< Ruth 3 >

1 Then said Na'omi her mother-in-law unto her, My daughter, behold I will seek for thee a resting-place, where it may be well with thee.
Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
2 And now, behold, Bo'az is our kinsman, he with whose maidens thou hast been. Lo, he is winnowing the barley to-night in the threshing-floor.
Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
3 Therefore bathe, and anoint thyself, and put thy garments upon thee, and go down to the threshing-floor; [but] make thyself not known unto the man, until he shall have finished eating and drinking.
Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
4 And it shall be, when he lieth down, that thou shalt note the place where he will lie, and thou shalt then go in, and lift up the covering that is on his feet, and lay thyself down: and he will tell thee what thou shalt do.
Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
5 And she said unto her, All that thou sayest unto me will I do.
Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
6 And she went down unto the threshing-floor, and did in accordance with all that her mother-in-law had commanded her.
Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
7 And Bo'az ate and drank, and his heart became merry; and he then went in to lie down at the end of the heap of corn: and she came in softly, and lifted up the covering that was on his feet, and laid herself down.
Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
8 And it came to pass at midnight, that the man became terrified, and bent himself forward; and, behold, a woman was lying at his feet.
Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
9 And he said, Who art thou? And she said, I am Ruth thy handmaid: spread therefore thy skirt over thy handmaid; for thou art a near kinsman.
Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
10 And he said, Blessed be thou unto the Lord, my daughter; for thou hast shown more kindness in the last instance than the first, by not going after the young men, whether they be poor or rich.
Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
11 And now, my daughter, fear not: all that thou mayest say will I do for thee; for all [the men in] the gate of my people know that thou art a virtuous woman.
Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
12 And now, it is indeed true that I am thy near kinsman; nevertheless, there is a kinsman nearer than I.
Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
13 Remain here this night, and it shall be in the morning, that if he will redeem thee, well, let him redeem; but if he be not willing to redeem thee, then will I redeem thee, as the Lord liveth: lie still until the morning.
Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
14 And she lay at his feet until the morning; and she rose up before one could know another. And he said, It must not be known that this woman came into the threshing-floor.
Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
15 Also he said, Bring hither the cloak that thou hast upon thee, and lay hold of it. And she laid hold of it, and he measured six [measures] of barley, and laid it on her, and went into the city.
Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
16 And she came to her mother-in-law, and she said, How is it with thee, my daughter? And she told her all that the man had done to her.
Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
17 And she said, These six measures of barley gave he unto me; for he said to me, Thou shalt not come empty to thy mother-in-law.
Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
18 Then said she, Remain still, my daughter, until thou know how the matter will fall out; for the man will not rest, until he have finished the matter this day.
Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”

< Ruth 3 >