< 1 John 2 >
1 My little children, these things I write to you that you may not sin: and if anyone may sin, we have an Advocate with the Father, Jesus Christ, [the] Righteous One,
Inu Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zimenezi kuti musachimwe. Koma wina akachimwa, tili nayo Nkhoswe yotinenera kwa Atate, Yesu Khristu, Wolungamayo.
2 and He is [the] propitiation for our sins, and not only for ours, but also for the whole world,
Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso machimo onse a dziko lapansi.
3 and in this we know that we have known Him, if we may keep His commands;
Ife timatsimikiza kuti tikumudziwa ngati tikusunga malamulo ake.
4 he who is saying, “I have known Him,” and is not keeping His commands, is a liar, and the truth is not in him;
Munthu akamanena kuti, “Ine ndimadziwa Mulungu,” koma samvera malamulo a Mulunguyo, ndi wabodza ameneyo ndipo mwa iye mulibe choonadi.
5 and whoever may keep His word, truly the love of God has been perfected in him; in this we know that we are in Him.
Koma munthu aliyense akamvera mawu ake, ndiye kuti chikondi cha Mulungu chafikadi penipeni mwa iyeyo. Pamenepo timatsimikizadi kuti tili mwa Iye.
6 He who is saying he remains in Him, himself ought to also walk according as He walked.
Aliyense amene amati amakhala mwa Mulungu, ayenera kukhala moyo umene Yesu ankakhala.
7 Beloved, I do not write a new command to you, but an old command, that you had from the beginning—the old command is the word that you heard from the beginning;
Okondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lakale lomwe lija, limene munali nalo kuyambira pachiyambi. Lamulo la kalelo ndi mawu amene munawamva kale.
8 again, a new command I write to you, which is true in Him and in you, because the darkness is passing away, and the true light now shines;
Komabe ndi lamulo latsopano limene ndikukulemberani. Choonadi chake chikuoneka mwa Yesu ndiponso mwa inu, chifukwa mdima ukutha ndipo kuwunika kwenikweni kwayamba kale kuwala.
9 he who is saying he is in the light, and is hating his brother, he is in the darkness until now;
Aliyense amene amati ali mʼkuwunika, koma nʼkumadana ndi mʼbale wake ali mu mdima.
10 he who is loving his brother, he remains in the light, and there is not a stumbling-block in him;
Aliyense amene amakonda mʼbale wake amakhalanso mʼkuwunika, ndipo mwa iye mulibe chokhumudwitsa.
11 but he who is hating his brother, he is in the darkness, and he walks in the darkness, and he has not known where he goes, because the darkness blinded his eyes.
Koma aliyense wodana ndi mʼbale wake ali mu mdima ndipo akuyenda mu mdima. Iyeyo sakudziwa kumene akupita, chifukwa mdima wamudetsa mʼmaso mwake.
12 I write to you, little children, because sins have been forgiven you through His Name;
Inu ana okondedwa, ndikukulemberani popeza kuti machimo anu akhululukidwa chifukwa cha dzina la Yesu.
13 I write to you, fathers, because you have known Him who [is] from the beginning; I write to you, young men, because you have overcome the evil [one]; I write to you, little youths, because you have known the Father;
Inu abambo, ndikukulemberani popeza kuti munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi. Inu anyamata, ndikukulemberani popeza kuti munagonjetsa woyipayo.
14 I wrote to you, fathers, because you have known Him who [is] from the beginning; I wrote to you, young men, because you are strong, and the word of God remains in you, and you have overcome the evil [one].
Ana okondedwa, ndikukulemberani chifukwa mumawadziwa Atate. Abambo, ndikukulemberani chifukwa munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi. Inu anyamata, ndikukulemberani chifukwa ndinu amphamvu. Mawu a Mulungu amakhala mwa inu ndipo mumamugonjetsa woyipayo.
15 Do not love the world, nor the things in the world; if anyone loves the world, the love of the Father is not in him,
Musamakonde dziko lapansi kapena chilichonse cha dziko lapansi. Ngati munthu wina aliyense akonda dziko lapansi, mwa iyeyo mulibe chikondi chokonda Atate.
