< 1 Samuel 24 >

1 And it comes to pass, when Saul has turned back from after the Philistines, that they declare to him, saying, “Behold, David [is] in the wilderness of En-gedi.”
Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
2 And Saul takes three thousand chosen men out of all Israel, and goes to seek David and his men, on the front of the rocks of the wild goats,
Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
3 and he comes to folds of the flock, on the way, and there [is] a cave, and Saul goes in to cover his feet; and David and his men are abiding in the sides of the cave.
Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
4 And the men of David say to him, “Behold, the day of which YHWH said to you, Behold, I am giving your enemy into your hand, and you have done to him as it is good in your eyes”; and David rises and cuts off the skirt of the upper robe which [is] on Saul with stealth.
Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
5 And it comes to pass afterward that the heart of David strikes him, because that he has cut off the skirt which [is] on Saul,
Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
6 and he says to his men, “Far be it from me, by YHWH; I do not do this thing to my lord—to the anointed of YHWH—to put forth my hand against him, for he [is] the anointed of YHWH.”
Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
7 And David subdues his men by words, and has not permitted them to rise against Saul; and Saul has risen from the cave, and goes on the way;
Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
8 and David rises afterward, and goes out from the cave, and calls after Saul, saying, “My lord, O king!” And Saul looks attentively behind him, and David bows—face to the earth—and pays respect.
Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
9 And David says to Saul, “Why do you hear the words of man, saying, Behold, David is seeking your calamity?
Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
10 Behold, this day your eyes have seen how that YHWH has given you into my hand today in the cave; and [one] said to slay you, and [my eye] has pity on you, and I say, I do not put forth my hand against my lord, for he [is] the anointed of YHWH.
Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
11 And my father, see, indeed see the skirt of your upper robe in my hand; for by cutting off the skirt of your upper robe, and I have not slain you, know and see that there is not evil and transgression in my hand, and I have not sinned against you, and you are hunting my soul to take it!
Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
12 YHWH judges between me and you, and YHWH has avenged me of you, and my hand is not on you;
Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
13 as the allegory of the ancients says, Wickedness goes out from the wicked, and my hand is not on you.
Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
14 After whom has the king of Israel come out? After whom are you pursuing? After a dead dog! After one flea!
“Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
15 And YHWH has been for judge, and has judged between me and you, indeed, He sees and pleads my cause, and delivers me out of your hand.”
Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
16 And it comes to pass, when David completes to speak these words to Saul, that Saul says, “Is this your voice, my son David?” And Saul lifts up his voice, and weeps.
Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
17 And he says to David, “You [are] more righteous than I; for you have done me good, and I have done you evil;
Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
18 and you have declared today how that you have done good with me, how that YHWH shut me up into your hand, and you did not slay me,
Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
19 and that a man finds his enemy, and has sent him away in a good manner; and YHWH repays you good for that which you did to me this day.
Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
20 And now, behold, I have known that you certainly reign, and the kingdom of Israel has stood in your hand;
Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
21 and now, swear to me by YHWH [that] you do not cut off my seed after me, nor do you destroy my name from the house of my father.”
Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
22 And David swears to Saul, and Saul goes to his house, and David and his men have gone up to the fortress.
Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.

< 1 Samuel 24 >