< 1 Chronicles 2 >

1 These [are] sons of Israel: Reuben, Simeon, Levi, and Judah, Issachar, and Zebulun,
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 Dan, Joseph, and Benjamin, Naphtali, Gad, and Asher.
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 Sons of Judah: Er, and Onan, and Shelah, three have been born to him of a daughter of Shua the Canaanitess. And Er, firstborn of Judah, is evil in the eyes of YHWH, and He puts him to death.
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 And his daughter-in-law Tamar has borne Perez and Zerah to him. All the sons of Judah [are] five.
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
5 Sons of Perez: Hezron, and Hamul.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 And sons of Zerah: Zimri, and Ethan, and Heman, and Calcol, and Dara; all of them five.
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 And sons of Carmi: Achar, troubler of Israel, who trespassed in the devoted thing.
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
8 And sons of Ethan: Azariah.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 And sons of Hezron who were born to him: Jerahmeel, and Ram, and Chelubai.
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 And Ram begot Amminadab, and Amminadab begot Nahshon, prince of the sons of Judah;
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
11 and Nahshon begot Salma, and Salma begot Boaz,
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 and Boaz begot Obed, and Obed begot Jesse;
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 and Jesse begot his firstborn Eliab, and Abinadab the second, and Shimea the third,
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
14 Nethaneel the fourth, Raddai the fifth,
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
15 Ozem the sixth, David the seventh,
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 and their sisters Zeruiah and Abigail. And sons of Zeruiah: Abishai, and Joab, and Asah-El—three.
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 And Abigail has borne Amasa, and the father of Amasa [is] Jether the Ishmaelite.
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 And Caleb son of Hezron has begotten Azubah, Isshah, and Jerioth; and these [are] her sons: Jesher, and Shobab, and Ardon.
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 And Azubah dies, and Caleb takes Ephrath to himself, and she bears Hur to him.
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
20 And Hur begot Uri, and Uri begot Bezaleel.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 And afterward Hezron has gone in to a daughter of Machir father of Gilead, and he has taken her, and he [is] a son of sixty years, and she bears Segub to him.
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 And Segub begot Jair, and he has twenty-three cities in the land of Gilead,
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 and he takes Geshur and Aram, the small villages of Jair, from them, with Kenath and its small towns, sixty cities—all these [belonged to] the sons of Machir father of Gilead.
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 And after the death of Hezron in Caleb-Ephratah, then the wife of Hezron, Abijah, even bears to him Asshur, father of Tekoa.
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 And sons of Jerahmeel, firstborn of Hezron, are: the firstborn Ram, and Bunah, and Oren, and Ozem, Ahijah.
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 And Jerahmeel has another wife, and her name [is] Atarah, she [is] mother of Onam.
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 And sons of Ram, firstborn of Jerahmeel, are Maaz, and Jamin, and Eker.
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 And sons of Onam are Shammai and Jada. And sons of Shammai: Nadab and Abishur.
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 And the name of the wife of Abishur [is] Abihail, and she bears Ahban and Molid to him.
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 And sons of Nadab: Seled and Appaim; and Seled dies without sons.
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 And sons of Appaim: Ishi. And sons of Ishi: Sheshan. And sons of Sheshan: Ahlai.
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 And sons of Jada, brother of Shammai: Jether and Jonathan; and Jether dies without sons.
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 And sons of Jonathan: Peleth and Zaza. These were sons of Jerahmeel.
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 And Sheshan had no sons, but daughters, and Sheshan has a servant, an Egyptian, and his name [is] Jarha,
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 and Sheshan gives his daughter to his servant Jarha for a wife, and she bears Attai to him;
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
36 and Attai begot Nathan, and Nathan begot Zabad,
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 and Zabad begot Ephlal, and Ephlal begot Obed,
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 and Obed begot Jehu,
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 and Jehu begot Azariah, and Azariah begot Helez, and Helez begot Eleasah,
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 and Eleasah begot Sismai, and Sismai begot Shallum,
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 and Shallum begot Jekamiah, and Jekamiah begot Elishama.
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 And sons of Caleb brother of Jerahmeel: Mesha his firstborn, he [is] father of Ziph; and sons of Mareshah: Abi-Hebron.
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 And sons of Hebron: Korah, and Tappuah, and Rekem, and Shema.
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 And Shema begot Raham father of Jorkoam, and Rekem begot Shammai.
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 And a son of Shammai [is] Maon, and Maon [is] father of Beth-Zur.
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 And Ephah concubine of Caleb bore Haran, and Moza, and Gazez; and Haran begot Gazez.
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 And sons of Jahdai: Regem, and Jotham, and Geshem, and Pelet, and Ephah, and Shaaph.
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 The concubine of Caleb, Maachah, bore Sheber and Tirhanah;
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 and she bears Shaaph father of Madmannah, Sheva father of Machbenah, and father of Gibea; and a daughter of Caleb [is] Achsa.
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 These were sons of Caleb son of Hur, firstborn of Ephrathah: Shobal father of Kirjath-Jearim,
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 Salma father of Beth-Lehem, Hareph father of Beth-Gader.
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 And there are sons to Shobal father of Kirjath-Jearim: Haroeh, half of the Menuhothite;
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 and the families of Kirjath-Jearim: the Ithrite, and the Puhite, and the Shumathite, and the Mishraite. The Zorathite and the Eshtaolite went out from these.
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 Sons of Salma: Beth-Lehem, and the Netophathite, Atroth, Beth-Joab, and half of the Menuhothite, the Zorite;
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 and the families of the scribes, the inhabitants of Jabez: Tirathites, Shimeathites, Suchathites. They [are] the Kenites, those coming of Hammath father of the house of Rechab.
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.

< 1 Chronicles 2 >