< 1 Kings 5 >

1 And Hiram king of Tyre sends his servants to Solomon, for he heard that they had anointed him for king instead of his father, for Hiram was loving toward David all the days;
Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
2 and Solomon sends to Hiram, saying,
Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
3 “You have known my father David, that he has not been able to build a house for the Name of his God YHWH, because of the wars that have been all around him, until YHWH’s putting them under the soles of his feet.
“Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
4 And now, my God YHWH has given rest to me all around, there is no adversary nor evil occurrence,
Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
5 and behold, I am saying to build a house for the Name of my God YHWH, as YHWH spoke to my father David, saying, Your son whom I appoint in your stead on your throne, he builds the house for My Name.
Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
6 And now, command, and they cut down cedars for me out of Lebanon, and my servants are with your servants, and I give the hire of your servants to you according to all that you say, for you have known that there is not a man among us acquainted with cutting wood, like the Sidonians.”
“Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
7 And it comes to pass at Hiram’s hearing the words of Solomon, that he rejoices exceedingly and says, “Blessed [is] YHWH today, who has given to David a wise son over this numerous people.”
Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
8 And Hiram sends to Solomon, saying, “I have heard that which you have sent to me, I do all your desire concerning cedar-wood and fir-wood;
Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
9 my servants bring [them] down from Lebanon to the sea, and I make them floats in the sea to the place that you send to me, and I have spread them out there; and you take [them] up, and you execute my desire, to give the food [for] my house.”
Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
10 And Hiram is giving cedar-trees and fir-trees to Solomon—all his desire,
Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
11 and Solomon has given twenty thousand cors of wheat to Hiram, [the] food for his house, and twenty cors of beaten oil; thus Solomon gives to Hiram year by year.
ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
12 And YHWH has given wisdom to Solomon as He spoke to him, and there is peace between Hiram and Solomon, and both of them make a covenant.
Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
13 And King Solomon lifts up a tribute out of all Israel, and the tribute is thirty thousand men,
Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
14 and he sends them to Lebanon, ten thousand a month, by changes; they are in Lebanon [for] a month [and] two months in their own house; and Adoniram [is] over the tribute.
Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
15 And King Solomon has seventy thousand bearing burdens, and eighty thousand hewing in the mountain,
Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
16 apart from the three thousand and three hundred heads of the officers of Solomon who [are] over the work—those ruling over the people who are working in the business.
ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
17 And the king commands, and they bring great stones, precious stones, [and] hewn stones, to lay the foundation of the house;
Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
18 and the builders of Solomon, and the builders of Hiram, and the Giblites hew [them], and prepare the wood and the stones to build the house.
Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.

< 1 Kings 5 >