo akuwuzani. Kotero akomereni mtima anyamata anga, pakuti tabwera pa nthawi yachikondwerero. Chonde apatseniko antchito anuwo ndi mwana wanu Davide chilichonse chimene mungakhale nacho.’”
9 And the young men of David come in, and speak to Nabal according to all these words, in the name of David—and rest.
Anyamata a Davide aja atafika, anamuwuza Nabala zonse zimene Davide anayankhula. Ndipo anadikira yankho.
10 And Nabal answers the servants of David and says, “Who [is] David, and who [is] the son of Jesse? Have servants been multiplied today who are each breaking away from his master?
Nabala anayankha anyamata a Davide kuti, “Kodi Davide ndi ndani? Mwana wa Yese ndi ndani? Masiku ano pali antchito ambiri amene akuthawa kwa mabwana awo.
11 And have I taken my bread, and my water, and my flesh, which I slaughtered for my shearers, and have given [it] to men whom I have not known where they [are] from?”
Nditengerenji buledi, madzi ndi nyama zimene ndaphera anthu anga ometa nkhosa ndi kuzipereka kwa anthu amene sindikudziwa kumene achokera?”
12 And the young men of David turn on their way, and turn back, and come in, and declare to him according to all these words.
Choncho anyamata a Davide aja anatembenuka nabwerera. Atafika anafotokozera Davide mawu onse a Nabala.
13 And David says to his men, “Each gird on his sword”; and they each gird on his sword, and David also girds on his sword, and about four hundred men go up after David, and two hundred have remained by the vessels.
Davide anawuza anthu ake kuti, “Aliyense amangirire lupanga lake!” Choncho aliyense anamangirira lupanga lake. Davidenso anamangirira lupanga lake. Anthu pafupifupi 400 ndiwo anapita ndi Davide, pamene anthu 200 anatsala ndi katundu.
14 And one young man of the youths has declared [it] to Abigail wife of Nabal, saying, “Behold, David has sent messengers out of the wilderness to bless our lord, and he flies on them;
Tsono mmodzi mwa antchito anawuza Abigayeli mkazi wa Nabala kuti, “Davide anatumiza amithenga kuchokera ku chipululu kudzalonjera mbuye wathu, koma iye anawalalatira.
15 and the men [are] very good to us, and have not put us to shame, and we have not looked after anything all the days we have gone up and down with them, in our being in the field;
Komatu anthuwa anatichitira zabwino kwambiri. Sanatizunze, ndipo nthawi yonse imene tinali nawo ku busa sitinasowe kanthu.
16 they have been a wall to us both by night and by day, all the days of our being with them, feeding the flock.
Ankatitchinjiriza ngati mpanda usiku ndi usana nthawi yonse tinkaweta nkhosa.
17 And now, know and consider what you do; for evil has been determined against our lord, and against all his house, and he [is] too much a son of worthlessness to be spoken to.”
Tsono onani chimene mungachite, chifukwa zimenezi zingadzetse tsoka pa mbuye wathu pamodzi ndi nyumba yake. Paja mbuye athu aja ndi munthu wa khalidwe loyipa moti palibe amene angathe kuyankhula naye.”
18 And Abigail hurries, and takes two hundred loaves, and two bottles of wine, and five sheep, prepared, and five measures of roasted grain, and one hundred bunches of raisins, and two hundred bunches of figs, and sets [them] on the donkeys.
Ndipo Abigayeli sanataye nthawi. Iye anatenga malofu a buledi 200, matumba a chikopa awiri a vinyo, nkhosa zisanu zowotcheratu, makilogalamu 17 a tirigu wokazinga, makeke a mphesa zowuma 100, ndiponso makeke a nkhuyu 200, ndipo anazisenzetsa abulu.
19 And she says to her young men, “Pass over before me; behold, I am coming after you”; and she has not declared [it] to her husband Nabal;
Kenaka anawuza antchito ake kuti, “Tsogolani, ine ndikutsatirani.” Koma sanawuze mwamuna wake Nabala.
20 and it has come to pass, she is riding on the donkey and is coming down in the secret part of the hill-country, and behold, David and his men are coming down to meet her, and she meets them.
Mayi uja atakwera pa bulu wake ndi kufika pa tsinde la phiri, anangoona Davide ndi ankhondo ake akubwera kunali iye. Choncho anakumana nawo.
