< 1 Chronicles 10 >
1 And the Philistines have fought with Israel, and the men of Israel flee from the face of the Philistines, and fall wounded in Mount Gilboa,
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 and the Philistines pursue after Saul, and after his sons, and the Philistines strike Jonathan, and Abinadab, and Malchi-Shua, sons of Saul.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 And the battle [is] heavy on Saul, and those shooting with the bow find him, and he is wounded by those shooting,
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza.
4 and Saul says to the bearer of his weapons, “Draw your sword and pierce me with it, lest these uncircumcised come and have abused me.” And the bearer of his weapons has not been willing, for he fears exceedingly, and Saul takes the sword, and falls on it;
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe, kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere ndi kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 and the bearer of his weapons sees that Saul [is] dead, and falls, he also, on the sword, and dies;
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa.
6 and Saul dies, and his three sons, and all his house—they died together.
Motero Sauli ndi ana ake atatu anafa, pamodzi ndi banja lake lonse anafera limodzi.
7 And all the men of Israel who [are] in the valley see that they have fled and that Saul and his sons have died, and they forsake their cities and flee, and the Philistines come and dwell in them.
Pamene Aisraeli onse amene anali mʼchigwa anaona kuti gulu lankhondo lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 And it comes to pass, on the next day, that the Philistines come to strip the wounded, and find Saul and his sons fallen in Mount Gilboa,
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa, anapeza Sauli ndi ana ake atafa pa phiri la Gilibowa.
9 and strip him, and carry away his head and his weapons, and send [them] into the land of the surrounding Philistines to proclaim tidings [to] their idols and the people;
Iwo anamuvula zovala zake, natenga mutu wake ndi zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 and they put his weapons in the house of their gods, and have fixed his skull in the house of Dagon.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba zopembedzera milungu yawo ndipo anapachika mutu wake mʼnyumba ya Dagoni.
11 And all Jabesh-Gilead hears of all that the Philistines have done to Saul,
Pamene anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 and all the men of valor rise and carry away the body of Saul, and the bodies of his sons, and bring them to Jabesh, and bury their bones under the oak in Jabesh, and fast seven days.
anthu awo onse olimba mtima anapita kukatenga mitembo ya Sauli ndi ana ake ndipo anabwera nayo ku Yabesi. Anakwirira mafupa awo pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
13 And Saul dies because of his trespass that he trespassed against YHWH, against the word of YHWH that he did not keep, and also for asking to inquire of a familiar spirit;
Sauli anafa chifukwa anali wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanasunge mawu a Yehova, pakuti anakafunsira nzeru kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa,
14 and he did not inquire of YHWH, and He puts him to death, and turns around the kingdom to David son of Jesse.
sanafunsire nzeruzo kwa Yehova. Choncho Yehova anamupha ndi kupereka ufumu kwa Davide mwana wa Yese.