< 1 Chronicles 25 >

1 And David and the heads of the host separate for service, of the sons of Asaph, and Heman, and Jeduthun, who are prophesying with harps, with psalteries, and with cymbals; and the number of the workmen is according to their service.
Davide ndi atsogoleri a asilikali anapatula ena mwa ana a Asafu, Hemani ndi Yedutuni ku utumiki wa uneneri pogwiritsa ntchito apangwe, azeze ndi ziwaya zamalipenga. Tsopano nawu mndandanda wa anthu amene ankagwira ntchito imeneyi:
2 Of sons of Asaph: Zaccur, and Joseph, and Nethaniah, and Asharelah; sons of Asaph [are] by the side of Asaph, who is prophesying by the side of the king.
Kuchokera kwa ana a Asafu: Zakuri, Yosefe, Netaniya ndi Asareli. Ana a Asafu amalamulidwa ndi Asafu ndipo amanenera moyangʼaniridwa ndi mfumu.
3 Of Jeduthun, sons of Jeduthun: Gedaliah, and Zeri, and Jeshaiah, [and Shimei, and] Hashabiah, and Mattithiah, six, by the side of their father Jeduthun; he is prophesying with a harp, for giving of thanks and of praise for YHWH.
Kwa Yedutuni, kuchokera kwa ana ake: Gedaliya, Zeri, Yesaya, Simei, Hasabiya ndi Matitiya. Onse analipo 9 ndipo amayangʼaniridwa ndi Yedutuni abambo awo, amene amanenera pogwiritsa ntchito apangwe poyamika ndi kutamanda Yehova.
4 Of Heman, sons of Heman: Bukkiah, Mattaniah, Uzziel, Shebuel, and Jerimoth, Hananiah, Hanani, Eliathah, Giddalti, and Romamti-Ezer, Joshbekashah, Mallothi, Hothir, Mahazioth;
Kwa Hemani, kuchokera kwa ana ake: Bukiya, Mataniya, Uzieli, Subaeli ndi Yerimoti; Hananiya, Hanani, Eliata, Gidaliti ndi Romamiti-Ezeri; Yosibakasa, Maloti, Hotiri ndi Mahazioti.
5 all these [are] sons of Heman, seer of the king in the things of God, to lift up a horn; and God gives fourteen sons and three daughters to Heman.
Onsewa anali ana a Hemani mlosi wa mfumu. Iye anapatsidwa anawa potsata mawu a Mulungu akuti adzamukweza. Mulungu anapatsa Hemani ana aamuna 14 ndi ana aakazi atatu.
6 All these [are] by the side of their father in the song of the house of YHWH, with cymbals, psalteries, and harps, for the service of the house of God; by the side of the king [are] Asaph, and Jeduthun, and Heman.
Anthu onsewa ankayangʼaniridwa ndi makolo awo pa mayimbidwe a mʼNyumba ya Yehova. Iwowatu ankayimba ndi ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe potumikira mʼNyumba ya Mulungu. Koma Asafu, Yedutuni ndi Hemani amayangʼaniridwa ndi mfumu.
7 And their number, with their brothers taught in the song of YHWH—all who are intelligent—[is] two hundred and eighty-eight.
Iwo pamodzi ndi abale awo onse ophunzitsidwa ndi aluso loyimbira Yehova chiwerengero chawo chinali 288.
8 And they cause lots to fall, charge next to [charge], the small as well as the great, the intelligent with the learner.
Angʼonoangʼono ndi akulu omwe, mphunzitsi ndi wophunzira yemwe anachita maere pa ntchito zawo.
9 And the first lot goes out for Asaph to Joseph; the second, Gedaliah—him, and his brothers and his sons—twelve;
Maere woyamba amene anali a Asafu, anagwera Yosefe, ana ndi abale ake. 12 Maere achiwiri anagwera Gedaliya, ndi abale ake ndi ana ake. 12
10 the third, Zaccur, his sons and his brothers—twelve;
Maere achitatu anagwera Zakuri, ana ake ndi abale ake. 12
11 the fourth to Izri, his sons and his brothers—twelve;
Maere achinayi anagwera Iziri, ana ake ndi abale ake. 12
12 the fifth, Nethaniah, his sons and his brothers—twelve;
Maere achisanu anagwera Netaniya, ana ake ndi abale ake. 12
13 the sixth, Bukkiah, his sons and his brothers—twelve;
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera Bukiya, ana ake ndi abale ake. 12
14 the seventh, Jesharelah, his sons and his brothers—twelve;
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera Yesarela, ana ake ndi abale ake. 12
15 the eighth, Jeshaiah, his sons and his brothers—twelve;
Maere achisanu ndi chitatu anagwera Yeshaya, ana ake ndi abale ake. 12
16 the ninth, Mattaniah, his sons and his brothers—twelve;
Maere achisanu ndi chinayi anagwera Mataniya, ana ake ndi abale ake. 12
17 the tenth, Shimei, his sons and his brothers—twelve:
Maere a khumi anagwera Simei, ana ake ndi abale ake. 12
18 eleventh, Azareel, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 11 anagwera Azareli, ana ake ndi abale ake. 12
19 the twelfth to Hashabiah, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 12 anagwera Hasabiya, ana ake ndi abale ake. 12
20 for the thirteenth, Shubael, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 13 anagwera Subaeli, ana ake ndi abale ake. 12
21 for the fourteenth, Mattithiah, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 14 anagwera Matitiya, ana ake ndi abale ake. 12
22 for the fifteenth to Jeremoth, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 15 anagwera Yeremoti, ana ake ndi abale ake. 12
23 the sixteenth to Hananiah, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 16 anagwera Hananiya, ana ake ndi abale ake. 12
24 the seventeenth to Joshbekashah, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 17 anagwera Yosibakasa, ana ake ndi abale ake. 12
25 the eighteenth to Hanani, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 18 anagwera Hanani, ana ake ndi abale ake. 12
26 the nineteenth to Mallothi, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 19 anagwera Maloti, ana ake ndi abale ake. 12
27 the twentieth to Eliathah, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 20 anagwera Eliyata, ana ake ndi abale ake. 12
28 the twenty-first to Hothir, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 21 anagwera Hotiri, ana ake ndi abale ake. 12
29 the twenty-second to Giddalti, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 22 anagwera Gidaliti, ana ake ndi abale ake. 12
30 the twenty-third to Mahazioth, his sons and his brothers—twelve;
Maere a 23 anagwera Mahazioti, ana ake ndi abale ake. 12
31 the twenty-fourth to Romamti-Ezer, his sons and his brothers—twelve.
Maere a 24 anagwera Romamiti-Ezeri, ana ake ndi abale ake 12.

< 1 Chronicles 25 >