16 because all that [is] in the world—the desire of the flesh, and the desire of the eyes, and the ostentation of [one’s] life—is not of the Father, but of the world,
Pakuti zonse za mʼdziko lapansi, zilakolako za thupi, zinthu zimene maso amakhumbira ndiponso kuyandikira zinthu za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi.
17 and the world is passing away, and the desire of it, but he who is doing the will of God, he remains—throughout the age. (aiōn )
Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya. (aiōn )
18 Little youths, it is the last hour; and even as you heard that the antichrist comes, even now antichrists have become many—whereby we know that it is [the] last hour;
Ana anga, ino ndi nthawi yotsiriza, ndipo monga munamva kale kuti anthu okana Khristu akubwera, ngakhale tsopano okana Khristu ambiri afika kale. Zimenezi zikutisonyeza kuti ino ndi nthawi yotsiriza.
19 they went forth out of us, but they were not of us, for if they had been of us, they would have remained with us; but [they went out] so that they might be revealed that they are not all of us.
Anthu amenewa anachoka pakati pathu, komatu sanali a mʼgulu lathu. Pakuti akanakhala a mʼgulu lathu, akanakhalabe nafe, koma kuchoka kwawo kunatisonyeza kuti sanali a mʼgulu lathu.
20 And you have an anointing from the Holy One, and have known all things;
Koma inu muli ndi kudzoza kochokera kwa Woyerayo, ndipo nonsenu mukudziwa choonadi.
21 I did not write to you because you have not known the truth, but because you have known it, and because no lie is of the truth.
Sindikukulemberani chifukwa choti simudziwa choonadi ayi, koma chifukwa choti mumadziwa choonadicho, ndipo mukudziwanso kuti bodza silichokera pa choonadi.
22 Who is the liar, except he who is denying that Jesus is the Christ? This one is the antichrist who is denying the Father and the Son;
Wabodzayo ndani? Ndi munthu aliyense amene amanena kuti Yesu si Mpulumutsi. Munthu woteroyo ndi wokana Khristu, ndiponso amakana Atate, ndi Mwana.
23 everyone who is denying the Son, neither has the Father; he who is confessing the Son has the Father also.
Aliyense wokana Mwana alibenso Atate. Wovomereza Mwana alinso ndi Atate.
24 You, then, that which you heard from the beginning, let it remain in you; if that which you heard from the beginning may remain in you, you also will remain in the Son and in the Father,
Onetsetsani kuti zimene munazimva kuyambira pachiyambi zikhalebe mwa inu. Ngati zikhala mwa inu, inunso mudzakhala mwa Mwana ndiponso mwa Atate.
25 and this is the promise that He promised us—the continuous life. (aiōnios )
Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha. (aiōnios )
26 These things I wrote to you concerning those leading you astray;
Ine ndikukulemberani zimenezi kuti ndikuwuzeni za amene akufuna kukusocheretsani.
27 and you, the anointing that you received from Him, it remains in you, and you have no need that anyone may teach you, but as the same anointing teaches you concerning all, and is true, and is not a lie, and even as was taught you, you will remain in Him.
Koma za inu, kudzoza kumene munalandira kwa Khristu kuli mwa inu, ndipo sipafunika wina aliyense kuti akuphunzitseni. Koma kudzozako kumakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo popeza kudzoza kwakeko nʼkoona osati konama, monga munaphunzira, khalani mwa Iyeyo.
28 And now, little children, remain in Him, so that when He may have appeared, we may have boldness, and may not be ashamed before Him, at His coming;
Tsopano ana okondedwa, khalani mwa Yesu, kuti pamene adzaonekera, ife tidzakhale otsimikizika mu mtima ndi wopanda manyazi pamaso pake akamadzabwera.
29 if you know that He is righteous, know that everyone doing righteousness, has been begotten of Him.
Popeza mukudziwa kuti Khristu ndi wolungama, choncho mukudziwanso kuti aliyense amene amachita chilungamo ndi mwana wa Mulungu.