< 1 Corinthians 16 >
1 And concerning the collection that [is] for the holy ones, as I directed to the assemblies of Galatia, so also you—do;
Tsopano za zopereka zothandiza anthu a Ambuye a ku Yerusalemu. Muchite zomwe ndinawuza mipingo ya ku Galatiya kuti ichite.
2 on every first [day] of the week, let each one of you lay by him, treasuring up whatever he may have prospered, that when I may come then collections may not be made;
Pa tsiku loyamba la sabata lililonse, aliyense wa inu azipatula ndalama molingana ndi zomwe wapezera. Asunge, kuti ndikabwera pasadzakhalenso msonkhamsonkha.
3 and whenever I may come, whomsoever you may approve, through letters, these I will send to carry your favor to Jerusalem;
Pamenepo, ndikadzafika, ndidzawapatsa makalata a umboni anthu amene mudzawasankhe ndi kuwatuma kuti akapereka mphatso zanu ku Yerusalemu.
4 and if it be worthy for me also to go, with me they will go.
Ngati kutaoneka kuti nʼkoyenera kuti ndipite nawo, adzapita nane limodzi.
5 And I will come to you when I pass through Macedonia—for I pass through Macedonia—
Ndidzafika kwanuko nditadutsa ku Makedoniya pakuti ndikuyembekezera kudzera ku Makedoniyako.
6 and with you, it may be, I will abide, or even winter, that you may send me forward wherever I go,
Mwina ndidzakhala nanu kanthawi kochepa kapenanso nyengo yonse yozizira, kuti mudzandithandize kupitiriza ulendo wanga kulikonse kumene ndingapite.
7 for I do not wish to see you now in the passing, but I hope to remain a certain time with you, if the LORD may permit;
Sindikufuna kuti ndikuoneni tsopano mongodutsa chabe, koma ndikuyembekezera kudzakhala nanu kwa kanthawi, ngati Ambuye alola.
8 and I will remain in Ephesus until the Pentecost,
Koma ndikhala ndili ku Efeso mpaka nthawi ya Pentekosite,
9 for a door has been opened to me—great and effectual—and withstanders [are] many.
pakuti mwayi waukulu wapezeka woti nʼkugwira ntchito yaphindu, koma pali ambiri amene akutsutsana nane.
10 And if Timotheus may come, see that he may become without fear with you, for he works the work of the LORD, even as I,
Ngati Timoteyo afike kwanuko, onetsetsani kuti pasakhale zina zomuchititsa mantha pamene ali pakati panu, pakuti iye akugwira ntchito ya Ambuye monga ine.
11 no one, then, may despise him; and send him forward in peace, that he may come to me, for I expect him with the brothers;
Wina aliyense asamunyoze. Muthandizeni kupitiriza ulendo wake mwamtendere kubwereranso kuli ine. Ndikumuyembekeza pamodzi ndi abale ena.
12 and concerning Apollos our brother, I begged him much that he may come to you with the brothers, and it was not at all [his] will that he may come now, and he will come when he may find convenient.
Tsono kunena za mʼbale wathu, Apolo, ndinamuwumiriza kwambiri kuti abwere kwa inu abale, ndipo iye sanafune kupita tsopano. Koma akadzapeza mpata wabwino adzabwera.
13 Watch, stand in the faith; be men, be strong;
Khalani tcheru; khazikikani mʼchikhulupiriro chanu; limbani mtima; khalani amphamvu.
14 let all your things be done in love.
Chitani zonse mwachikondi.
15 And I beg you, brothers, you have known the household of Stephanas, that it is the first-fruit of Achaia, and they set themselves to the ministry to the holy ones—
Mukudziwa kuti a mʼbanja la Stefano ndiye anali oyamba kutembenuka mtima ku Akaya, ndipo akhala akudzipereka kutumikira oyera mtima. Choncho ndikukudandaulirani, inu abale,
16 that you also be subject to such, and to everyone who is working with [us] and laboring;
kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka.
17 and I rejoice over the coming of Stephanas, and Fortunatus, and Achaicus, because these filled up the lack of you;
Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane.
18 for they refreshed my spirit and yours; acknowledge, therefore, those who [are] such.
Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu womwe. Anthu a mtundu oterewa ngofunika kuwalemekeza.
19 The assemblies of Asia greet you; Aquilas and Priscilla greet you much in the LORD, with the assembly in their house;
Mpingo wa mʼchigawo cha ku Asiya ukupereka moni. Akula ndi Prisila akuperekanso moni wachisangalalo, mwa Ambuye, ndiponso mpingo umene umakumana mʼnyumba mwawo ukupereka moni.
20 all the brothers greet you; greet one another in a holy kiss.
Abale onse kuno akupereka moni wawo. Patsanani moni wachikondi chenicheni.
21 The salutation of [me], Paul, with my hand;
Ineyo Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa mawu awa akuti moni.
22 if anyone does not cherish the Lord Jesus Christ—let him be accursed! The LORD has come!
Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!
23 The grace of the Lord Jesus Christ [is] with you;
Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi inu.
24 my love [is] with you all in Christ Jesus! Amen.
Chikondi changa chikhale ndi nonsenu mwa Khristu Yesu.