< Song of Solomon 4 >

1 Behold, thou art beautiful, my beloved, behold, thou art beautiful: thy dovelike eyes [look forth] from behind thy vail; thy hair is like a flock of goats, that come quietly down from Mount Gil'ad.
Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga! Ndithudi, ndiwe wokongola! Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
2 Thy teeth are like a flock of well-selected sheep, which are come up from the washing, all of which bear twins, and there is not one among them that is deprived of her young.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene, zochokera kozisambitsa kumene. Iliyonse ili ndi ana amapasa; palibe imene ili yokha.
3 Like a thread of scarlet are thy lips, and thy mouth is comely: like the half of a pomegranate is the upper part of thy cheek behind thy vail.
Milomo yako ili ngati mbota yofiira; pakamwa pako ndi pokongola kwambiri. Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
4 Thy neck is like the tower of David built on terraces, a thousand shields hang-thereon, all the quivers of the mighty men.
Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide, yomangidwa bwino ndi yosalala; pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000, zishango zonsezo za anthu ankhondo.
5 Thy two breasts are like two fawns, the twins of the roe, that feed among the lilies.
Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala, ngati ana amapasa a nswala amene akudya pakati pa maluwa okongola.
6 Until the day became cool, and the shadows flee away, will I get me to the mountain of myrrh, and to the hill of frankincense.
Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira ndipo mithunzi ikayamba kuthawa, ndidzapita ku phiri la mure ndi ku chitunda cha lubani.
7 Thou art altogether beautiful, my beloved, and there is no blemish on thee.—
Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga; palibe chilema pa iwe.
8 Come with me from Lebanon, O bride, with me from Lebanon: look about from the top of Amanah, from the top of Senir and Chermon, from the lions' dens, from the leopards' mountains.
Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga, tiye tichoke ku Lebanoni, utsikepo pa msonga ya Amana, kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni, kuchoka ku mapanga a mikango ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
9 Thou hast ravished my heart, O my sister, [my] bride; thou hast ravished my heart with one of thy eyes, with one chain of thy neck.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima, iwe wanditenga mtima ndi kapenyedwe ka maso ako, ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
10 How beautiful are thy caresses, O my sister, [my] bride! how much more pleasant are thy caresses than wine! and the smell of thy fragrant oils more than all spices.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa! Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo, ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
11 Of sweet honey drop thy lips, O bride: honey and milk are under thy tongue; and the scent of thy garments is like the scent of Lebanon.
Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi; pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi. Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
12 A locked-up garden is my sister, [my] bride; a locked-up spring, a sealed fountain.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa; ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
13 Thy sprouts are an orchard of pomegranates, with precious fruits, copher and spikenard;
Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza; muli zipatso zokoma kwambiri, muli hena ndi nadi,
14 Spikenard and saffron; calamus and cinnamon, with all the trees of frankincense; myrrh and aloes, with all the chief of spices;
nadi ndi safiro, kalamusi ndi sinamoni, komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino. Mulinso mure ndi aloe ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
15 A garden-spring, a well of living waters, and flowing down from Lebanon.—
Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda, chitsime cha madzi oyenda, mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
16 Awake, O north wind; and come thou, O south; blow over my garden, that its spices may flow out. Let my friend come into his garden, and eat its precious fruits.—
Dzuka, iwe mphepo yakumpoto, ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera! Uzira pa munda wanga, kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse. Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.

< Song of Solomon 4 >