21 And David said, “Surely in vain I have kept all that this [one] has in the wilderness, and nothing has been looked after of all that he has, and he turns back to me evil for good;
Nthawiyi nʼkuti Davide atanena kuti, “Kani ndinalondera pachabe katundu wa munthu uyu mʼchipululu muja! Ndipotu palibe kanthu nʼkamodzi komwe kake kamene kanasowa. Tsono wandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino.
22 thus God does to the enemies of David, and thus He adds, if I leave of all that he has until the morning light—of those sitting on the wall.”
Mulungu andilange kwambiri ngati pofika mmawa nditakhale nditasiyako ngakhale munthu mmodzi mwa onse amene ali nawo.”
23 And Abigail sees David, and hurries and comes down from off the donkey, and falls on her face before David, and bows herself to the earth,
Abigayeli ataona Davide, anatsika pa bulu wake mofulumira ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pa Davide.
24 and falls at his feet and says, “On me, my lord, the iniquity; and please let your handmaid speak in your ear, and hear the words of your handmaid.
Ali chigonere choncho pa mapazi a Davide anati, “Mbuye wanga, kulakwa kukhale pa ine ndekha. Chonde lolani kuti mdzakazi wanune ndiyankhule nanu, ndipo mumve mawu a ine mdzakazi wanu.
25 Please do not let my lord set his heart to this man of worthlessness, on Nabal, for as his name [is] so [is] he; Nabal [is] his name, and folly [is] with him; and I, your handmaid, did not see the young men of my lord whom you sent;
Mbuye wanga musasamale za mwamuna wanga Nabala, munthu wa khalidwe loyipa. Iyeyu ali monga dzina lake liliri. Monga dzina lake litanthauza kuti chitsiru, ndiye kuti zake zonse ndi zauchitsiru basi. Koma ine mdzakazi wanu, sindinawaone anthu amene mbuye wanga munawatuma.
26 and now, my lord, YHWH lives, and your soul lives, in that YHWH has withheld you from coming in with blood, and to save your hand from yourself—now let your enemies be as Nabal, even those seeking evil toward my lord.
Tsono mbuye wanga muli apa, ndikulumbira pali Yehova wamoyo amene wakuletsani kuti musakhetse magazi a munthu ndi kulipsira nokha, kuti adani anu amene afuna kukuchitani zoyipa adzakhale ngati Nabala.
27 And now, this blessing which your maidservant has brought to my lord—it has been given to the young men who are going up and down at the feet of my lord.
Choncho, nazi mphatso zimene mdzakazi wanu ndabwera nazo kwa mbuye wanga kuti zipatsidwe kwa anyamata amene muli nawo.
28 Please bear with the transgression of your handmaid, for YHWH certainly makes a steadfast house for my lord; for my lord has fought the battles of YHWH, and evil is not found in you [all] your days.
Chonde khululukani zolakwa za ine mdzakazi wanu. Ndithu Yehova adzakhazikitsa banja la mbuye wanga mu ufumu, popeza mukumenya nkhondo ya Yehova. Choncho choyipa sichidzapezeka mwa inu masiku onse a moyo wanu.
29 And man rises to pursue you and to seek your soul, and the soul of my lord has been bound in the bundle of life with your God YHWH; as for the soul of your enemies, He slings them out in the midst of the hollow of the sling.
Ngati munthu wina akuwukirani ndi kukulondani, Yehova Mulungu wanu adzateteza moyo wa mbuye wanga monga mmene munthu asungira chuma mʼphukusi, koma moyo wa adani anu adzawutaya kutali monga momwe munthu amaponyera mwala ndi legeni.
30 And it has been, when YHWH does to my lord according to all the good which He has spoken concerning you, and appointed you for leader over Israel,
Yehova adzakuchitirani mbuye wanga zabwino zonse zimene anakulonjezani. Adzakuyikani kukhala wolamulira Aisraeli.
31 that this is not to you for a stumbling-block, and for an offense of heart to my lord—either to shed blood for nothing, or my lord’s restraining himself; and YHWH has done good to my lord, and you have remembered your handmaid.”
Zikadzatero, inu mbuye wanga simudzakhala ndi chikumbumtima choti munakhetsa magazi kapena kulipsira popanda chifukwa. Koma Yehova akadzakuchitirani zabwino zonsezi musadzandiyiwale ine mdzakazi wanu.”
32 And David says to Abigail, “Blessed [is] YHWH, God of Israel, who has sent you to meet me this day,
Tsono Davide anawuza Abigayeli kuti, “Alemekezeke Yehova Mulungu wa Israeli, amene wakutuma iwe lero kuti ukumane nane.
33 and blessed [is] your discretion, and blessed [are] you in that you have restrained me this day from coming in with blood, and to restrain my hand to myself.
Yehova akudalitseni chifukwa cha nzeru zanu pondiletsa lero kuti ndisakhetse magazi ndi kubwezera adani anga ndi manja anga.
34 And yet, YHWH lives, God of Israel, who has kept me back from doing evil with you, for unless you had hurried, and come to meet me, surely there had not been left to Nabal until the morning light, of those sitting on the wall.”
Kunena zoona, pali Yehova Wamoyo, Mulungu wa Israeli, amene wandiletsa kuti ndisakupwetekeni, mukanapanda kubwera msanga kudzakumana nane, palibe munthu aliyense wamwamuna wa Nabala akanasiyidwa wamoyo pakucha mmawa.”
35 And David receives from her hand that which she has brought to him, and he has said to her, “Go up in peace to your house; see, I have listened to your voice, and accept your face.”
Ndipo Davide analandira kwa mayiyo zimene anamutengera ndipo anati, “Pitani kwanu mu mtendere. Ine ndamva mawu anu ndipo ndavomera zimene mwapempha.”
36 And Abigail comes to Nabal, and behold, he has a banquet in his house, like a banquet of the king, and the heart of Nabal [is] glad within him, and he [is] drunk to excess, and she has not declared anything to him, little or much, until the morning light.
Abigayeli atabwerera kwa Nabala anamupeza ali mʼnyumba akuchita mphwando ngati la mfumu. Iye anali atakondwa kwambiri popeza anali ataledzera kwambiri. Choncho mkazi wakeyo sanamuwuze kalikonse mpaka mmawa kutacha.
37 And it comes to pass in the morning, when the wine is gone out from Nabal, that his wife declares these things to him, and his heart dies within him, and he has been as a stone.
Tsono mmawa, mowa utamuchoka Nabala, mkazi wake anamuwuza zonse. Pomwepo mtima wake unaleka kugunda ndipo unawuma gwaa ngati mwala.
38 And it comes to pass [in] about ten days, that YHWH strikes Nabal and he dies,
Patapita masiku khumi, Yehova anakantha Nabala ndipo anafa.
39 and David hears that Nabal [is] dead and says, “Blessed [is] YHWH who has pleaded the cause of my reproach from the hand of Nabal, and His servant has kept back from evil, and YHWH has turned back the wickedness of Nabal on his own head”; and David sends and speaks with Abigail, to take her to himself for a wife.
Pamene Davide anamva kuti Nabala wamwalira, iye anati, “Alemekezeke Yehova, walipsira Nabala chipongwe chimene anandichita ndipo anandiletsa ine mtumiki wake kuti ndisachite choyipa. Yehova wabwezera pamutu pa Nabala choyipa chimene iye anachita.” Kenaka Davide anatumiza mawu kwa Abigayeli, kumupempha kuti akhale mkazi wake.
40 And the servants of David come to Abigail at Carmel, and speak to her, saying, “David has sent us to you to take you to himself for a wife.”
Anyamata a Davide atafika ku Karimeli anawuza Abigayeli kuti, “Davide watituma kwa iwe kuti tikutenge ukhale mkazi wake.”
41 And she rises and bows herself—face to the earth—and says, “Behold, your handmaid [is] for a maidservant to wash the feet of the servants of my lord.”
Abigayeli anagwada nagunditsa nkhope yake pansi ndipo anati, “Ine mdzakazi wa mbuye wanga ndakonzeka kutumikira ngakhale kusambitsa mapazi a anyamata ake.”
42 And Abigail hurries and rises, and rides on the donkey; and [there are] five of her young women who are going at her feet; and she goes after the messengers of David, and is to him for a wife.
Motero Abigayeli ananyamuka mofulumira nakwera bulu wake. Tsono iye pamodzi ndi anamwali ake asanu amene ankamutumikira, anatsagana ndi amithenga a Davide aja ndipo anakakhala mkazi wake wa Davide.
43 And David has taken Ahinoam from Jezreel, and they are—even both of them—for wives to him;
Davide nʼkuti atakwatiranso Ahinoamu wa ku Yezireeli ndipo onse awiri anali akazi ake.
44 and Saul gave his daughter Michal, David’s wife, to Phalti son of Laish, who [is] of Gallim.
Koma Sauli anali atakwatitsa Mikala, mkazi wa Davide kwa Paliti mwana wa Laisi wa ku Galimu.